< Josué 23 >

1 Et bien des jours s'étaient écoulés après que le Seigneur avait donné le repos à Israël; les ennemis qui l'entouraient étaient désarmés. Josué était vieux, et avait vécu bien des jours.
Panapita nthawi yayitali kuchokera pamene Yehova anakhazikitsa mtendere pakati pa Aisraeli ndi adani awo owazungulira. Nthawi imeneyi nʼkuti Yoswa atakalamba, ali ndi zaka zambiri.
2 Et Josué convoqua tous les fils d'Israël, leurs anciens, leurs chefs, leurs juges, leurs scribes, et il leur dit: Je suis vieux, j'ai vécu bien des jours,
Yoswayo anayitanitsa Aisraeli onse pamodzi ndi akuluakulu, atsogoleri, oweruza, ndi oyangʼanira anthu antchito ndipo anawawuza kuti, “Ine ndakalamba ndipo ndili ndi zaka zambiri.
3 Et vous avez vu comment le Seigneur notre Dieu a traité toutes ces nations devant vous, parce que le Seigneur lui-même a combattu pour vous.
Inu mwaona zonse zimene Yehova Mulungu wanu wachita kwa mitundu yonseyi chifukwa cha inu. Ndi Yehova Mulungu wanu amene anakumenyerani nkhondo.
4 Vous voyez que je vous ai soumis ce qui reste de toutes ces nations parmi vous, sur les territoires de vos tribus; je les ai exterminées entre le Jourdain et la grande mer qui sera votre limite à l'occident.
Tsono onani! Mitundu ya anthu otsalawa ndayipereka kwa mafuko anu pamodzi ndi mitundu ya anthu ya pakati pa Yorodani ndi Nyanja Yayikulu ya kumadzulo imene ndinayigonjetsa.
5 Le Seigneur votre Dieu lui-même continuera de les exterminer devant vous, jusqu'à ce qu'elles soient toutes détruites; il enverra contre elles des bêtes farouches, tant qu'il ne les aura pas exterminées devant vous, elles et leurs rois; vous hériterez de leurs terres, comme l'a dit le Seigneur notre Dieu.
Yehova Mulungu wanu ndiye adzawathamangitsa pamaso panu. Mudzatenga dziko lawo monga Yehova anakulonjezerani.
6 Efforcez-vous donc avec zèle de garder et de pratiquer tout ce qui est écrit au livre de la loi de Moïse, afin de ne vous en écarter ni à droite ni à gauche;
“Choncho khalani amphamvu, ndipo samalani kuti mumvere zonse zimene zalembedwa mʼbuku la malamulo a Mose. Musapatuke pa malamulo onse amene alembedwamo.
7 Afin de ne vous point mêler à ces nations qui existent encore. Que le nom de leurs dieux ne soit jamais prononcé parmi vous; gardez-vous de les servir ou de les adorer.
Musagwirizane ndi mitundu ya anthu imene yatsala pakati panu. Musatchule mayina a milungu yawo kapena kuyitchula polumbira. Musayitumikire kapena kuyigwadira.
8 Mais restez fortement attachés au Seigneur notre Dieu, comme vous l'avez été jusqu'à ce jour.
Koma mukuyenera kugwiritsa Yehova Mulungu wanu, monga mwachitira mpaka lero lino.
9 Et le Seigneur exterminera, devant votre face, ces nations grandes et puissantes; nulle, jusqu'à ce jour, n'a tenu devant vous.
“Yehova wapirikitsa patsogolo panu mitundu ya anthu ikuluikulu ndi yolimba. Mpaka lero palibe amene watha kulimbana nanu.
10 Un seul de vous a mis en fuite mille hommes, parce que le Seigneur notre Dieu lui-même a combattu pour vous, comme il vous l'a dit.
Aliyense wa inu atha kuthamangitsa anthu 1,000 chifukwa Yehova Mulungu wanu ndiye amakumenyerani nkhondo, monga momwe analonjezera.
11 Et vous veillerez diligemment à aimer le Seigneur votre Dieu.
Choncho samalitsani kuti mukonde Yehova Mulungu wanu.
12 Car, si vous vous détournez de lui, si vous vous joignez aux nations qui sont restées parmi vous, si vous contractez chez elles des mariages, si vous vous mêlez à elles et elles à vous,
“Koma ngati mubwerera mʼmbuyo ndi kuphatikizana ndi mitundu yotsalayi imene ili pakati panu ndi kumakwatirana nayo,
13 Vous reconnaîtrez que le Seigneur ne continuera plus d'exterminer ces nations devant votre face. Et pour vous, elles seront des filets, des pièges, des clous sous vos pieds, et des flèches dans vos yeux, jusqu'à ce que vous soyez effacés de cette terre fortunée que vous a donnée le Seigneur notre Dieu.
pamenepo mudziwe kuti Yehova, Mulungu wanu, sadzapirikitsa mitundu imeneyi pamaso panu, koma idzakhala ngati msampha kwa inu kapenanso khwekhwe lokukolani. Idzakhala ngati zikwapu pa msana panu kapenanso ngati minga mʼmaso mwanu mpaka mutatha psiti mʼdziko labwinoli limene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.
14 Pour moi, je m'en vais à grands pas sur le chemin de la vie, comme font ceux qui sont sur la terre. Et vous, vous reconnaîtrez, en vos cœurs et en vos âmes, que nulle parole n'est tombée à terre de toutes celles qu'a prononcées le Seigneur notre Dieu sur tout ce qui vous concernait, et qu'il n'en a laissé aucune en arrière.
“Aliyense wa inu akudziwa mu mtima mwake komanso mʼmoyo mwake kuti zabwino zonse zimene Yehova Mulungu wanu anakulonjezani zachitika. Palibe lonjezo ndi limodzi lomwe limene silinakwaniritsidwe.
15 Or, de même que toutes les bonnes paroles du Seigneur se sont accomplies pour vous, de même le Seigneur sera fidèle à toutes ses menaces, jusqu'à ce qu'il vous ait effacés de cette terre fortunée que vous a donnée le Seigneur,
Monga momwe Yehova Mulungu wanu wakuchitirani zabwino zonse zimene ananena kuti adzachita, Yehovayo angathenso kukuchitirani zoyipa zonse zimene waopseza, mpaka kukuchotsani mʼdziko lokoma limene anakupatsani.
16 Si vous violez l'alliance du Seigneur notre Dieu que lui-même vous a donnée pour loi, si vous vous en allez servir d'autres dieux et les adorer.
Ngati muphwanya pangano la Yehova Mulungu wanu, limene anakulamulirani nʼkumapita kukatumikira milungu ina ndi kuyigwadira, Yehova adzakukwiyirani, ndiye mudzachotsedwa mʼdziko labwinoli limene Yehova wakupatsani.”

< Josué 23 >