< Jonas 2 >

1 Et Jonas pria le Seigneur son Dieu, dans le ventre de la baleine.
Yona ali mʼmimba mwa chinsomba chija anapemphera kwa Yehova Mulungu wake.
2 Et il dit: J'ai crié dans ma tribulation au Seigneur mon Dieu, et Il m'a exaucé; mon cri est parti des entrailles de l'enfer, et Tu as écouté ma voix; (Sheol h7585)
Iye anati: “Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova, ndipo Iye anandiyankha. Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo, ndipo Inu munamva kulira kwanga. (Sheol h7585)
3 Tu m'as précipité au plus profond du cœur de la mer; et les fleuves m'ont enveloppé, et toutes tes grandes vagues, tous Tes flots ont passé sur moi.
Munandiponya mʼnyanja yozama, mʼkati mwenimweni mwa nyanja, ndipo madzi oyenda anandizungulira; mafunde anu onse ndi mkokomo wake zinandimiza.
4 Et j'ai dit: C'est moi qui me suis éloigné de Tes yeux; me permettras-Tu de voir encore Ton saint temple?
Ndinati, ‘Ine ndachotsedwa pamaso panu; komabe ndidzayangʼananso ku Nyumba yanu yopatulika.’
5 L'eau s'est répandue autour de moi, jusqu'à l'âme; l'abîme le plus profond m'a enclos, et ma tête a plongé
Madzi wondimiza anandichititsa mantha, nyanja yozama inandizungulira; udzu wa mʼmadzi zinakuta mutu wanga.
6 jusqu'aux racines des monts; je suis descendu sous la terre, dont les verrous sont des barrières éternelles. Seigneur mon Dieu, que la destruction de ma vie remonte à la surface des flots.
Ndinatsikira kunsi ndithu, mʼtsinde mwa mapiri; mipiringidzo ya dziko inanditsekereza kosatha. Koma Inu munatulutsa moyo wanga mʼmandamo, Inu Yehova Mulungu wanga.
7 En la défaillance de mon âme, je me suis souvenu de Toi, Seigneur; que ma prière arrive à Toi dans Ton saint temple!
“Pamene moyo wanga umachoka mwa ine, ine ndinakumbukira Inu Yehova, ndipo pemphero langa linafika kwa inu, ku Nyumba yanu yopatulika.
8 Ceux-là seuls qui s'attachent aux vanités et aux mensonges ont renoncé à Ta miséricorde.
“Iwo amene amagwiritsitsa mafano achabechabe amataya chisomo chawo.
9 Pour moi, je T'offrirai dans mes chants un sacrifice de louanges et d'admiration; je rendrai au Seigneur les vœux que je Lui ai faits pour mon salut.
Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe ndikuyimba nyimbo yamayamiko. Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa. Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”
10 Et le Seigneur donna ordre à la baleine, et elle rejeta Jonas sur la terre ferme.
Ndipo Yehova analamula chinsomba chija, ndipo chinakamusanza Yonayo mʼmbali mwa nyanja.

< Jonas 2 >