< Jonas 1 >

1 Et la parole du Seigneur vint à Jonas, fils d'Amathi, disant
Yehova anayankhula ndi Yona mwana wa Amitai kuti,
2 Lève-toi, et pars pour Ninive, la grande ville, et proclame dans ses murs que le cri de sa méchanceté est monté jusqu'à Moi.
“Nyamuka, pita ku mzinda waukulu wa Ninive ndipo ukalalikire motsutsana nawo, chifukwa zoyipa zawo zafika pamaso panga.”
3 Et Jonas se leva pour s'enfuir à Tharsis, loin de la face du Seigneur; et il descendit à Joppé; il y trouva une barque allant à Tharsis, et il paya son passage, et il s'embarqua pour naviguer avec les matelots, jusqu'à Tharsis, loin de la face du Seigneur.
Koma Yona anathawa Yehova ndi kulowera ku Tarisisi. Anapita ku Yopa, kumene anapeza sitima yapamadzi yopita ku Tarisisi. Atagula chiphaso, anakwera sitimayo kupita ku Tarisisi kuthawa Yehova.
4 Et le Seigneur excita un grand vent sur la mer, et les vagues s'élevèrent, et la barque fut en danger de se rompre.
Koma Yehova anatumiza chimphepo champhamvu pa nyanja, ndipo panauka namondwe wamphamvu amene anafuna kuphwanya sitimayo.
5 Et les matelots eurent crainte, et ils crièrent chacun vers son dieu, et ils lancèrent à la mer le chargement de la barque, pour s'en alléger. Jonas descendit à fond de cale, et là il s'endormit, et il ronfla.
Onse oyendetsa sitimayo anachita mantha ndipo aliyense anayamba kupemphera kwa mulungu wake. Ndipo anaponya katundu mʼnyanja kuti sitimayo ipepuke. Koma Yona pa nthawiyi nʼkuti atatsikira mʼkatikati mwa sitimayo kumene anagona tulo tofa nato.
6 Et le pilote l'alla trouver, et il lui dit: Pourquoi ronfles-tu? Lève- toi, et invoque ton Dieu, afin que Dieu nous sauve, et que nous ne mourions pas.
Mkulu wa oyendetsa sitimayo anapita kwa iye ndipo anati, “Kodi iwe, nʼchifukwa chiyani ukugona? Dzuka pemphera kwa mulungu wako! Mwina adzatithandiza, ndipo sitidzawonongeka.”
7 Et chacun des matelots dit à son voisin: Allons, agitons les sorts, et sachons par qui ce malheur nous arrive. Et ils agitèrent des sorts, et le sort tomba sur Jonas.
Ndipo oyendetsa sitimayo anayamba kuwuzana kuti, “Bwerani, tichite maere kuti tipeze amene wabweretsa tsoka limeneli.” Iwo anachita maerewo ndipo anagwera Yona.
8 Et ils lui dirent: Déclare-nous quel est ton métier; d'où viens-tu? de quelle contrée, de quel peuple es-tu?
Tsono anamufunsa kuti, “Tatiwuze, tsoka limeneli latigwera chifukwa chiyani? Umagwira ntchito yanji? Ukuchokera kuti? Kwanu nʼkuti? Ndiwe mtundu wanji wa anthu?”
9 Et il leur dit: Je suis un serviteur du Seigneur; j'adore le Seigneur Dieu du ciel, qui a créé la mer et la terre.
Iye anayankha kuti, “Ndine Mhebri, ndipo ndimapembedza Yehova, Mulungu Wakumwamba, amene analenga nyanja ndi mtunda.”
10 Et ces hommes eurent grande crainte, et ils lui dirent: Pourquoi as-tu fait cela? Car ces hommes connurent qu'il fuyait loin de la face du Seigneur; car il le leur avait déclaré.
Izi zinawachititsa mantha kwambiri ndipo anafunsa kuti, “Kodi wachita chiyani?” (Iwo ankadziwa kuti iyeyo amathawa Yehova, chifukwa nʼkuti atawawuza kale).
11 Et ils lui dirent: Que te ferons-nous, afin que pour nous la mer se calme? Car la mer allait, et soulevait encore plus de vagues.
Namondwe ananka nakulirakulirabe pa nyanjapo. Tsono anamufunsa iye kuti, “Kodi tikuchite chiyani kuti nyanjayi ikhale bata?”
12 Et Jonas leur dit: Prenez-moi et jetez-moi à la mer, et la mer se calmera pour vous; car je sais que c'est à cause de moi qu'il y a contre vous ces grandes vagues.
Iye anayankha kuti, “Nyamuleni ndi kundiponya mʼnyanjamu ndipo nyanjayi ikhala bata. Ndikudziwa kuti wolakwa ndine nʼchifukwa chake chimphepo champhamvuchi chabwera pa inu.”
13 Et ces hommes s'efforcèrent de retourner à la côte; mais ils ne le purent, parce que la mer allait et soulevait contre eux toujours plus de vagues.
Komabe oyendetsa sitimayo anayesetsa kupalasa kwambiri kuti abwerere ku mtunda koma analephera ndithu poti nyanja inawinduka kwambiri kuposa poyamba paja
14 Et ils crièrent au Seigneur, et ils dirent: Non, Seigneur, que nous ne périssions pas pour la vie de cet homme; ne fais pas retomber sur nous un sang innocent; car, Seigneur, Tu as fait selon Ta volonté.
Pamenepo iwo anafuwulira kwa Yehova nati, “Inu Yehova, musalole kuti ife tife chifukwa cha moyo wa munthu uyu. Musatizenge mlandu wa kupha munthu wosalakwa, pakuti ife tachita monga mwakufuna kwanu, Inu Yehova.”
15 Et ils prirent Jonas, et ils le lancèrent à la mer; et la mer cessa de s'agiter.
Ndipo anatenga Yona namuponya mʼnyanja, ndipo nyanja yowindukayo inakhala bata.
16 Et ces hommes eurent grande crainte du Seigneur; et ils offrirent au Seigneur un sacrifice, et ils Lui firent des vœux.
Anthuwo ataona zimenezi anachita mantha akulu ndi Yehova, ndipo anapereka nsembe kwa Yehova nalumbira kuti adzatumikira Yehovayo.
17 Et le Seigneur prescrivit à une grande baleine d'avaler Jonas, et Jonas fut dans le ventre de la baleine trois jours et trois nuits.
Koma Yehova anatuma nsomba yayikulu kuti imeze Yona. Motero Yona anakhala mʼmimba mwa nsombayo masiku atatu, usana ndi usiku.

< Jonas 1 >