< Joël 1 >
1 Parole du Seigneur qui vint à Joël, fils de Bathuel.
Yehova anayankhula ndi Yoweli mwana wa Petueli.
2 Écoutez ce que je vais dire, vieillards; prêtez l'oreille, vous tous qui habitez la terre: Est-il rien arrivé de pareil, soit de nos jours, soit du temps de nos pères?
Inu akuluakulu, imvani izi; mvetserani, nonse amene mumakhala mʼdziko. Kodi zinthu zokhala ngati izi zinayamba zaonekapo mʼnthawi yanu, kapena mʼnthawi ya makolo anu?
3 Plus que vos pères, vous aurez à raconter à vos enfants, et plus encore vos enfants à leurs enfants, et ceux-ci plus encore à la génération suivante.
Muwafotokozere ana anu, ndipo ana anuwo afotokozere ana awo, ndipo ana awo adzafotokozere mʼbado winawo.
4 La sauterelle a dévoré ce qu'avait laissé la chenille; la grosse sauterelle a dévoré ce qu'avait laissé la sauterelle; la nielle a dévoré ce qu'avait laissé la grosse sauterelle.
Chimene dzombe losamera mapiko lasiya dzombe lowuluka ladya; chimene dzombe lowuluka lasiya dzombe lalingʼono ladya; chimene dzombe lalingʼono lasiya chilimamine wadya.
5 Réveillez-vous, ô vous qui vous enivrez de votre vin, et pleurez. Lamentez- vous, ô vous qui buvez du vin jusqu'à l'ivresse; car la gaieté et la joie sont ôtées de vos lèvres.
Dzukani, inu zidakwa ndipo mulire! Lirani mofuwula, inu nonse amene mumamwa vinyo; lirani mofuwula chifukwa cha vinyo watsopano, pakuti wachotsedwa pakamwa panu.
6 Une nation puissante et innombrable est montée sur ma terre; ses dents sont des dents de lion, et ses mâchoires des mâchoires de lionceaux.
Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa, wamphamvu ndi wosawerengeka; uli ndi mano a mkango, zibwano za mkango waukazi.
7 Elle a rasé ma vigne, elle a brisé mon figuier, elle a cherché ma vigne et l'a tout arrachée; elle a pelé les rameaux de mon figuier.
Wawononga mphesa zanga ndipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu. Wakungunula makungwa ake ndi kuwataya, kusiya nthambi zake zili mbee.
8 Pleurez avec moi, plus que la jeune femme ceinte d'un cilice ne pleure l'époux de sa virginité.
Lirani ngati namwali wovala chiguduli, chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.
9 La victime et les libations ont été enlevées du temple du Seigneur; pleurez, prêtres, qui serviez l'autel du Seigneur;
Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova. Ansembe akulira, amene amatumikira pamaso pa Yehova.
10 car les champs sont désolés. Que la terre soit en deuil, car le blé manque, les sources du vin sont desséchées, l'olivier est stérile,
Minda yaguga, nthaka yauma; tirigu wawonongeka, vinyo watsopano watha, mitengo ya mafuta yauma.
11 les laboureurs sont épuisés. Pleurez vos richesses, votre froment, votre orge; car dans les champs la récolte a péri.
Khalani ndi nkhawa, inu alimi, lirani mofuwula inu alimi a mphesa; imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele, pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.
12 La vigne a été desséchée, les figuiers ont perdu leur fertilité; le grenadier, le palmier, le pommier, tous les arbres fruitiers de la campagne sont morts, parce que les fils des hommes sont confondus dans leur joie.
Mpesa wauma ndipo mtengo wamkuyu wafota; makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi, mitengo yonse ya mʼmunda yauma. Ndithudi chimwemwe cha anthu chatheratu.
13 Prêtres, ceignez-vous, frappez-vous la poitrine; pleurez, vous qui servez à l'autel. Entrez et dormez avec vos cilices, ministres de Dieu, parce que les victimes et les libations sont ravies au temple de Dieu.
Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani; lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe. Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse, inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga; pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.
14 Sanctifiez le jeûne, proclamez le service du Seigneur; rassemblez dans le temple de notre Dieu les anciens de tout le peuple de la terre, et criez sans relâche au Seigneur
Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya, itanani msonkhano wopatulika. Sonkhanitsani akuluakulu ndi anthu onse okhala mʼdziko ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu ndipo alirire Yehova.
15 Malheur, malheur, malheur en ce jour! Car le jour du Seigneur approche, et il viendra comme une calamité naissant d'une calamité.
Kalanga ine tsikulo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira; lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
16 Sous vos yeux, votre subsistance a été détruite; et les réjouissances et la joie ont disparu du temple de votre Dieu.
Kodi chakudya chathu sichachotsedwa ife tikuona? Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathu simulibe chimwemwe ndi chisangalalo?
17 Les génisses ont bondi devant leurs crèches vides; les trésors de vos granges sont dissipés; les pressoirs sont détruits; les froments desséchés.
Mbewu zikunyala poti pansi ndi powuma. Nyumba zosungiramo zinthu zawonongeka; nkhokwe zapasuka popeza tirigu wauma.
18 Que mettrons-nous en réserve pour nous? Les bœufs du troupeau ont mugi, parce qu'ils n'avaient plus de pâturage, et les petits des agneaux ont entièrement péri.
Taonani mmene zikulirira ziweto; ngʼombe zikungoyenda uku ndi uku chifukwa zilibe msipu; ngakhalenso nkhosa zikusauka.
19 Je crierai vers Toi, Seigneur; car le feu a consumé les beautés du désert, et la flamme tous les arbres des champs.
Kwa Inu Yehova ndilirira, pakuti moto wapsereza msipu wakuthengo, malawi amoto apsereza mitengo yonse ya mʼtchire.
20 Et les bêtes de la plaine ont tourné les yeux vers Toi, parce que les cours d'eau étaient à sec, et que le feu a dévoré les beautés du désert.
Ngakhale nyama zakuthengo zikulirira Inu; timitsinje tonse taphwa ndipo moto wapsereza msipu wa kuthengo.