< Joël 2 >
1 Sonnez de la trompette du haut de Sion, publiez à grands cris sur la montagne sainte; et que tous ceux qui habitent la terre soient confondus, parce que voilà le jour du Seigneur; il est près de vous,
Lizani lipenga mu Ziyoni. Chenjezani pa phiri langa loyera. Onse okhala mʼdziko anjenjemere, pakuti tsiku la Yehova likubwera, layandikira;
2 ce jour d'obscurité et de ténèbres, ce jour de nuées et de brouillards. Un peuple nombreux et puissant va se répandre sur les montagnes, comme la lumière du matin; jamais, dans les temps passés, on n'a vu son pareil, et après lui on n'en verra point de semblable durant les années, de générations en générations.
tsiku la mdima ndi chisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani. Ngati mʼbandakucha umene wakuta mapiri, gulu lalikulu ndi la ankhondo amphamvu likubwera, gulu limene nʼkale lomwe silinaonekepo ngakhale kutsogolo kuno silidzaonekanso.
3 Ce qui marche devant lui est un feu dévorant; ce qui marche à sa suite est une flamme ardente. La terre, avant qu'il arrive, était comme un jardin de délices; quand il fut passé, c'était un champ désert, et nul ne lui échappera.
Patsogolo pawo moto ukupsereza, kumbuyo kwawo malawi amoto akutentha zinthu. Patsogolo pawo dziko lili ngati munda wa Edeni, kumbuyo kwawo kuli ngati chipululu, kulibe kanthu kotsalapo.
4 Ils apparaîtront comme une vision de chevaux; ils courront comme des cavaliers.
Maonekedwe awo ali ngati akavalo; akuthamanga ngati akavalo ankhondo.
5 Ils s'élanceront sur les cimes des montagnes, comme un bruit de chars, comme un bruit de flammes dévorant des maisons, comme un peuple puissant et nombreux se rangeant en bataille.
Akulumpha pamwamba pa mapiri ndi phokoso ngati la magaleta, ngati moto wothetheka wonyeketsa ziputu, ngati gulu lalikulu la ankhondo lokonzekera nkhondo.
6 Devant leur force, les peuples seront broyés; tout visage sera comme le côté brûlé d'une chaudière.
Akangowaona, anthu a mitundu ina amazunzika mu mtima; nkhope iliyonse imagwa.
7 Ils courront comme des combattants; ils escaladeront les murailles comme des hommes de guerre; et chacun d'eux marchera dans sa voie, et ils ne dévieront pas de leurs sentiers;
Amathamanga ngati ankhondo; amakwera makoma ngati asilikali. Onse amayenda pa mizere, osaphonya njira yawo.
8 et nul ne s'écartera de son frère; ils marcheront chargés de leurs armes; ils tomberont avec leurs traits, et ils ne seront pas détruits.
Iwo sakankhanakankhana, aliyense amayenda molunjika. Amadutsa malo otchingidwa popanda kumwazikana.
9 Ils prendront la ville; ils courront sur les remparts; ils monteront sur les maisons; ils entreront comme des larrons par les fenêtres.
Amakhamukira mu mzinda, amathamanga mʼmbali mwa khoma. Amakwera nyumba ndi kulowamo; amalowera pa zenera ngati mbala.
10 Devant leur face, la terre sera confondue, et le ciel tremblera. le soleil et la lune seront voilés de ténèbres, et les étoiles retireront leur lumière.
Patsogolo pawo dziko limagwedezeka, thambo limanjenjemera, dzuwa ndi mwezi zimachita mdima, ndipo nyenyezi zimaleka kuwala.
11 Et le Seigneur fera entendre Sa voix devant Son armée, car Son camp est très nombreux, et les œuvres qui accomplissent Ses paroles sont puissantes, et le jour du Seigneur est un grand jour: il est éclatant; et qui sera capable de le soutenir?
Yehova amabangula patsogolo pawo, gulu lake lankhondo ndi losawerengeka, ndipo amphamvu ndi amene amamvera kulamula kwake. Tsiku la Yehova ndi lalikulu; ndi loopsa. Ndani adzapirira pa tsikulo?
12 Et maintenant le Seigneur Dieu vous dit: Convertissez-vous à Moi de toute votreâme; jeûnez, pleurez, frappez-vous la poitrine.
“Ngakhale tsopano, bwererani kwa Ine ndi mtima wanu wonse posala zakudya ndi kukhetsa misozi,” akutero Yehova.
13 Déchirez vos cœurs, et non vos vêtements. Et convertissez-vous au Seigneur votre Dieu, parce qu'Il est plein de clémence et de compassion, patient, abondant en miséricorde, et repentant des maux qu'Il fait en punissant.
Ngʼambani mtima wanu osati zovala zanu. Bwererani kwa Yehova Mulungu wanu, pakuti Iye ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka, ndipo amaleka kubweretsa mavuto.
14 Qui sait s'Il ne Se repentira pas, s'Il ne laissera pas après Lui des bénédictions, des offrandes et des libations pour le Seigneur votre Dieu.
Akudziwa ndani? Mwina adzasintha maganizo nʼkutimvera chisoni, nʼkutisiyira madalitso, a chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa kwa Yehova Mulungu wanu.
15 Sonnez de la trompette en Sion; sanctifiez le jeûne; publiez le service de Dieu;
Lizani lipenga mu Ziyoni, lengezani tsiku losala zakudya, itanitsani msonkhano wopatulika.
16 réunissez le peuple; sanctifiez l'Église; rassemblez les anciens; rassemblez les enfants à la mamelle; que l'époux quitte sa couche, et la femme son lit nuptial.
Sonkhanitsani anthu pamodzi, muwawuze kuti adziyeretse; sonkhanitsani akuluakulu, sonkhanitsani ana, sonkhanitsani ndi oyamwa omwe. Mkwati atuluke mʼchipinda chake, mkwatibwi atuluke mokhala mwake.
17 Que les prêtres qui servent le Seigneur pleurent au pied de l'autel; qu'ils disent: Seigneur, épargne Ton peuple; ne livre pas Ton héritage à l'opprobre; ne laisse pas les gentils dominer sur lui, de peur que l'on ne dise parmi les nations: Où est leur Dieu?
Ansembe amene amatumikira pamaso pa Yehova, alire pakati pa guwa lansembe ndi khonde la Nyumba ya Yehova. Azinena kuti, “Inu Yehova, achitireni chifundo anthu anu. Musalole kuti cholowa chanu chikhale chinthu chonyozeka, kuti anthu a mitundu ina awalamulire. Kodi nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina amanena kuti, ‘Ali kuti Mulungu wawo?’”
18 Mais le Seigneur a été jaloux de Sa terre, et Il a épargné Son peuple.
Pamenepo Yehova adzachitira nsanje dziko lake ndi kuchitira chisoni anthu ake.
19 Et le Seigneur a parlé, et Il a dit à Son peuple: Voilà que Je vous enverrai du blé, du vin et de l'huile, et vous vous en rassasierez, et Je ne vous livrerai pas plus longtemps aux opprobres des gentils.
Yehova adzawayankha kuti, “Ine ndikukutumizirani tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta ndipo mudzakhuta ndithu; sindidzakuperekaninso kuti mukhale chitonzo kwa anthu a mitundu ina.
20 Et Je chasserai loin de vous celui qui est venu de l'aquilon; Je le repousserai dans une contrée aride, et Je ferai disparaître sa tête dans la première mer, et sa queue dans la dernière; et sa pourriture montera, et son infection s'élèvera; car il s'est glorifié de ses œuvres.
“Ine ndidzachotsa ankhondo akumpoto kuti apite kutali ndi inu, kuwapirikitsira ku dziko lowuma ndi lachipululu, gulu lawo lakutsogolo ndidzalipirikitsira ku nyanja ya kummawa ndi gulu lawo lakumbuyo, ku nyanja ya kumadzulo. Ndipo mitembo yawo idzawola, fungo lake lidzamveka.” Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
21 Rassure-toi, terre; réjouis-toi et tressaille d'allégresse, parce que le Seigneur se glorifie d'agir.
Iwe dziko usachite mantha; sangalala ndipo kondwera. Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
22 Rassurez-vous, bêtes des champs, les plaines du désert ont bourgeonné; les arbres ont porté leurs fruits; le figuier et la vigne ont donné toute leur force.
Inu nyama zakuthengo, musachite mantha, pakuti msipu wa ku chipululu ukuphukira. Mitengo ikubala zipatso zake; mitengo ya mkuyu ndi mpesa ikubereka kwambiri.
23 Et vous, enfants de Sion, réjouissez-vous, tressaillez d'allégresse dans le Seigneur votre Dieu; Il vous a donné abondance de vivres; Il fera pleuvoir pour vous, comme autrefois, les pluies du printemps et de l'automne.
Inu anthu a ku Ziyoni sangalalani, kondwerani mwa Yehova Mulungu wanu, pakuti wakupatsani mvula yoyambirira mwachilungamo chake. Iye wakutumizirani mivumbi yochuluka, mvula yoyambirira ndi mvula ya nthawi ya mphukira, monga poyamba paja.
24 Et vos granges seront remplies de blé; et vos pressoirs regorgeront de vin et d'huile.
Pa malo opunthira padzaza tirigu; mʼmitsuko mudzasefukira vinyo watsopano ndi mafuta.
25 Et Je vous dédommagerai des ravages que pendant des années ont faits la sauterelle et la grande sauterelle, la nielle et la chenille, Ma grande armée que J'ai envoyée contre vous.
“Ine ndidzakubwezerani zonse zimene zinawonongedwa ndi dzombe, dzombe lalikulu ndi dzombe lalingʼono, dzombe lopanda mapiko ndi dzombe lowuluka; gulu langa lalikulu la nkhondo limene ndinalitumiza pakati panu.
26 Et vous mangerez, et vous serez rassasiés, et vous louerez le Nom du Seigneur votre Dieu, à cause des prodiges qu'en votre faveur Il aura faits. Et Mon peuple ne sera plus humilié.
Mudzakhala ndi chakudya chambiri, mpaka mudzakhuta, ndipo mudzatamanda dzina la Yehova Mulungu wanu, amene wakuchitirani zodabwitsa; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
27 Et vous connaîtrez que Je suis au milieu d'Israël, et que Je suis le Seigneur votre Dieu, et qu'il n'est point d'autre Dieu que Moi, et Mon peuple ne sera plus humilié à jamais.
Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndili mu Israeli, kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, ndi kuti palibenso wina; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
28 Et ensuite, voici ce qui arrivera: Je répandrai Mon Esprit sur toute chair; et vos fils prophétiseront, et vos anciens auront des songes, et vos jeunes hommes des visions.
“Ndipo patapita nthawi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi ana anu aakazi adzanenera, nkhalamba zanu zidzalota maloto, anyamata anu adzaona masomphenya.
29 Et en ce jour-là Je répandrai Mon Esprit sur Mes serviteurs et sur Mes servantes.
Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo.
30 Et Je mettrai des signes au ciel; et sur la terre, du sang, du feu et de la fumée.
Ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi pa dziko lapansi, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
31 Le soleil sera changé en ténèbres, et la lune en sang, avant qu'arrive le grand jour, le jour éclatant du Seigneur.
Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Ambuye.
32 Et il arrivera que quiconque invoquera le Nom du Seigneur sera sauvé; car alors sera sauvé tout ce qui sera sur la montagne de Sion et de Jérusalem, et avec eux tous les évangélisés que le Seigneur a élus, comme l'a dit le Seigneur.
Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka; pakuti chipulumutso chidzakhala pa Phiri la Ziyoni ndi mu Yerusalemu, monga Yehova wanenera, pakati pa otsala amene Yehova wawayitana.