< Job 5 >

1 Vois donc s'il est quelqu'un que tu puisses invoquer et qui t'écoute; peut-être l'un des saints anges t'apparaîtra.
“Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
2 Songe que la colère détruit l'insensé; l'envie tue celui qui s'égare.
Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
3 J'ai cependant vu des insensés prendre racine; mais leurs richesses ont été aussitôt dévorées.
Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
4 Qu'il n'y ait point de salut pour leurs enfants; que l'on forme autour d'eux des danses railleuses, devant la porte des petits; que nul ne les délivre.
Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
5 Que les justes mangent ce qu'ils ont amassé; qu'eux-mêmes ne puissent sortir de leur infortune et que leur force soit épuisée.
Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
6 Ce n'est point de la terre que naît le mal; ce n'est point dans les montagnes que germent les peines.
Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
7 Mais l'homme est né pour se rendre malheureux comme les petits des vautours pour voler sur les hautes cimes.
Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
8 Pour moi, je prierai le Seigneur, j'invoquerai le Seigneur maître de toutes choses,
“Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
9 Qui fait des merveilles innombrables et incompréhensibles, et des actions glorieuses et grandes,
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
10 Qui donne à la terre de la pluie et lui envoie l'eau du ciel,
Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
11 Qui élève les humbles et ranime ceux qui se croyaient perdus,
Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
12 Qui dissipe les desseins des trompeurs et empêche leurs mains de les exécuter,
Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
13 Qui confond la prudence des sages et bouleverse les artifices des gens dissimulés.
Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
14 Il les enveloppe en plein jour de ténèbres; il les fait marcher à tâtons, à midi comme à minuit.
Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
15 Puissent-ils périr dans les batailles; puisse le faible être délivré de la main des grands.
Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
16 Puisse le petit conserver de l'espérance; puisse le Seigneur fermer la bouche de l'injuste.
Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
17 Heureux l'homme qu'a châtié le Seigneur; qu'il se garde de rejeter de tels avertissements.
“Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
18 Car le Seigneur fait souffrir et il répare: il frappe et ses mains guérissent.
Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
19 Six fois il te tirera de peine; la septième fois, le mal ne t'atteindra plus.
Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
20 Pendant la famine, il te préservera de la mort; à la guerre il détournera de toi le fer ennemi.
Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
21 Il te mettra à l'abri des flagellations de la langue et tu n'auras rien à craindre des fléaux qui surviendront.
Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
22 Tu te riras des injustes et des déréglés; tu braveras les bêtes fauves.
Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
23 Les animaux les plus farouches te laisseront en paix.
Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
24 Tu sentiras d'où vient le calme de ta maison; et tes habitudes seront irréprochables.
Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
25 Tu verras croître une florissante famille, aussi nombreuse que les herbes des champs.
Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
26 Et tu descendras à la tombe mûr comme le blé que l'on moissonne en la saison, ou comme le monceau que l'on a renfermé dans l'aire après l'avoir récolté.
Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
27 Telles sont les pensées que j'ai cherchées et conçues; rentre en toi-même et vois ce que tu as fait.
“Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”

< Job 5 >