< Job 38 >

1 Aussitôt qu'Elihou eut fini son discours, le Seigneur dit à Job à travers un nuage et un tourbillon:
Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
2 Quel est celui qui me cache ses desseins? Il renferme des pensées en son cœur; croit-il qu'elles m'échapperont?
“Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
3 Ceins-toi les reins comme un homme; je vais te questionner: réponds-moi.
Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
4 Où étais-tu quand j'ai créé la terre? Déclare-le-moi si tu en as connaissance.
“Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
5 Qui en a réglé les dimensions; le sais-tu? Qui a promené sur elle le cordeau pour en prendre la mesure?
Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
6 Comment en a-t-on attaché les anneaux? Qui a posé sur elle la pierre angulaire?
Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
7 Lorsque les astres ont paru, tous mes anges à haute voix m'ont applaudi.
pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
8 J'ai renfermé la mer, j'ai placé des portes pour que, dans sa fureur, elle ne pût s'élancer hors des entrailles qui la contiennent.
“Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
9 Pour langes, je lui ai donné les brouillards, et pour vêtement les nuées.
pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
10 J'ai fixé ses limites, je l'ai entourée de battants et de verrous.
pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
11 Je lui ai dit: Tu iras jusque-là, tu n'iras pas plus loin; tes vagues se briseront sur toi-même.
Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
12 Est-ce de ton temps que j'ai disposé la lueur de l'aurore? et que l'étoile du matin a su qu'elle avait pour devoir
“Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
13 De secouer la terre, en la tenant par les deux ailes, et d'en faire tomber les impies?
kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
14 Est-ce toi qui, ayant pris de l'argile, as formé un être vivant et l'as mis sur la terre, doué de parole?
Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
15 As-tu ôté aux méchants la lumière, as-tu broyé les bras des orgueilleux?
Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
16 Es-tu descendu jusqu'au sources de la mer? As-tu marché dans les profondeurs de l'abîme?
“Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
17 Les portes de la mort s'ouvrent-elles sans t'effrayer? Peux-tu soutenir sans épouvante les regards des gardiens de l'enfer? (questioned)
Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
18 La vaste étendue que le ciel recouvre ne t'a-t-elle pas averti? Dis-le- moi, que penses-tu de sa grandeur?
Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
19 Quelle est la contrée où la lumière passe la nuit? Quel est le lieu où résident les ténèbres?
“Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
20 Pourrais-tu m'y conduire, en connais-tu le chemin?
Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
21 Ne sais-je point que si dès lors tu étais né, tes jours ont été bien nombreux?
Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
22 As-tu visité les trésors de la neige? As-tu vu les trésors de la grêle?
“Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
23 Les tiens-tu en réserve pour l'heure où se montreront tes ennemis, pour les jours de la guerre et des combats?
zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
24 D'où viennent les frimas ou le vent du midi qui souffle sous le ciel?
Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
25 Quelle puissance a préparé la chute des pluies violente et la voie des cataclysmes
Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
26 Qui fondent sur des contrées où il n'y a point d'hommes, sur des déserts où les mortels ne possèdent rien;
kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
27 Qui fécondent des champs inhabités et leur font produire une herbe luxuriante?
kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
28 Quel est le père de la pluie? Qui a produit les gouttes de la rosée?
Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
29 De quel sein est sortie la glace, d'où est né le givre du ciel
Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
30 Qui descend comme l'eau coule? Quel est celui qui frappe de terreur les impies?
pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
31 Est-ce toi qui as enchaîné les pléiades et ouvert la clôture qui retenait Orion?
“Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
32 Feras-tu voir Mazuroth en son temps, et conduiras-tu sur sa chevelure l'étoile du soir elle-même?
Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
33 Connais-tu les révolutions du ciel et ce qui arrive en même temps sur la terre?
Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
34 Appelles-tu de la voix le nuage, t'obéit-il, en s'ébranlant verse-t-il des torrents d'eau?
“Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
35 Convoques-tu les éclairs? Viennent-ils en disant: Qu'y a-t-il?
Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
36 Qui donc a enseigné aux femmes l'art de faire des tissus; qui les a douées de l'adresse d'y tracer des ornements divers?
Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
37 Qui sait, en sa sagesse, dompter les nuages, et qui a courbé le ciel vers la terre?
Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
38 Il a été malléable comme de la terre en poudre, et je l'ai consolidé comme un bloc de pierre.
pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
39 Chasseras-tu pour donner aux lions leur nourriture? Rempliras-tu l'âme des serpents?
“Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
40 Ils craignent dans leurs repaires, et ils se tiennent en embuscade au fond des forêts.
pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
41 Qui a préparé au corbeau sa pâture? car ses petits, en secouant leurs ailes, ont crié au Seigneur pour demander à manger.
Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?

< Job 38 >