< Job 37 >

1 Ces réflexions ont troublé mon cœur, et il s'est écoulé hors de son enveloppe.
“Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.
2 Ecoute les accents de la colère du Seigneur; songe à tout ce qui sortira de sa bouche.
Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake, kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.
3 Il règne sur tout ce que le ciel recouvre, et sa lumière s'étend sur les ailes de la terre.
Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.
4 Des voix s'élèveront derrière lui, elles se récrieront avec insolence; elles ne changeront pas ceux qui le servent, parce qu'ils l'auront compris.
Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka. Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero. Pamene wabangula, palibe chimene amalephera kuchita.
5 Le Tout-Puissant fera retentir son tonnerre; il proclamera ses merveilles; car il a fait de grandes choses qui nous sont inconnues.
Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.
6 Il commande à la neige de tomber sur les champs; il règle l'hiver, la pluie, les tempêtes et les inondations qui signalent sa puissance.
Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’ ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’
7 Il appose son scel sur la main de l'homme, afin que chacun connaisse sa propre faiblesse.
Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake. Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.
8 Les bêtes fauves sont entrées en l'asile de l'homme; elles se sont reposées sur sa couche.
Zirombo zimakabisala ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.
9 Les douleurs envahissent ses chambres les plus retirées; elles naissent au plus profond de son âme.
Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake, kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.
10 Le Tout-Puissant de son souffle répand la froidure; il dispose de l'eau comme il lui plaît.
Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.
11 La nuée enveloppe aussi son élu, mais sa lumière la dissipe.
Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula, amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.
12 Et lui-même contourne selon sa volonté le cercle des travaux humains. Tout ce qu'il leur a prescrit,
Mulungu amayendetsa mitamboyo mozungulirazungulira dziko lonse lapansi kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.
13 Tout ce qu'il a réglé sur la terre le manifestera, et les champs, et les plantes, et sa miséricorde.
Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu, kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.
14 Recueille tout ce que j'ai dit, Job; contiens-toi, et ne perds pas de vue la puissance du Seigneur.
“Abambo Yobu, tamvani izi; imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.
15 Nous savons que Dieu, avant de créer les êtres, a séparé la lumière des ténèbres.
Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?
16 Il prévoit la dispersion des nuages et la chute des méchants.
Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo, ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?
17 Ta robe te tient chaud: c'est qu'il fait régner le calme sur la terre.
Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,
18 S'il te protège, tu consolideras ce qui tombe de vétusté; les choses les plus fortes, sans lui, sont comme la vision de l'onde qui s'écoule.
kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo limene ndi lolimba ngati chitsulo?
19 C'est pourquoi, apprends-le-moi, que lui dirons-nous? Cessons nos longs discours.
“Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye; sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.
20 Est-ce qu'il n'y a pas le livre ou bien le scribe, afin qu'étant homme je sache garder le silence?
Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu? Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?
21 La lumière n'est pas visible pour tous; la lèpre blanche s'attache aux vieux édifices, semblable à la faible lueur que Dieu répand sur les nuées.
Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa, ndi kunyezimira mlengalenga, kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.
22 L'aquilon amène des nuages éclatants comme l'or; ils ont la splendeur et la gloire
Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto; Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.
23 Du Tout-Puissant, et nous ne connaissons aucun vent qui lui soit semblable pour la force. Le souverain juge des choses justes croit-il devoir lui prêter la moindre attention?
Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa; pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.
24 Aussi les hommes craindront Dieu; les sages en leur cœur auront crainte devant lui.
Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri, kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”

< Job 37 >