< Job 19 >

1 Et Job reprenant dit:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Jusqu'à quand fatiguerez-vous mon âme et me tuerez-vous de vos discours?
“Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
3 Sachez seulement que le Seigneur m'a traité de la sorte. Persuadez-moi, et ne vous attachez pas tant à me faire honte.
Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
4 En vérité, j'ai sans doute failli; l'erreur réside avec moi. Dis-moi donc quelque chose que j'ignore, sans quoi je m'égarerai en mes réponses, et elles manqueront d'à propos.
Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
5 Cessez, car vous vous grandissez pour m'assaillir, et vous m'accablez d'outrages.
Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
6 Mais ne perdez donc pas de vue que c'est le Seigneur qui m'a troublé, et qu'il a élevé contre moi ses murailles.
pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
7 De vos injures je ne ferais que rire, et je ne dirais mot; quand je crierais, je n'obtiendrais pas de jugement.
“Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
8 Mais des remparts m'étreignent et je ne puis les traverser, et l'obscurité règne devant moi.
Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
9 Le Seigneur m'a ravi toute gloire, il a ôté la couronne que je portais sur la tête.
Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
10 Il m'a tiraillé dans tous les sens et j'ai succombé; il a abattu comme un arbre toute mon espérance.
Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
11 Il a déployé contre moi une colère terrible; il m'a regardé comme un ennemi.
Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
12 Ses épreuves me sont venues toutes ensemble; ses embuscades étaient placées sur toutes mes voies.
Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
13 Mes frères se sont éloignés; ils m'ont préféré des inconnus; mes amis n'ont eu aucune compassion.
“Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
14 Mes plus proches m'ont laissé sans soins; et ceux qui savaient mon nom l'ont oublié.
Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
15 Mes voisins, les servantes de ma maison; je suis un étranger pour eux.
Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
16 J'ai appelé mon serviteur, il n'est point venu; ma bouche est devenue suppliante.
Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
17 J'ai imploré ma femme, j'ai demandé les fils de mes concubines en les flattant,
Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
18 Ils m'ont répudié pour toujours; si je me relève, ils se récrient contre moi.
Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
19 J'ai été pour eux un objet d'horreur pour ceux qui m'ont vu; j'ai pour ennemis ceux que j'avais aimés.
Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
20 Mes chairs sous ma peau pourrissent, mes os sont entre les dents qui les rongent.
Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
21 Ayez pitié de moi, ayez pitié de moi, ô mes amis, car c'est la main du Seigneur qui m'a touché.
“Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
22 Pourquoi me poursuivez-vous comme me poursuit le Seigneur? Voulez-vous vous repaître de ma chair?
Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
23 Qui donc écrira mes plaintes pour les déposer en un livre impérissable?
“Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
24 Qui les gravera au burin sur la pierre ou le plomb?
akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
25 Car je sais que de toute éternité existe celui qui doit me délivrer, et sur la terre
Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
26 Faire revivre ma peau pour que je jouisse de ces choses...car c'est le Seigneur qui a fait ces choses
Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
27 Qu'en moi-même je sais; que mon œil a vues, et non l'œil d'autrui; et qui déjà sont accomplies en mon sein.
Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
28 Et si vous dites: Quel langage tiendrons-nous devant lui? quel sujet de discours trouverons-nous en sa personne?
“Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
29 Prenez garde aux choses cachées; songez que la colère tombera aussi sur les méchants; et alors ils sentiront où est la matière dont ils sont formés.
Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”

< Job 19 >