< Jérémie 6 >

1 Armez-vous de force, fils de Benjamin, pour fuir du milieu de Jérusalem; sonnez de la trompette à Thécué, et levez l'étendard de Béthacharam, parce que, du côté de l'aquilon, des maux nous menacent, et qu'une grande affliction arrive sur nous;
“Thawani, inu anthu a ku Benjamini! Tulukani mu Yerusalemu! Lizani lipenga ku Tekowa! Kwezani mbendera ku Beti-Hakeremu! Pakuti tsoka lalikulu likubwera kuchokera kumpoto, ndipo chiwonongekocho nʼchachikulu.
2 Et ton orgueil sera abaissé, fille de Sion.
Kodi mzinda wa Ziyoni suli ngati msipu wokongola kwambiri, kumene abusa amafikako ndi ziweto zawo?
3 Coutre elle marcheront les pasteurs avec leurs troupeaux, et ils dresseront leurs tentes autour d'elle, et chacun y viendra paître sa part de bétail.
Abusa ndi nkhosa zawo adzabwera kudzalimbana nawo; adzamanga matenti awo mowuzinga, ndipo aliyense adzakhazika anthu ake pamalo pake.”
4 Préparez-vous à la combattre; levez-vous, et donnons-lui l'assaut en plein midi. Malheur à nous! parce que le jour décline, et que les ombres du jour s'évanouissent.
Adzanena kuti, “Konzekani kuwuthira nkhondo mzindawo! Nyamukani, kuti tiwuthire nkhondo mzindawu masana ano. Koma tili ndi tsoka, dzuwa lapendeka, ndipo zithunzithunzi za kumadzulo zikunka zitalika.
5 Levez-vous, et donnons-lui l'assaut dans les ténèbres, et arrachons-lui ses fondations.
Tsono nyamukani kuti tiwuthire nkhondo mzindawu usiku uno ndi kuwononga malinga ake!”
6 Car voici ce que dit le Seigneur: Abats ses arbres, répands tes forces autour de Jérusalem. O ville menteuse, il y a en elle toute sorte d'oppression.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Dulani mitengo ndipo mumange mitumbira yankhondo kulimbana ndi Yerusalemu. Mzinda umenewu uyenera kulangidwa; wadzaza ndi kuponderezana.
7 Comme une citerne refroidit l'eau, ainsi sa méchanceté glace de froid; sans cesse on entend parler devant elle d'impiétés et d'afflictions.
Monga momwe chitsime chimatulutsira madzi ndi mmenenso Yerusalemu amatulutsira zoyipa zake. Chiwawa ndi chiwonongeko ndi zomwe zimamveka mu mzindamo; nthenda yake ndi mabala ake ndimaziona nthawi zonse.
8 Jérusalem, tu seras instruite par le fouet et la douleur; mon âme ne se séparera point de toi que je n'aie fait de toi une terre impraticable, qui ne sera plus habitée.
Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro, kuopa kuti chikondi changa pa iwe chingakuchokere ndi kusandutsa dziko lako kukhala bwinja mopanda munthu wokhalamo.”
9 Car voici ce que dit le Seigneur: Grappillez, grappillez comme une vigne les restes d'Israël; allez et revenez, comme le vendangeur pour remplir son panier.
Yehova Wamphamvuzonse anandiwuza kuti, “Adani adzawakunkha ndithu anthu otsala a Israeli, monga momwe amachitira populula mphesa. Tsono iwe yesetsa kupulumutsa amene ungathe monga mmene amachitira munthu wokolola mphesa.”
10 A qui vais-je parler et attester, et qui m'écoutera? Voilà que leurs oreilles sont incirconcises, et ils ne pourront entendre. Voilà que la parole du Seigneur leur inspire du mépris, et ils n'en veulent point.
Kodi ndiyankhule ndi yani ndi kumuchenjeza? Ndinene mawu ochenjeza kwa yani kuti amve? Makutu awo ndi otsekeka kotero kuti sangathe kumva. Mawu a Yehova ndi onyansa kwa iwo; sasangalatsidwa nawo.
11 Et j'ai assouvi ma colère, et je l'ai contenue en moi, et je ne les ai pas entièrement détruits. Mais je la répandrai au dehors sur les enfants à la mamelle, sur la synagogue des jeunes gens; en même temps l'on prendra les hommes et les femmes, et le vieillard plein de jours.
Koma ine ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova, ndipo ndatopa ndi kusunga mkwiyo wa Yehova. Yehova anandiwuza kuti, “Tsono ndidzawutulutsira mkwiyo umenewu pa ana oyenda mʼmisewu ndi pa achinyamata amene asonkhana pamodzi; pakutinso mwamuna ndi mkazi wake adzatengedwa, pamodzi ndi okalamba amene ali ndi zaka zochuluka.
12 Et leurs maisons, leurs champs, leurs femmes aussi appartiendront à d'autres, parce que j'étendrai la main sur les habitants de cette terre, dit le Seigneur.
Nyumba zawo adzazipereka kwa ena, pamodzi ndi minda yawo ndi akazi awo. Ndidzatambasula dzanja langa kukantha anthu okhala mʼdzikomo,” akutero Yehova.
13 Car, du petit au grand, ils ont commis des iniquités; depuis le prêtre jusqu'au faux prophète, ils ont fait des œuvres de mensonge.
“Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi dyera lofuna kupeza phindu mwa kuba; aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
14 Ils pansaient les plaies de mon peuple, mais avec dédain, en lui disant: La paix, la paix! Et où est-elle la paix?
Amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba pokha. Iwo amanena kuti, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
15 Aussi ont-ils été confondus parce qu'ils ont failli. Et encore ils n'ont pas été confondus comme ceux qui le sont réellement; car leur confusion même ne les a pas confondus. Et à cause de cela ils tomberont, et ce sera leur ruine; et au temps de ma visite ils périront, dit le Seigneur.
Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazo? Ayi, sachita manyazi ndi pangʼono pomwe; sadziwa ndi kugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalange,” akutero Yehova.
16 Voici ce que dit le Seigneur: Tenez-vous dans les voies, et regardez, et informez-vous des éternels sentiers du Seigneur. Voyez quelle est la bonne voie et marchez-y, et vous trouverez la purification de vos âmes. Et ils ont dit: Nous n'irons pas.
Yehova akuti, “Imani pa mphambano ndipo mupenye; kumeneko ndiye kuli njira zakale, funsani kumene kuli njira yabwino. Yendani mʼmenemo, ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu. Koma inu munati, ‘Ife sitidzayenda njira imeneyo.’
17 J'ai établi sur vous des sentinelles, disant: Écoutez la voix de la trompette. Et ils ont dit: Nous n'écouterons pas.
Ine ndinakupatsani alonda oti akuyangʼanireni ndipo ndinati, ‘Imvani kulira kwa lipenga!’ koma inu munati, ‘Sitidzamvera.’
18 A cause de cela, ils ont entendu les nations, et ceux qui paissaient leurs troupeaux.
Nʼchifukwa chake imvani, inu anthu a mitundu ina; yangʼanitsitsani, inu amene mwasonkhana pano, chimene chidzawachitikire anthuwo.
19 Terre, écoute: Voilà que je vais amener sur ce peuple des malheurs, fruit de leur rébellion; car ils n'ont point eu souci de mes paroles, et ils ont répudié ma loi.
Imvani, inu anthu okhala pa dziko lapansi, ndikubweretsa masautso pa anthu awa. Zimenezi ndi mphotho ya ntchito zawo. Iwowa sanamvere mawu anga ndipo anakana lamulo langa.
20 A quoi bon m'offrir de l'encens de Saba et du cinnamome d'une contrée lointaine, vos holocaustes ne me sont point agréables, et vos victimes ne me causent point de joie.
Kodi pali phindu lanji ngakhale mubwere ndi lubani kuchokera ku Seba, kapena zonunkhira zina kuchokera ku dziko lakutali? Nsembe zanu zopsereza Ine sindidzalandira; nsembe zanu sizindikondweretsa.”
21 Et c'est pourquoi le Seigneur a dit: Voilà que je vais envoyer une maladie sur ce peuple; les pères et les fils tomberont malades ensemble, les proches périront avec leurs voisins.
Choncho Yehova akuti, “Ndidzayika zokhumudwitsa pamaso pa anthu awa. Abambo ndi ana awo aamuna onse adzapunthwa ndi kugwa; anansi awo ndi abwenzi awo adzawonongeka.”
22 Et le Seigneur a dit: Voilà qu'un peuple vient de l'aquilon, et les nations se lèveront des extrémités de la terre.
Yehova akunena kuti, “Taonani, gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
23 Ils tiendront l'arc et le javelot. Ce peuple est audacieux, il sera sans pitié; sa voix est comme les flots de la mer; il combattra à cheval et sur des chars et tombera sur toi comme la flamme, ô fille de Sion.
Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndi opanda chifundo. Phokoso lawo lili ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo ndipo akonzekera ngati anthu ankhondo, kudzakuthirani nkhondo anthu a ku Ziyoni.”
24 Nous avons entendu ce qu'on en dit, et nos mains en sont défaillantes; l'angoisse nous a saisis avec des douleurs comme celles de l'enfantement.
A ku Ziyoni akuti “Ife tamva mbiri yawo, ndipo manja anthu alefukiratu. Nkhawa yatigwira, ndipo tikumva ululu ngati mayi pa nthawi yake yochira.
25 Ne sortez pas dans les champs, n'allez pas sur les chemins; car le glaive des ennemis est là tout alentour.
Musapite ku minda kapena kuyenda mʼmisewu, pakuti mdani ali ndi lupanga, ndipo ponseponse anthu akuchita mantha.
26 Fille de mon peuple, ceins-toi d'un cilice; couvre-toi de cendre; frappe amèrement ta poitrine, comme lorsqu'on pleure un bien-aimé; car soudain le malheur tombera sur vous.
Inu anthu anga, valani ziguduli ndipo gubudukani pa phulusa; lirani mwamphamvu ngati munthu wolirira mwana wake mmodzi yekha, pakuti mwadzidzidzi wowonongayo adzabwera kudzatipha.
27 Je t'ai établi pour mettre à l'épreuve ces peuples tant de fois éprouvés, et tu me connaîtras à ma manière d'éprouver moi-même leurs voies.
“Iwe Yeremiya, ndakuyika kuti ukhale choyesera zitsulo. Uwayese anthu anga monga ungayesere chitsulo kuti uwone makhalidwe awo.
28 Ils sont tous indociles, ils ne marchent point droit; c'est de l'airain et du fer, ils sont tous corrompus.
Onsewo ali ndi khalidwe lokanika ndi lowukira ndipo akunka nanena zamiseche. Iwo ndi olimba ngati mkuwa ndi chitsulo. Onse amangochita zoyipa zokhazokha.
29 Le soufflet manque à la forge, le plomb y manque, le batteur d'argent frappe à vide; seule leur malice n'est point épuisée.
Moto mu mvukuto ukuyaka kwambiri; mtovu watha kusungunuka ndi moto. Koma ntchito yosungunulayo sikupindula chifukwa zoyipa sizikuchokapo.
30 Appelez-les de l'argent réprouvé; car ils sont réprouvés par le Seigneur.
Iwo ali ngati siliva wotayidwa, chifukwa Yehova wawakana.”

< Jérémie 6 >