< Jérémie 2 >

1 Et voici ce que dit encore le Seigneur: Je me suis souvenu de ta jeunesse en ma miséricorde, et de mon amour pour ta consécration, quand tu suivais le Saint d'Israël, dit le Seigneur.
Yehova anandiwuza kuti,
2 Et voici ce que dit encore le Seigneur: Je me suis souvenu de ta jeunesse en ma miséricorde, et de mon amour pour ta consécration, quand tu suivais le Saint d'Israël, dit le Seigneur.
“Pita ukalengeze kwa anthu a ku Yerusalemu kuti Yehova akuti, “‘Ine ndikukumbukira mmene umakhulupirikira pa unyamata wako, mmene unkandikondera ngati momwe amachitira mkwatibwi, mmene unkanditsata mʼchipululu muja; mʼdziko losadzalamo kanthu.
3 Israël est le peuple saint du Seigneur, prémices de ses fruits; tous ceux qui le dévorent sont coupables; les maux viendront sur eux, dit le Seigneur.
Israeli anali wopatulika wa Yehova, anali ngati zipatso zake zoyamba kucha pa nthawi yokolola; onse amene anamuzunza anapezeka kuti ndi olakwa ndipo mavuto anawagwera,’” akutero Yehova.
4 Écoutez la parole du Seigneur, maison de Jacob, et vous, famille entière de la maison d'Israël
Imvani mawu a Yehova, inu zidzukulu za Yakobo, inu mafuko onse a Israeli.
5 Voici ce que dit le Seigneur: Quelle faute vos pères ont-ils trouvée en moi, pour s'éloigner ainsi de moi et marcher après les vanités et devenir vains eux-mêmes?
Yehova akuti, “Kodi makolo anu anandipeza nʼcholakwa chanji, kuti andithawe? Iwo anatsata milungu yachabechabe, nawonso nʼkusanduka achabechabe.
6 Et ils n'ont point dit: Où est le Seigneur qui nous a ramenés de la terre d'Égypte, qui nous a conduits dans le désert, en une terre inhabitée et sans chemin, terre sans eau et sans fruit, que nul n'avait traversée et que nul n'habitait?
Iwo sanafunse nʼkomwe kuti, ‘Kodi Yehova ali kuti, amene anatitulutsa mʼdziko la Igupto natitsogolera mʼchipululu mʼdziko lowuma ndi lokumbikakumbika, mʼdziko lopanda mvula ndi la mdima, dziko limene munthu sadutsamo ndipo simukhala munthu aliyense?’
7 Et je vous ai menés sur le Carmel, pour vous en faire manger les fruits et les biens; et vous êtes entrés dans ma terre, et vous l'avez souillée, et vous avez fait de mon héritage une abomination.
Ndinakufikitsani ku dziko lachonde kuti mudye zipatso zake ndi zabwino zake zina. Koma inu mutafika munaliyipitsa dziko langa ndi kusandutsa cholowa changa kukhala chonyansa.
8 Les prêtres n'ont pas dit: Où est le Seigneur? Et les dépositaires de la loi ne m'ont point connu; et les pasteurs ont péché contre moi, et les prophètes ont prophétisé pour Baal, et ils ont marché après des vanités.
Ansembe nawonso sanafunse kuti, ‘Yehova ali kuti?’ Iwo amene amaphunzitsa malamulo sanandidziwe; atsogoleri anandiwukira. Aneneri ankanenera mʼdzina la Baala, ndi kutsatira mafano achabechabe.
9 A cause de cela, j'entrerai encore en jugement avec vous, et j'entrerai en jugement avec vos fils.
“Chifukwa chake Ine ndidzakuyimbaninso mlandu,” akutero Yehova. “Ndipo ndidzayimbanso mlandu zidzukulu zanu.
10 Allez aux lies de Céthim et voyez, envoyez à Cédar, informez-vous et voyez si on y fait pareilles choses;
Pitani kumadzulo ku chilumba cha Kitimu, ndipo mukaone, tumizani anthu ku Kedara kuti akafufuze bwino; ndipo muona kuti zinthu zoterezi sizinachitikepo nʼkale lomwe:
11 Si les gentils ont changé leurs dieux (et ce ne sont pas des dieux). Cependant mon peuple a échangé sa gloire pour des choses sans utilité.
Kodi ulipo mtundu wa anthu uliwonse umene unasinthapo milungu yake? (Ngakhale kuti si milungu nʼkomwe). Koma anthu anga asinthitsa Mulungu wawo waulemerero ndi mafano achabechabe.
12 Le ciel en a été stupéfait et il a frémi de choses pires encore, dit le Seigneur.
Inu mayiko akumwamba, dabwani ndi zimenezi, ndipo njenjemerani ndi mantha aakulu,” akutero Yehova.
13 Car mon peuple a fait deux choses mauvaises: ils m'ont délaissé, moi la fontaine d'eau vive, et ils se sont creusé des citernes crevassées qui ne pourront retenir l'eau.
“Popeza anthu anga achita machimo awiri: Andisiya Ine kasupe wa madzi a moyo, ndi kukadzikumbira zitsime zawo, zitsime zongʼaluka, zomwe sizingathe kusunga madzi.
14 Israël est-il un esclave? est-il né dans la servitude? Pourquoi est-il devenu une proie?
Israeli si wantchito kapena kapolo wobadwira mʼnyumba, ayi. Nanga nʼchifukwa chiyani amuwononga chotere?
15 Les lions ont rugi contre lui; et ceux qui ont fait de ses champs un désert ont jeté des clameurs; et ses cités ont été détruites, parce qu'elles n'étaient plus habitées.
Adani ake abangulira ndi kumuopseza ngati mikango. Dziko lake analisandutsa bwinja; mizinda yake anayitentha popanda wokhalamo.
16 Et les fils de Memphis et de Taphnès t'ont connue, ô Jérusalem, et ils se sont joués de toi.
Ndiponso Aigupto a ku Mefisi ndi a ku Tapanesi akuphwanyani mitu.
17 Et n'as tu pas été traitée de la sorte pour m'avoir abandonné? dit le Seigneur ton Dieu.
Zimenezitu zakuchitikirani chifukwa munasiya Yehova Mulungu wanu pamene Iye ankakutsogolerani pa njira yanu?
18 Et maintenant qu'as-tu à faire avec la voie de l'Égypte, pour y boire l'eau du Géhon? Qu'as-tu à faire avec la voie des Assyriens, pour y boire l'eau de leurs fleuves?
Tsopano mudzapindula chiyani mukapita ku Igupto, kukamwa madzi a mu Sihori? Ndipo mudzapindulanji mukapita ku Asiriya, kukamwa madzi a mu mtsinje wa Yufurate?
19 Ta rébellion même te punira, et ta malice t'accusera; sache donc, et vois comme il est amer pour toi de m'avoir abandonné, dit le Seigneur ton Dieu; je ne me suis point complu en toi, dit le Seigneur ton Dieu.
Kuyipa kwanuko kudzakulangani; kubwerera mʼmbuyo kwanuko kudzakutsutsani. Tsono ganizirani bwino, popeza ndi chinthu choyipa kundisiya Ine Yehova Mulungu wanu; ndi chinthu chowawa ndithu kusandiopa Ine Mulungu wanu. Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
20 Dès les premiers temps, tu as rompu ton joug, tu as mis en pièces tes liens, et tu as dit: Je ne vous servirai pas, mais j'irai sur tous les hauts lieux, et à l'ombre de tous les bois touffus je me livrerai à ma prostitution.
“Kuyambira kalekale inu munathyola goli lanu ndi kudula msinga zanu; munanena kuti, ‘Sitidzakutumikirani!’ Ndithudi, inu mwakhala ngati mkazi wachiwerewere. Mukupembedza milungu ina pa phiri lililonse lalitali ndiponso pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
21 Moi cependant j'ai planté pour toi une vigne féconde en fruits, toute de bon plant; pourquoi as-tu tourné à l'amertume, ô vigne étrangère?
Ine ndinakudzala iwe ngati mtengo wampesa wosankhika; unali mpesa wabwino kwambiri ndi wodalirika. Nanga nʼchifukwa chiyani wasanduka mpesa wachabechabe wonga wa kutchire?
22 Quand même on te laverait dans le nitre, quand tu multiplierais pour toi la saponaire, tu serais toujours souillée de tes iniquités devant moi, dit le Seigneur.
Ngakhale utasamba ndi soda kapena kusambira sopo wambiri, kuthimbirira kwa machimo ako kumaonekabe pamaso panga,” akutero Ambuye Yehova.
23 Comment peux-tu dire: Je ne me suis point souillée, je n'ai point couru après Baal? Considère tes voies dans le cimetière, et reconnais ce que tu as fait; sa voix a poussé des hurlements jusqu'à l'entrée de la nuit.
“Iwe ukunena bwanji kuti, ‘Ine sindinadziyipitse; sindinatsatire Abaala’? Takumbukira mmene unkandichimwira mʼchigwa muja; zindikira bwino zomwe wachita. Iwe uli ngati ngamira yayikazi yaliwiro yomangothamanga uku ndi uku,
24 Elle a dilaté ses voies vers les eaux du désert; elle a été emportée au gré des désirs de son âme; elle a été asservie; qui la ramènera? Tous ceux qui la cherchent n'auront pas de peine; ils la trouveront dans son abaissement.
wakhala ngati mbidzi yozolowera mʼchipululu, yonka ninunkhiza pa nthawi yachisika. Ndani angayiretse chilakolako chakecho? Mphongo iliyonse yoyikhumba sidzavutika. Pa nthawi yachisika chakecho mphongoyo idzayipeza.
25 Détourne ton pied de la voie escarpée, et ton gosier de la soif; mais elle a dit: J'aurai du courage, parce que j'aime les étrangers; et elle a cheminé après eux.
Iwe usathamange, nsapato zingakuthere kuphazi ndi kukhosi kwako kuwuma ndi ludzu. Koma unati, ‘Zamkutu! Ine ndimakonda milungu yachilendo, ndipo ndidzayitsatira.’
26 Comme un larron est confondu quand il est surpris, ainsi seront confondus les enfants d'Israël, et leurs rois, et leurs princes, et leurs prêtres, et leurs prophètes.
“Monga momwe mbala imachitira manyazi pamene yagwidwa, moteronso nyumba ya Israeli idzachita manyazi; Aisraeliwo, mafumu ndi akuluakulu awo, ansembe ndi aneneri awo.
27 Ils ont dit au bois: Tu es mon père; et au marbre: Tu m'as engendré; et ils m'ont tourné le dos, et non la face. Et au jour de leurs maux ils diront: Seigneur, levez-vous et sauvez-nous!
Iwo amawuza mtengo kuti, ‘Iwe ndiwe abambo athu,’ ndipo amawuza mwala kuti, ‘Iwe ndiye amene unatibala.’ Iwo andifulatira Ine, ndipo safuna kundiyangʼana; Koma akakhala pa mavuto amati, ‘Bwerani mudzatipulumutse!’
28 Et où sont tes dieux, que tu t'es fabriqués? Se lèveront-ils? te sauveront-ils au jour de ton malheur? car tu avais autant de dieux que de villes, Juda; et dans toutes les rues de Jérusalem on sacrifiait à Baal.
Nanga ili kuti milungu yanu imene munadzipangira nokha? Ibweretu ngati ingathe kukupulumutsani pamene muli pamavuto! Inu anthu a ku Yuda, milungu yanu ndi yambiri kuchuluka kwake ngati mizinda yanu.
29 Pourquoi me parlez-vous? Vous avez tous été impies, et tous vous avez péché contre moi, dit le Seigneur.
“Kodi mukundizengeranji mlandu? Nonse mwandiwukira,” akutero Yehova.
30 En vain j'ai frappé vos enfants; vous n'en avez point été corrigés; le glaive a détruit vos prophètes, comme un lion dévorant, et vous n'en avez pas été épouvantés.
“Ine ndinalanga anthu ako popanda phindu; iwo sanaphunzirepo kanthu. Monga mkango wolusa, lupanga lanu lapha aneneri anu.
31 Écoutez la parole du Seigneur: Voici ce que dit le Seigneur: Ai-je été un désert, ou une terre aride pour Israël? Pourquoi mon peuple a-t-il dit: Nous ne voulons pas de maître, nous n'irons plus à vous?
“Inu anthu a mʼbado uno, ganizirani bwino mawu a Yehova: “Kodi Ine ndinakhalapo ngati chipululu kwa Israeli kapena ngati dziko la mdima wandiweyani? Chifukwa chiyani anthu anga akunena kuti, ‘Ife tili ndi ufulu omayendayenda; sitidzabweranso kwa Inu’?
32 Est-ce qu'une jeune épouse oublie sa parure, et une vierge les bandelettes de son sein? Et moi, mon peuple m'a oublié durant des jours sans nombre.
Kodi namwali amayiwala zokongoletsera zake, kapena kuyiwala zovala zake za ukwati? Komatu anthu anga andiyiwala masiku osawerengeka.
33 Quel bien fais-tu encore dans ta voie, pour rechercher ma tendresse? Tu ne fais rien; au contraire, tu as fait le mal pour souiller tes voies.
Mumadziwa bwino njira zopezera zibwenzi! Choncho ngakhale akazi oyipa omwe mumawaphunzitsa njira zanu.
34 Et l'on a trouvé dans tes mains le sang d'âmes innocentes. Je ne les ai point vus dans des tombeaux, mais au pied de chaque chêne.
Ngakhale pa zovala zako anthu amapezapo magazi a anthu osauka osalakwa. Anthuwo simunawapeze akuthyola nyumba. Komabe ngakhale zinthu zili chomwechi,
35 Et tu as dit: Je suis innocente, détournez de moi votre colère. Mais voilà que j'entrerai en jugement avec toi, parce que tu as dit: Je n'ai point péché;
inu mukunena kuti, ‘Ndife osalakwa, sadzatikwiyira.’ Ndidzakuyimbani mlandu chifukwa mukunena kuti, ‘Ife sitinachimwe.’
36 Parce que, pleine de mépris pour moi, tu es rentrée dans tes anciennes voies. Et tu seras déshonorée par l'Égypte, comme tu l'as été par Assur,
Chifukwa chiyani mukunkabe nimusinthasintha njira zanu? Aigupto adzakukhumudwitsani monga momwe Asiriya anakuchititsani manyazi.
37 D'où tu es sortie les mains sur la tête; car le Seigneur a rejeté ton espérance, et en Égypte tu n'auras aucune prospérité.
Mudzachokanso kumeneko manja ali kunkhongo. Popeza Ine Yehova ndawakana anthu amene munkawadalira, choncho sadzakuthandizani konse.

< Jérémie 2 >