< Jérémie 15 >

1 Et le Seigneur me dit: Quand même Moïse et Samuël comparaîtraient devant ma face, mon âme n'est pas pour ce peuple; chasse-le et qu'il s'en aille.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Ngakhale Mose ndi Samueli akanayima pamaso panga kupempherera anthu awa, Ine sindikanawachitira chisoni. Achotseni ndipo ndisawaonenso! Aleke apite!
2 Et s'ils te disent: Où irons-nous? réponds, voici ce que dit le Seigneur: Vous irez les uns à la peste, les autres au glaive, d'autres à la famine, d'autres à la captivité, autant que ces fléaux en pourront frapper.
Ndipo ngati akufunsa iwe kuti, ‘Kodi tipite kuti?’ uwawuze kuti, ‘Yehova akuti, “‘Oyenera kufa adzafa; oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga; oyenera kufa ndi njala adzafa ndi njala; oyenera kupita ku ukapolo adzapita ku ukapolo.’
3 Et je les punirai de quatre manières, dit le Seigneur; il y aura le glaive pour égorger, les chiens pour déchirer, les bêtes de la terre et les oiseaux du ciel pour dévorer et consumer.
“Ine ndidzawatumizira mitundu inayi ya zinthu zowononga,” akutero Yehova, “lupanga lowapha, agalu owaluma, mbalame zamumlengalenga ndiponso zirombo zoti ziwadye ndi kuwawononga.
4 Et je les livrerai, pour leur affliction, à toutes les nations de la terre, à cause de Manassès, fils d'Ézéchias, roi de Juda, et de tout ce qu'il a fait dans Jérusalem?
Ndidzawasandutsa kukhala chinthu chonyansa kwa anthu a maufumu onse a dziko lapansi chifukwa cha zimene Manase mwana wa Hezekiya mfumu ya Yuda anachita mu Yerusalemu.
5 Qui t'épargnera, Jérusalem? Qui craindra de te punir? Qui se penchera vers toi pour te rendre la paix.
“Kodi adzakumvera chisoni ndani, Yerusalemu? Kodi adzakulira ndani? Kodi ndani amene adzapatuka kufunsa za moyo wako?
6 Tu t'es détournée. de moi, dit le Seigneur, tu as reculé loin de moi; et j'étendrai la main sur toi, et je te détruirai, et je ne leur donnerai pas de rémission.
Inu mwandikana Ine,” akutero Yehova. “Inu mukubwererabe mʼmbuyo. Choncho Ine ndidzakukanthani. Ndatopa ndi kukuchitirani chifundo.
7 Et je les disperserai de toutes parts; aux portes mêmes de mon peuple, ils ont été privés de leurs enfants; ils ont perdu mon peuple par leurs méchancetés.
Ine ndidzakubalalitsani kukuchotsani mʼmizinda ya mʼdzikomo monga mmene amachitira ndi mankhusu popeta ndi lichero. Anthu anga ndinawaliritsa ndi kuwawononga chifukwa sanasinthe makhalidwe awo oyipa.
8 Les veuves chez eux ont été multipliées plus que le sable du rivage. J'ai en plein midi envoyé le malheur sur les fils et sur les mères; et la ville, soudain je l'ai frappée de trouble et de terreur.
Ndinachulukitsa amayi awo amasiye kupambana mchenga wa kunyanja. Amayiwo ndinawawonongera ana awo aamuna dzuwa lili pamutu. Mwadzidzidzi ndinawagwetsera kuwawa mtima ndi mantha.
9 Celle qui avait sept enfants en est privée; son âme a défailli; son soleil s'est couché au milieu du jour; elle a été confondue et maudite. Ce qui reste d'eux, je le livrerai au glaive en face de leurs ennemis.
Mayi wa ana asanu ndi awiri wakomoka ndipo akupuma wefuwefu. Dzuwa lake lalowa ukanali usana; anamuchititsa manyazi ndipo wathedwa nzeru. Otsala ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo kuti awaphe ndi lupanga,” akutero Yehova.
10 Hélas! ma mère, pourquoi m'avez-vous enfanté, pour être un homme de contradiction par toute la terre? Je n'ai été utile à personne, et personne ne m'a été utile; la force m'a manqué contre ceux qui me maudissent.
Kalanga ine, amayi pakuti munandibereka ine, munthu amene ndikutsutsana ndi kulimbana ndi anthu pa dziko lonse! Ine sindinakongoze kapena kukongola kanthu, komatu aliyense akunditemberera.
11 Soit, Maître, qu'ils aient raison contre moi si je ne me suis tenu auprès de vous au temps de leurs calamités et au temps de leur tribulation, pour les servir contre leurs ennemis.
Yehova anati, “Ndithudi, Ine ndidzakulanditsa kuti upeze bwino. Ndithudi, adani ako adzakupempha pa nthawi ya tsoka ndi ya mavuto awo.
12 En vain le fer est connu de toi, en vain un vêtement d'airain
“Palibe munthu amene angathe kudula chitsulo, makamaka chitsulo chochokera kumpoto chosakaniza ndi mkuwa.
13 est ta force; je livrerai tes trésors au pillage sur ton territoire entier pour prix de tous tes péchés,
Anthu ako ndi chuma chako ndidzazipereka kwa ofunkha popanda malipiro, chifukwa cha machimo anu onse a mʼdziko lanu lonse.
14 Et je t'asservirai à tes ennemis d'alentour, en une terre que tu ne connaissais pas; car le feu de ma colère est allumé, et il vous brûlera.
Ndidzakusandutsani akapolo a adani anu mʼdziko limene inu simulidziwa, chifukwa mkwiyo wanga wayaka ngati moto umene udzakutenthani.”
15 Seigneur, souvenez-vous de moi et visitez-moi; protégez-moi contre ceux qui me poursuivent, et ne tardez pas; sachez que c'est à cause de vous que je suis outragé
Ine ndinati, “Inu Yehova, mumadziwa zonse; kumbukireni ndi kundisamalira. Ndilipsireni anthu ondizunza. Ndilezereni mtima musandilande moyo wanga. Onani momwe ndi kuvutikira chifukwa cha Inu.
16 Par ceux qui tiennent pour rien votre parole; exterminez-les, et votre parole fera mes délices et la joie de mon cœur, parce que j'ai été appelé de votre nom, Seigneur tout-puissant.
Munandiyankhula ndipo mawu anu ndinawalandira bwino. Mawu anu anandipatsa chimwemwe ndipo mtima wanga unasangalala. Paja ine, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndimadziwika ndi dzina lanu.
17 Je ne me suis point assis dans leur assemblée quand ils vous raillaient; mais j'ai été saisi de crainte en face de votre main; je me suis assis solitaire, parce que j'étais rempli d'amertume.
Sindinakhale nawo mʼgulu la anthu amadyera, sindinasangalale nawo anthu amenewo. Ndinakhala ndekha chifukwa choti dzanja lanu linali pa ine ndipo munadzaza mu mtima mwanga ndi mkwiyo.
18 Pourquoi ceux qui m'affligent ont-ils prévalu sur moi? Ma blessure est profonde: comment en guérirai-je? me voici comme dans une eau trompeuse, à laquelle on ne peut se fier.
Nanga nʼchifukwa chiyani mavuto anga sakutha? Bwanji chilonda changa sichikupola? Kodi inu mudzakhala ngati mtsinje wowuma nthawi yachilimwe, kapena ngati kasupe wopanda madzi?”
19 A cause de cela, voici ce que dit le Seigneur: Si tu reviens toujours à moi, je te fortifierai, et tu resteras debout devant ma face; et si tu sépares le bien du mal, tu seras comme ma bouche, et ils reviendront à toi, sans que tu reviennes à eux.
Tsono Yehova anandiyankha kuti, “Ukabwerera kwa Ine, ndidzakulandiranso ndipo udzakhalanso mtumiki wanga. Ngati udzayankhula mawu oyenera osati achabechabe, udzakhalanso mneneri wanga. Anthu adzabwera kwa iwe ndipo sipadzafunika kuti iwe upite kwa iwo.
20 Et je te donnerai contre ce peuple une défense et un rempart d'airain; et ils te combattront et ne pourront rien contre toi, parce que je suis avec toi pour te sauver
Ndidzakusandutsa ngati khoma lolimba ngati mkuwa kwa anthu awa. Adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, pakuti Ine ndili nawe kukulanditsa ndi kukupulumutsa,” akutero Yehova.
21 Et te retirer des mains des méchants, et je te rachèterai de la main des hommes de pestilence.
“Ndidzakupulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa ndipo ndidzakuwombola kwa anthu ankhanza.”

< Jérémie 15 >