< Jérémie 12 >
1 Seigneur, vous êtes juste; aussi je me défendrai devant vous; je vous demanderai justice. Pourquoi la voie des impies est-elle prospère? pourquoi ceux qui vous ont répudié sont-ils florissants?
Yehova, Inu mumakhala wokhoza nthawi zonse ndikati nditsutsane nanu. Komabe ndikufuna kuyankhula nanu za mlandu wanga. Chifukwa chiyani anthu oyipa zinthu zimawayendera bwino? Chifukwa chiyani anthu achinyengo amakhala pabwino?
2 Vous les avez plantés, et ils ont pris racine; ils ont engendré, et ils ont produit des fruits. Vous êtes près de leur bouche, et loin de leurs reins.
Inu munawadzala ndipo anamera mizu; amakula ndi kubereka zipatso. Dzina lanu limakhala pakamwa pawo nthawi zonse, koma mitima yawo imakhala kutali ndi Inu.
3 Et vous, Seigneur, vous me connaissez, vous avez devant vous éprouvé mon cœur; purifiez-les pour le jour de leur égorgement.
Koma Inu Yehova, ine mumandidziwa; mumandiona ndipo mumayesa zolingalira zanga. Akokeni anthu oyipawo ngati nkhosa zokaphedwa! Ayikeni padera mpaka tsiku loti akaphedwe!
4 Jusques à quand la terre sera-t-elle en deuil avec des pâturages et des champs desséchés par la malice de ceux qui l'habitent? Les oiseaux et le bétail ont été détruits, parce que les hommes ont dit: Dieu ne verra point. nos voies.
Kodi dziko lidzakhala likulirabe mpaka liti ndipo udzu mʼmunda uliwonse udzakhalabe ofota mpaka liti? Nyama ndi mbalame kulibiretu chifukwa anthu amene amakhalamo ndi oyipa. Iwo amati: “Yehova sangathe kuona ntchito zathu.”
5 Tes pieds courent, et te voilà énervé; comment feras-tu donc pour combattre des cavaliers et te confier dans une terre de paix? Que feras-tu contre les débordements du Jourdain?
Yehova anayankha kuti, “Ngati kukutopetsa kuthamanga pamodzi ndi anthu nanga ungapikisane bwanji ndi akavalo? Ngati ukupunthwa ndi kugwa pa malo abwino, udzatha bwanji kuthamanga mʼnkhalango za ku Yorodani?
6 Tes frères eux-mêmes et la maison de ton père t'ont méprisé; ils ont eux- mêmes crié contre toi, ils se sont donc unis à ceux qui te poursuivaient par derrière; ne te fie pas à eux, quoiqu'ils te disent de belles paroles.
Ngakhale abale ako ndi anansi akuwukira, onsewo amvana zokuyimba mlandu. Usawakhulupirire, ngakhale ayankhule zabwino ndi iwe.
7 J'ai abandonné ma maison; j'ai renoncé à mon héritage; j'ai livré aux mains de ses ennemis celle qui était ma bien-aimée et ma vie.
“Ine ndawasiya anthu anga; anthu amene ndinawasankha ndawataya. Ndapereka okondedwa anga mʼmanja mwa adani awo.
8 Mon héritage est devenu contre moi comme le lion dans une forêt; il a rugi contre moi; à cause de cela je l'ai pris en haine.
Anthu amene ndinawasankha asanduka ngati mkango wa mʼnkhalango. Akundibangulira mwaukali; nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawo.
9 Mon héritage est-il pour moi un antre d'hyène ou l'enceinte d'une caverne? Allez, rassemblez toutes les bêtes fauves de la terre, et qu'elles viennent dévorer mon héritage.
Anthu anga amene ndinawasankha asanduka ngati mbalame yolusa yamawangamawanga imene akabawi ayizinga. Pitani, kasonkhanitseni nyama zakuthengo. Mubwere nazo kuti zidzadye mbalameyo.
10 Maints pasteurs ont ravagé ma vigne; ils ont souillé mon partage; ils ont fait de ma part bien-aimée un désert sans chemin.
Abusa ambiri anawononga munda wanga wa mpesa, anapondereza munda wanga; munda wanga wabwino uja anawusandutsa chipululu.
11 Elle a été livrée au ravage et à la dévastation. Toute la terre a été frappée de ruine à cause de moi, parce que nul homme n'a souci de moi en son cœur.
Unawusandutsadi chipululu. Ukanali wokhawokha chomwecho ukundilirira Ine. Dziko lonse lasanduka chipululu chifukwa palibe wolisamalira.
12 Ceux qui la dévastaient sont venus par toutes les voies du désert, parce que le glaive du Seigneur va dévorer la terre d'une extrémité à l'autre; il n'est plus de paix pour aucune chair.
Anthu onse owononga abalalikira ku zitunda zonse za mʼchipululu. Yehova watuma ankhondo ake kudzawatha kuyambira kumalire ena a dziko mpaka ku malire enanso a dziko, ndipo palibe amene adzakhale pa mtendere.
13 Semez des froments, et vous récolterez des chardons; leur part d'héritage ne leur rapportera rien; soyez confondus à cause de votre orgueil et de vos outrages à la face du Seigneur.
Anthu anafesa tirigu koma anatuta minga; anadzitopetsa kugwira ntchito koma osapeza phindu lililonse. Choncho mudzachita manyazi ndi zokolola zanu chifukwa cha mkwiyo wa Yehova.”
14 Car ainsi parle le Seigneur contre tous les méchants voisins qui touchent à mon héritage, que j'ai distribué à mon peuple d'Israël: Voilà que je vais les arracher de leur terre, et je rejetterai Juda du milieu d'eux.
“Anthu oyipa oyandikana ndi anthu anga Aisraeli, akuwalanda Aisraeliwo dziko, cholowa chimene ndinawapatsa. Nʼchifukwa chake ndidzawachotsa mʼdziko limenelo, ndipo ndidzachotsa banja la Yuda pakati pawo.
15 Et voici ce qui arrivera: après les avoir bannis, je changerai, et j'aurai pitié d'eux, et je les ferai rentrer dans leurs demeures, chacun dans son héritage et chacun dans son champ.
Komabe nditawachotsa, ndidzawachitiranso chifundo, ndipo ndidzabwezera aliyense cholowa chake ndi dziko lake.
16 Et ceci arrivera encore: s'ils s'instruisent, s'ils apprennent la voie de mon peuple, et à jurer en mon nom: Vive le Seigneur! comme ils avaient enseigné mon peuple à jurer par le nom de Baal, ils seront édifiés au milieu de mon peuple.
Ndipo ngati iwo adzaphunzira bwino njira za anthu anga ndi kulumbira mʼdzina langa, namanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ monga iwo anaphunzitsira anthu anga kulumbira mʼdzina la Baala, Ine ndidzawakhazikitsa pakati pa anthu anga.
17 Et s'il est une de ces nations qui ne se convertisse pas, je la détruirai, et elle sera perdue à jamais.
Koma ngati mtundu wina uliwonse sudzamvera, Ine ndidzawuchotsa ndi kuwuwonongeratu,” akutero Yehova.