< Jérémie 11 >
1 Voici la parole du Seigneur qui est venue à Jérémie, disant:
Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
2 Écoutez tous les paroles de cette alliance; et toi parle aux hommes de Juda et à ceux qui habitent Jérusalem.
“Imvani mawu a pangano ili, ndipo uwawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
3 Dis-leur: Voici ce que dit le Seigneur Dieu d'Israël: Maudit soit l'homme qui n'écoutera pas les paroles de cette alliance,
Awuze kuti Yehova, Mulungu wa Israeli akuti ‘adzakhala wotembereredwa munthu amene samvera mawu a pangano ili.
4 Que j'ai commandée à vos pères, le jour où je les ai conduits hors de la terre d'Égypte, hors de la fournaise de fer, disant: Soyez dociles à ma voix, et faites toutes les choses que je vous prescris; et vous serez mon peuple, et moi je serai votre Dieu;
Awa anali mawu amene ndinalamulira makolo anu nditawatulutsa mu Igupto, kuchoka mʼngʼanjo yamoto.’ Ine ndinati, ‘Mverani Ine ndi kuchita chilichonse chimene ndakulamulirani. Mukatero mudzakhala anthu anga ndi Ine ndidzakhala Mulungu wanu.
5 Afin que j'accomplisse le serment que j'ai fait à vos pères de leur donner une terre où coulent le lait et le miel, comme en ce jour. Et je répondis: Seigneur, qu'il soit ainsi!
Tsono Ine ndidzakwaniritsa lumbiro lomwe ndinalumbira kwa makolo anu kuti ndidzawapatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi,’ dziko lomwe inu lero mukukhalamo.” Tsono Ine ndinayankha kuti, “Ameni, Yehova.”
6 Et le Seigneur me dit: Lis ces paroles dans les villes de Juda. et hors de Jérusalem, disant: Écoutez les paroles de cette alliance, et mettez-les en pratique.
Yehova anandiwuza kuti, “Lengeza mawu onsewa mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu: ‘Mverani mawu a pangano ili ndi kuzitsatira.
7 Et ils ne les ont point pratiquées.
Kuyambira nthawi imene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto mpaka lero, ndakhala ndi kuwachenjeza kawirikawiri kuti, ‘Mverani Ine.’
8 Et ils ne les ont point pratiquées.
Koma sanamvere kapena kulabadirako. Aliyense anawumirira kuchita zoyipa za mʼmitima yawo. Ngakhale ndinawalamulira kuti asunge pangano langa koma iwo sanasunge. Choncho ndinawalanga monga ndinaneneramo.’”
9 Et le Seigneur me dit: On a découvert un complot tramé contre moi par les hommes de Juda, et ceux qui habitent Jérusalem;
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu andiwukira.
10 Ils sont revenus aux iniquités de leurs pères, qui autrefois n'ont point voulu écouter mes paroles, et voilà qu'ils marchent à la suite des dieux étrangers pour les servir; et la maison d'Israël et la maison de Juda ont déchiré l'alliance que j'avais faite avec leurs pères.
Abwereranso ku machimo a makolo awo, amene anakana kumvera mawu anga. Akutsata milungu ina ndi kumayitumikira. Aisraeli ndi Ayuda aphwanya pangano limene ndinachita ndi makolo awo.
11 A cause de cela, ainsi dit le Seigneur: Voilà que je vais amener sur ce peuple des maux dont il ne pourra se tirer; et ils crieront vers moi, et je ne les écouterai pas
Choncho Yehova akuti, ‘Ndidzawagwetsera mavuto amene sadzatha kuwalewa. Ngakhale adzandilirire, sindidzawamvera.
12 Et les villes de Juda et les habitants de Jérusalem s'en iront, et ils crieront vers les dieux étrangers, pour qui ils ont brûlé de l'encens; et ces dieux ne les sauveront pas au temps de leurs malheurs.
Anthu a mʼmizinda ya Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu adzapita ndi kukalirira milungu imene ankayifukizira lubani, koma milunguyo sidzawathandiza ndi pangʼono pomwe mavuto akadzafika.
13 Car, Juda, tu as autant de dieux que de villes; et vous avez dressé autant d'autels pour sacrifier à Baal qu'il y a de rues à Jérusalem.
Iwe Yuda, uli ndi milungu yochuluka ngati chiwerengero cha mizinda yako; chiwerengero cha maguwa ansembe amene umafukizirapo lubani kwa Baala chili ngati misewu ya mu Yerusalemu.’
14 Et toi, ne prie point pour ce peuple, n'intercède pas pour eux, par oraison ou prière; car je ne les écouterai pas le jour où ils m'invoqueront, le jour de leur affliction.
“Tsono iwe Yeremiya usawapempherere anthu amenewa ngakhale kuwadandaulira kapena kuwapepesera, chifukwa sindidzawamvera akadzandiyitana pa nthawi ya mavuto awo.
15 D'où vient que ma bien-aimée a commis l'abomination dans ma demeure? Les prières ou les chairs sanctifiées effaceront-elles les malices ou te les feront-elles éviter?
“Kodi anthu anga okondedwa akudzachita chiyani mʼNyumba yanga? Kodi suja iwowa amachita zoyipa zambiri? Kodi mungathe kupulumuka, tsoka osakugwerani chifukwa cha nsembe zanuzo?”
16 Le Seigneur t'a donné le nom d'olivier, beau à la vue et donnant un bon ombrage; mais au bruit de son ébranchement, un feu a été allumé contre lui; grande est ton affliction, car ses rameaux sont devenus inutiles.
Kale Yehova ankakutchani mtengo wa olivi wa masamba obiriwira, wokhala ndi zipatso zokongola. Koma tsopano adzawutentha ndi mkuntho wamkokomo ndipo nthambi zake zidzapserera.
17 Et le Seigneur, qui t'avait plantée, a prononcé des maux contre toi en punition de ta méchanceté, maison d'Israël, et de la tienne, maison de Juda; car ils se sont nui à eux-mêmes pour m'irriter, en brûlant de l'encens à Baal.
Yehova Wamphamvuzonse, amene anakudzalani, walamula kuti mavuto akugwereni. Inu a banja la Yuda ndi a banja la Israeli munachitira Yehova zoyipa ndi kumukwiyitsa pamene munkapereka nsembe zanu kwa Baala.
18 Seigneur, instruisez-moi, et je saurai. Et alors j'ai vu leurs machinations contre moi.
Yehova anandiwululira ndipo ndinadziwa. Iye anatsekula maso anga kuti ndione chiwembu chawocho.
19 Mais moi, comme un agneau innocent conduit au sacrifice, je ne remarquais rien. Ils avaient conçu contre moi un mauvais dessein, disant: Allons, mêlons du bois à son pain, effaçons-le de la terre des vivants, et que nul ne se souvienne de son nom.
Ndinali ngati mwana wankhosa wofatsa amene akupita naye kukamupha; sindinkadziwa kuti chiwembu chimene ankakonzekeracho chinkaloza ine. Iwo amati: “Tiyeni timuphe munthu ameneyu kuti dzina lake lisadzakumbukiridwenso.”
20 Seigneur, qui jugez selon la justice, qui sondez les reins et les cœurs, puissé-je voir la vengeance que vous tirerez d'eux; car je vous ai exposé ma cause.
Koma, Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumaweruza molungama ndi kuyesa mitima ndi maganizo, lolani kuti ine ndione kuti mwawalipsira, pakuti mlandu wanga ndawupereka mʼmanja mwanu.
21 A cause de cela, voici ce que dit le Seigneur contre les hommes d'Anathoth qui en veulent à ma vie, et qui disent: Tu cesseras de prophétiser au nom du Seigneur, sinon tu périras de nos mains.
“Nʼchifukwa chake Yehova akunena za anthu a ku Anatoti amene akufuna kuwononga moyo wako namanena kuti, ‘Usanenere mʼdzina la Yehova, ukatero ife tidzakupha ndi manja athu,’
22 Et moi, voilà que je les visiterai; leurs jeunes gens mourront par le glaive, et leurs fils et leurs filles mourront de faim.
koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndidzawalanga. Achinyamata awo adzaphedwa ndi lupanga, ana awo aamuna ndi aakazi adzafa ndi njala.
23 Et il ne restera rien d'eux, parce que je vais amener des maux sur les habitants d'Anathoth, en l'année où je les visiterai.
Sipadzakhala otsala ndi mmodzi yemwe, chifukwa ndidzalanga anthu a ku Anatoti chikadzafika chaka chawo cha chilango.’”