< Isaïe 60 >

1 Resplendis, Jérusalem, resplendis de lumière; car ta lumière est venue, et la gloire du Seigneur s'est levée sur toi.
“Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika, ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.
2 Voilà que les ténèbres enveloppent la terre, et que les Gentils sont dans l'obscurité; mais le Seigneur apparaîtra sur toi, et sa gloire va se montrer en toi.
Taona, mdima waphimba dziko lapansi ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina, koma Yehova adzakuwalira iwe, ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.
3 Et les rois viendront à ta lumière, et les nations à ta splendeur.
Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.
4 Lève les yeux autour de toi, et vois tes enfants rassemblés; tous tes fils sont venus de loin, et tes filles seront transportées sur les épaules des hommes.
“Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika. Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe; ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.
5 Tu verras alors, et tu seras dans l'admiration, et tu seras extasiée en ton cœur; car les richesses de la mer, des nations et des peuples seront transportées chez toi.
Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri, mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe; chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.
6 Et il te viendra des troupeaux de chamelles, et des chameaux de Madian et de Gépha couvriront tes chemins. Tous les hommes de Saba viendront chargés d'or, et t'offriront de l'encens, et publieront la bonne nouvelle du salut de Dieu.
Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako, ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai. Ndipo onse a ku Seba adzabwera atanyamula golide ndi lubani uku akutamanda Yehova.
7 Et toutes les brebis de Cédar seront rassemblées, et les béliers de Nabajoth viendront à toi; et sur mon autel on fera des offrandes qui me seront agréables, et ma maison de prière sera glorifiée.
Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu, nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani; zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe, ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.
8 Qui sont ceux-là qui volent vers moi comme des nuages, ou comme des colombes avec leurs petits?
“Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo, ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?
9 Les îles m'ont attendu, et les navires de Tarsis sont les premiers à ramener de loin tes enfants, et avec eux leur argent et leur or, pour sanctifier le nom du Seigneur saint, et glorifier le Saint d'Israël.
Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali; patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi, zikubweretsa ana ako ochokera kutali, pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo, kudzalemekeza Yehova Mulungu wako, Woyerayo wa Israeli, pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.
10 Et les étrangers réédifieront tes remparts, et leurs rois s'empresseront autour, de toi; car je t'ai frappée dans ma colère, et je t'ai aimée dans ma miséricorde.
“Alendo adzamanganso malinga ako, ndipo mafumu awo adzakutumikira. Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya, koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.
11 Et tes portes seront toujours ouvertes; on ne les fermera ni jour ni nuit pour introduire chez toi les richesses des Gentils et leurs rois qu'on t'amènera.
Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse, sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku, kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo, akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.
12 Car les nations et les rois qui ne te seront pas assujettis périront, et ces nations seront complètement dévastées.
Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe; adzawonongeka kotheratu.
13 La gloire du Liban viendra à toi, avec le cyprès, et le cèdre, pour glorifier mon lieu saint.
“Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini, mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika; ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.
14 Et les fils de ceux qui t'ont humiliée et irritée viendront à toi, tout tremblants, et tu seras appelée Sion, la ville du Saint d'Israël,
Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani; onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu. Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova; Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.
15 Parce que tu auras été abandonnée et haïe, sans que personne te secourût. Et je te donnerai une allégresse éternelle, une joie qui passera de générations en générations.
“Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe, koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya, ndipo udzakhala malo a chimwemwe cha anthu amibado yonse.
16 Et tu seras allaitée du lait des nations, et tu seras nourrie des richesses des rois. Et tu sauras que je suis le Seigneur qui te sauve, le Dieu d'Israël qui te rachète.
Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu ndi kuleredwa pa maere aufumu, motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako, Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.
17 Et au lieu d'airain je t'apporterai de l'or; au lieu de fer, je t'apporterai de l'argent; au lieu de bois, je t'apporterai de l'airain, et au lieu de pierre, je t'apporterai du fer. Et je te donnerai des princes dans la paix, et des surveillants dans la justice.
Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa, ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo. Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala. Olamulira ako adzakhala a mtendere. Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.
18 Et l'on n'entendra plus parler d'iniquité sur ta terre, de misère ni d'oppression sur ton territoire; mais tes remparts seront appelés Salut, et tes portes, Louanges.
Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako, bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako, ndidzakhala malinga ako okuteteza ndipo udzanditamanda.
19 Et ce ne sera plus le soleil qui éclairera tes jours, ni la lune tes nuits; mais le Seigneur sera ta lumière éternelle, et Dieu ta gloire.
Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire, kapena mwezi kuti uwunikire usiku, pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya, ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.
20 Et pour toi le soleil ne se couchera point, la lune ne sera point éclipsée; car le Seigneur sera ta lumière éternelle, et tes jours de deuil seront accomplis.
Dzuwa lako silidzalowanso, ndipo mwezi wako sudzazimiriranso; Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya, ndipo masiku a mavuto ako adzatha.
21 Et ton peuple entier sera juste, et il héritera de la terre pour toujours; et il conservera ses rejetons et les œuvres de ses mains pour ma gloire.
Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya. Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala, ntchito ya manja anga, kuti aonetse ulemerero wanga.
22 Du plus petit il en sortira des milliers, et du plus faible, une grande nation. Et moi le Seigneur, au temps marqué, je les réunirai tous.
Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko, kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu. Ine ndine Yehova, nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”

< Isaïe 60 >