< Isaïe 56 >

1 Voici ce que dit le Seigneur: Observez le jugement et agissez selon la justice; car mon salut est près d'arriver, et ma miséricorde va se révéler.
Yehova akuti, “Chitani chilungamo ndi zinthu zabwino, chifukwa chipulumutso changa chili pafupi ndipo ndidzakuwombolani posachedwapa.
2 Heureux l'homme qui fait ces choses! Heureux celui qui s'y attache, qui se garde de profaner les sabbats, et conserve ses mains pures de toute iniquité!
Ndi wodala munthu amene amachita zimenezi, munthu amene amalimbika kuzichita, amene amasunga Sabata osaliyipitsa, ndipo amadziletsa kuchita zoyipa.”
3 Que l'étranger qui se donne au Seigneur ne dise pas: Le Seigneur me séparera certainement de son peuple! Que l'eunuque ne dise pas: Je suis un bois mort!
Mlendo amene waphatikana ndi Yehova asanene kuti, “Ndithu Yehova wandichotsa pakati pa anthu ake.” Ndipo munthu wofulidwa asanene kuti, “Ine ndine mtengo wowuma basi.”
4 Voici ce que le Seigneur dit aux eunuques, à tous ceux qui garderont mes sabbats, qui choisiront les choses que j'aime, et s'attacheront à mon alliance:
Popeza Yehova akuti, “Wofulidwa amene amasunga masabata anga, nachita zokomera Ine ndi kusunga pangano langa,
5 Je leur donnerai dans ma demeure et dans mes murailles une place honorable, meilleure pour eux que des fils et des filles; je leur donnerai un nom éternel, qui ne défaillira jamais.
ndidzawapatsa dzina ndi mbiri yabwino mʼkati mwa Nyumba yanga ndi makoma ake, kuposa kukhala ndi ana aamuna ndi aakazi. Ndidzawapatsa dzina labwino, losatha ndi losayiwalika.”
6 Quant aux étrangers qui se donnent au Seigneur pour le servir, pour aimer le nom du Seigneur, et pour être dévoués à son service; quant à tous ceux qui sont attentifs à ne point profaner mes sabbats, et qui s'attachent à mon alliance,
Yehova akuti, “Alendo amene amadziphatika kwa Yehova, motero kuti amamutumikira Iye, amakonda dzina la Yehova, amamugwirira ntchito, komanso kusunga Sabata osaliyipitsa ndi kusunga bwino pangano langa,
7 Je les conduirai sur ma montagne sainte; je les réjouirai dans la maison de ma prière. Leurs holocaustes et leurs victimes seront agréés sur mon autel. Car ma maison sera appelée une maison de prière pour toutes les nations.
amenewa Ine ndidzawafikitsa ku phiri langa lopatulika, ndidzawapatsa chimwemwe mʼnyumba yanga ya mapemphero. Zopereka zawo zopsereza ndi nsembe zawo ndidzazilandira pa guwa langa la nsembe. Paja nyumba yanga idzatchedwa nyumba ya mapemphero ya anthu a mitundu yonse.”
8 Car ainsi dit le Seigneur, qui rassemble les fils dispersés d'Israël: Je rassemblerai près d'Israël une nouvelle synagogue.
Ambuye Yehova, amene amasonkhanitsa Aisraeli onse ali ku ukapolo akunena kuti, “Ndidzasonkhanitsano anthu ena kuwonjezera amene anasonkhana kale.”
9 Et vous, bêtes fauves des champs, venez; bêtes fauves de la forêt, dévorez.
Bwerani, inu zirombo zonse zakuthengo, inu nonse zirombo zamʼnkhalango bwerani mudzadye!
10 Voyez comme ils sont tous aveuglés; ils ne connaissent rien; ce sont des chiens muets; ils ne peuvent pas aboyer, ils sont endormis sur leurs couches, ils n'aiment qu'à sommeiller.
Atsogoleri onse a Israeli ndi akhungu, onse ndi opanda nzeru; onse ndi agalu opanda mawu, samatha kuwuwa: amagona pansi nʼkumalota amakonda kugona tulo.
11 Ce sont des chiens impudents en leur âme, ils ne savent ce que c'est que d'être rassasiés. Ils sont méchants et sans intelligence; ils ont suivi toutes leurs voies, chacun à son gré.
Ali ngati agalu amene ali ndi njala yayikulu; sakhuta konse. Abusa nawonso samvetsa zinthu; onse amachita monga akufunira, aliyense amafunafuna zomupindulitsa iye mwini.
Aliyense amafuwulira mnzake kuti, “Bwera, tiye timwe vinyo! Tiyeni timwe mowa mpaka kukhuta! Mawa lidzakhala ngati leroli, kapena kuposa lero lino.”

< Isaïe 56 >