< Isaïe 55 >

1 Vous qui êtes altérés, venez à l'eau; vous qui n'avez point d'argent, allez et achetez; sans argent et sans échange, nourrissez-vous de graisse et de vin.
“Bwerani, inu nonse amene muli ndi ludzu, bwerani madzi alipo; ndipo inu amene mulibe ndalama bwerani, mudzagule chakudya kuti mudye! Bwerani mudzagule vinyo ndi mkaka osalipira ndalama, osalipira chilichonse.
2 Pourquoi faites-vous cas de l'argent et vous fatiguez-vous pour ce qui ne rassasie pas? Écoutez-moi, et vous mangerez ce qui est vraiment bon; et votre âme se délectera des vrais biens.
Chifukwa chiyani ndalama zanu mukuwonongera zinthu zimene samadya, ndipo mukuwononga malipiro anu pa zinthu zimene sizikhutitsa? Tamverani, mvetsetsani zimene ndikunena kuti mudye zimene zili zabwino; ndipo mudzisangalatse.
3 Prêtez-moi des oreilles attentives, et suivez mes voies; écoutez-moi, et votre âme vivra des vrais biens, et je ferai avec vous une alliance éternelle, et les promesses faites à David seront vérifiées.
Tcherani makutu ndipo mubwere kwa Ine; mvereni Ine, kuti mukhale ndi moyo. Ndidzachita nanu pangano losatha, chikondi changa chija chosasinthika ndi chodalirika ndinalonjeza Davide.
4 Voilà que j'ai donné aux nations un témoignage; c'est lui, le prince, le maître des Gentils.
Taonani, ine ndamusankha kuti akhale mboni yanga kwa mitundu ya anthu, kuti akhale mtsogoleri ndi wolamulira mitundu ya anthu.
5 Des nations qui ne te connaissaient pas t'invoqueront, et des peuples à qui tu étais inconnu se réfugieront auprès de toi, à cause du Seigneur ton Dieu, le Saint d'Israël, parce qu'il t'aura glorifié.
Ndithu inu mudzayitanitsa mitundu ya anthu imene simuyidziwa, ndipo mitundu ya anthu imene sikudziwani idzabwera ndi liwiro kwa inu. Izi zidzatero chifukwa Yehova Mulungu wanu, Woyerayo wa Israeli, wakuvekani ulemerero.”
6 Cherchez le Seigneur, et, quand vous l'aurez trouvé, invoquez-le. Et lorsqu'il sera près de vous,
Funafunani Yehova pamene Iye akupezeka. Mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi.
7 Que l'impie quitte ses voies, et le prévaricateur ses conseils; qu'il se convertisse au Seigneur, et il lui sera fait miséricorde, parce qu'il vous remettra beaucoup de péchés.
Woyipa asiye makhalidwe ake oyipa, ndipo wosalungama asinthe maganizo ake oyipa. Abwerere kwa Yehova, ndipo adzamuchitira chifundo, ndi kwa Mulungu wathu, pakuti adzamukhululukira koposa.
8 Car mes conseils ne sont pas comme vos conseils, ni mes voies comme vos voies, dit le Seigneur.
“Pakuti maganizo anga siwofanana ndi maganizo anu, ngakhale njira zanu si njira zanga,” akutero Yehova.
9 Mais autant le ciel est loin de la terre, autant ma voie est loin de vos voies, et vos pensées, loin de ma pensée.
“Monga momwe mlengalenga muli kutali ndi dziko lapansi, momwemonso zochita zanga nʼzolekana kutali ndi zochita zanu, ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.
10 Car telle la pluie ou la neige descend du ciel et n'y retournera point avant d'avoir abreuvé la terre et humecté les champs; avant d'avoir produit des graines pour le semeur, et donné du pain pour sa nourriture;
Monga mvula ndi chisanu chowundana zimatsika kuchokera kumwamba, ndipo sizibwerera komweko koma zimathirira dziko lapansi. Ndipo zimameretsa ndi kukulitsa zomera kenaka nʼkupatsa mlimi mbewu ndi chakudya.
11 Telle sera ma parole; toute parole qui sortira de ma bouche ne reviendra point à moi que mes volontés ne soient accomplies; et je ferai prospérer tes voies, et mes ordres auront leur effet.
Ndi mmenenso amachitira mawu ochokera mʼkamwa mwanga. Sadzabwerera kwa Ine kopanda phindu lake, koma adzachita zonse zimene ndifuna, ndipo adzakwaniritsa cholinga chimene ndinawatumira.
12 Car vous sortirez pleins d'allégresse, et vous serez enseignés dans la joie. Les montagnes et les collines bondiront de joie pour votre bienvenue, et les arbres de la plaine vous applaudiront du bruit de leurs rameaux.
Inu mudzatuluka mu mzindawo mwachimwemwe ndipo adzakutsogolerani mwamtendere; mapiri ndi zitunda zidzakuyimbirani nyimbo, ndipo mitengo yonse yamʼthengo idzakuwombereni mʼmanja.
13 Où croissaient la mousse et les épines, s'élèveront le myrte et le cyprès. Et le nom du Seigneur sera proclamé, et ce sera un signe éternel, et il ne disparaîtra jamais.
Mʼmalo mʼmene tsopano muli mitengo ya minga mudzamera mitengo ya payini, ndipo kumene kuli mkandankhuku kudzamera mchisu. Zimenezi zidzakhala chikumbutso cha Yehova, ngati chizindikiro chamuyaya, chimene sichidzafafanizika konse.”

< Isaïe 55 >