< Isaïe 53 >

1 Mais, Seigneur, qui a cru à notre parole? A qui le bras du Seigneur a-t- il été révélé?
Ndani wakhulupirira zimene tanenazi; kapena ndani amene Yehova wamuzindikiritsa mphamvu zake?
2 Nous l'avons annoncé, comme un petit enfant devant le Seigneur, comme une racine dans une terre altérée; il n'est point en lui de beauté ni de gloire; nous l'avons vu, et il n'avait ni éclat ni beauté.
Iye anakula ngati mphukira pamaso pake, ndiponso ngati muzu mʼnthaka yowuma. Iye analibe thupi labwino kapena nkhope yokongola yoti ife nʼkumamuchewukira, analibe maonekedwe woti ife nʼkumamukhumbira.
3 Mais son aspect était méprisable, au-dessous de celui des fils des hommes. C'était un homme couvert de plaies, et sachant ce que c'est que la souffrance; car son visage était repoussant, sans honneur, et compté pour rien.
Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu, munthu amene moyo wake unali wamasautso, wozolowera zowawa, ndipo anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona. Iye ananyozedwa, ndipo ife sitinamuyese kanthu.
4 Il porte nos péchés, il souffre pour nous; et nous avons remarqué qu'il était dans la peine, dans la douleur, dans la torture.
Ndithudi, iye anamva zowawa mʼmalo mwa ife; ndipo anasautsidwa mʼmalo mwathu. Koma ife tinkaganiza kuti ndi Mulungu amene akumulanga, kumukantha ndi kumusautsa.
5 Mais il avait été blessé pour nos péchés, il était brisé pour nos crimes; le châtiment qui devait nous rendre la paix est tombé sur lui; nous avons été guéris par ses meurtrissures.
Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu, ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu; iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere, ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.
6 Nous étions égarés comme des brebis; tout homme errait dans sa voie. Et le Seigneur l'a livré pour nos péchés;
Ife tonse, ngati nkhosa, tasochera, aliyense mwa ife akungodziyendera; ndipo Yehova wamusenzetsa zoyipa zathu zonse.
7 Et lui, si fort qu'on l'ait maltraité, il n'ouvre pas la bouche. Il a été conduit sous le couteau comme une brebis; et comme l'agneau muet devant le tondeur, ainsi il n'ouvre pas la bouche.
Anthu anamuzunza ndi kumusautsa, koma sanayankhule kanthu. Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira, kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta, momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
8 Tout jugement lui a été enlevé en son humiliation. Qui racontera sa génération? car sa vie est effacée de la terre; il a été conduit à la mort à cause des péchés de mon peuple.
Atatha kumugwira mwankhanza ndikumuyimba mlandu, kenaka anapita naye kukamupha. Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake, poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo? Ndani anaganizirapo poona kuti iye anakanthidwa chifukwa cha zolakwa za anthu anga?
9 Je donnerai les méchants pour prix de sa sépulture, et les riches pour prix de sa mort; parce qu'il n'a point commis de péchés, et que le mensonge n'a jamais été dans sa bouche.
Anamukonzera manda ake pamodzi ndi anthu oyipa ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi anthu achuma, ngakhale kuti iye sanachite za chiwawa, kapena kuyankhula za chinyengo.
10 Et il a plu au Seigneur de le purifier par l'effet de sa souffrance. Si vous faites une offrande, pour vos péchés, votre vie verra une postérité qui vivra longtemps. Et il a plu au Seigneur d'effacer
Komatu ndi Yehova amene anafuna kuti amuzunze ndi kumusautsa. Yehova anapereka moyo wa mtumiki wake kuti ukhale nsembe yoperekedwa chifukwa cha zolakwa. Tsono iye adzaona zidzukulu zake ndipo adzakhala ndi moyo wautali, ndipo chifuniro cha Yehova chidzachitika mwa iye.
11 Une part des douleurs de son âme, de lui montrer la lumière, de la former à l'intelligence, de justifier le Juste qui s'est sacrifié pour un grand nombre, et qui a porté leurs péchés.
Atatha mazunzo a moyo wake, adzaona kuwala, ndipo adzakhutira. Mwa nzeru zake mtumiki wanga wolungamayo adzalungamitsa anthu ambiri, popeza adzasenza zolakwa zawo.
12 C'est pourquoi il aura pour héritage une grande multitude; il partagera les dépouilles des forts, en récompense de ce que sa vie aura été livrée au supplice, qu'il aura été regardé comme un pécheur, qu'il aura porté sur lui les péchés de beaucoup d'hommes, et que, pour leurs iniquités, il aura été livré à la mort.
Motero Ine ndidzamupatsa ulemu pamodzi ndi akuluakulu, adzagawana zofunkha ndi ankhondo amphamvu, popeza anapereka moyo wake mpaka kufa, ndipo anamuyika mʼgulu la anthu olakwa kuti akhululukidwe. Pakuti iye anasenza machimo a anthu ambiri, ndipo anawapempherera anthu olakwa.

< Isaïe 53 >