< Isaïe 51 >

1 Pour vous, écoutez-moi, vous qui suivez la justice et qui cherchez le Seigneur. Regardez la roche solide que vous avez taillée, et le fond de la source que vous avez creusée.
“Mverani Ine, inu amene mukufuna chipulumutso ndiponso amene mumafunafuna Yehova: Taganizani za thanthwe kumene munasemedwa ndipo ku ngwenya kumene anakukumbani;
2 Regardez Abraham votre père, et Sara qui vous a enfantés dans la douleur; car il était unique, et je l'ai appelé, je l'ai béni, je l'ai chéri et multiplié.
taganizani za Abrahamu, kholo lanu, ndi Sara, amene anakubalani. Pamene ndinkamuyitana nʼkuti alibe mwana, koma ndinamudalitsa ndi kumupatsa ana ambiri.
3 De même, je vais maintenant te consoler, ô Sion; j'ai déjà consolé toutes ses solitudes, je changerai ses déserts en jardins, et ceux qui s'étendent au couchant seront comme le paradis du Seigneur; en elle on trouvera joie et allégresse, actions de grâces et paroles de louanges.
Yehova adzatonthozadi Ziyoni, ndipo adzachitira chifundo mabwinja ake onse; Dziko lake la chipululu adzalisandutsa ngati Edeni, malo ake owuma ngati munda wa Yehova. Anthu adzayimba nyimbo zonditamanda ndi kundiyamika.
4 Écoutez-moi, mon peuple, écoutez-moi, et vous, rois, prêtez-moi une oreille attentive; car la loi sortira de moi, et ma justice sera la lumière des nations.
“Mverani Ine, anthu anga: tcherani khutu, inu mtundu wanga: malangizo adzachokera kwa Ine; cholungama changa chidzawunikira anthu a mitundu yonse.
5 Elle est proche ma justice, et mon salut va se lever comme une lumière; et les Gentils espèreront en mon bras; les îles m'attendront et elles espèreront aussi en mon bras.
Ndili pafupi kubwera kudzawombola anthu anga. Ndidzabwera mofulumira ngati kuwunika kudzapulumutsa anthu anga; ndipo ndidzalamulira anthu a mitundu yonse. Mayiko akutali akundiyembekezera. Iwo akudikira kuti ndidzawapulumutse.
6 Levez les yeux au ciel, et regardez au-dessous la terre; le ciel n'est pas plus solide que la fumée, la terre vieillira comme un manteau, et comme eux mourront ceux qui l'habitent; mais mon salut subsistera durant tous les siècles, et ma justice ne défaillira point.
Kwezani maso anu mlengalenga, yangʼanani pansi pa dziko; mlengalenga udzazimirira ngati utsi, dziko lapansi lidzatha ngati chovala ndipo anthu ake adzafa ngati nsabwe. Koma chipulumutso changa chidzakhala mpaka muyaya, chilungamo changa chidzakhala cha nthawi zonse.
7 Écoutez-moi, vous qui connaissez le jugement, et vous, mon peuple, qui conservez ma loi dans votre cœur. Ne craignez pas les outrages des hommes; ne soyez pas abattus par leur mépris;
“Mverani Ine, inu amene mukudziwa choonadi, anthu inu amene mukusunga malangizo anga mʼmitima yanu; musaope kudzudzulidwa ndi anthu kapena kuopsezedwa akamakulalatirani.
8 Car ils seront consumés comme un manteau par l'effet du temps; ils seront rongés des vers comme de la laine; mais ma justice subsistera dans tous les siècles, et mon salut durant les générations des générations.
Pakuti njenjete idzawadya ngati chovala; mbozi idzawadya ngati thonje. Koma chilungamo changa chidzakhala mpaka muyaya, chipulumutso changa chidzakhala mpaka mibadomibado.”
9 Réveille-toi, réveille-toi, Jérusalem, arme de force ton bras; réveille- toi comme au commencement des jours, comme les antiques générations. N'es-tu pas
Dzambatukani, dzambatukani! Valani zilimbe, Inu Yehova; dzambatukani, monga munkachitira masiku amakedzana, monga nthawi ya mibado yakale. Si ndinu kodi amene munaduladula Rahabe, amene munabaya chinjoka cha mʼnyanja chija?
10 Celle qui a desséché la mer et la plénitude des eaux de l'abîme? N'as-tu pas fait du fond de la mer une voie pour le passage de mon peuple délivré
Kodi sindinu amene munawumitsa nyanja yayikulu, madzi ozama kwambiri aja? Kodi sindinu amene munapanga njira pa madzi ozama, kuti anthu amene munawapulumutsa awoloke powuma?
11 Et racheté? Car tes enfants seront ramenés par le Seigneur, et ils reviendront dans Sion pleins d'une joie et d'une allégresse éternelle; ils seront couronnés de louanges et transportés de joie; les douleurs, la tristesse, les gémissements se sont enfuis.
Anthu amene Yehova anawawombola adzabwerera nakafika ku Ziyoni nyimbo ili pakamwa; chimwemwe chamuyaya chizidzaonekera pa nkhope zawo. Adzakhala ndi chikondwerero ndi chimwemwe, chisoni ndi kubuwula zidzathawa.
12 C'est moi, c'est moi ton consolateur; sache qui tu es, et si tu devais craindre un homme mortel, un fils de l'homme, qui sèchera comme l'herbe des champs.
Yehova akuti, “Ndinetu amene ndimakutonthozani mtima. Chifukwa chiyani mukuopa munthu woti adzafa? Mukuopa munthu woti monga udzu sadzakhalitsa.
13 Et tu avais oublié Dieu ton créateur, le créateur du ciel et de la terre; et tous les jours tu avais peur en voyant en face la furie de ton persécuteur! Il a péri comme il avait résolu de te faire périr; et la furie de ton persécuteur, où est-elle à présent?
Koma inu mumayiwala Yehova Mlengi wanu, amene anayala za mlengalenga ndi kuyika maziko a dziko lapansi. Inu nthawi zonse mumaopsezedwa chifukwa cha ukali wa anthu okuponderezani amene angofuna kukuwonongani. Kodi uli kuti tsopano ukali wa anthu okuponderezaniwo?
14 Le Seigneur ne s'arrêtera point, il ne mettra point de lenteur à te sauver.
Amʼndende adzamasulidwa posachedwa; sadzalowa mʼmanda awo, kapena kusowa chakudya.
15 Car je suis ton Dieu; c'est moi qui trouble la mer, et qui fais retentir ses flots. Mon nom est le Seigneur des armées.
Pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndimavundula nyanja kotero mafunde ake amakokoma. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
16 Je mettrai mes paroles en ta bouche; je t'abriterai à l'ombre de ma main, qui a fixé le ciel et affermi la terre, et je dirai à Sion: Tu es mon peuple.
Ndayika mawu anga mʼkamwa mwanu ndipo ndakuphimbani ndi mthunzi wa dzanja langa. Ine ndimayika pa malo pake zinthu za mlengalenga, ndipo ndinayika maziko a dziko lapansi, ndimawuza anthu a ku Ziyoni kuti, ‘Ndinu anthu anga.’”
17 Réveille-toi, réveille-toi, lève-toi, Jérusalem, qui as bu de la main du Seigneur le calice de sa colère. Car tu as bu, tu as épuisé le calice de la ruine, la grande coupe de la fureur.
Dzambatuka, dzambatuka! Imirira iwe Yerusalemu. Iwe amene wamwa chikho cha mkwiyo chimene Yehova anakupatsa. Iwe amene unagugudiza chikho chochititsa chizwezwe.
18 Et de tous les enfants que tu as mis au jour, nul ne t'a consolée; et de tous les fils que tu as élevés, nul ne t'a prise par la main.
Mwa ana onse amene anabereka, panalibe ndi mmodzi yemwe anamutsogolera; mwa ana onse amene analera, panalibe ndi mmodzi yemwe anamugwira dzanja.
19 Quand ces choses fondront sur toi, qui partagera ta tristesse? Quand il y aura ruine et désolation, famine et coups de glaive, qui te consolera?
Mavuto awiriwa akugwera iwe. Dziko lako lasakazika ndi kuwonongeka. Anthu afa ndi njala ndi lupanga. Ndani angakumvere chisoni? Ndani angakutonthoze?
20 Tes fils ont été pressés par la détresse, couchés au bout de chaque rue, comme une blette à demi cuite, pleins de la colère du Seigneur, énervés par le Seigneur Dieu.
Ana ako akomoka; ali lambalamba pa msewu, ngati mphoyo yogwidwa mu ukonde. Ukali wa Yehova ndi chidzudzulo chake zidzawagwera.
21 C'est pourquoi, écoute, ô toi qui es humiliée et enivrée, mais non de vin:
Nʼchifukwa chake imva izi iwe amene ukuvutika, iwe amene waledzera, koma osati ndi vinyo.
22 Ainsi dit le Seigneur Dieu, juge de son peuple: Voilà que j'ai ôté de tes mains le calice de la ruine, la grande coupe de ma fureur; tu ne continueras plus d'y boire à l'avenir.
Ambuye Yehova wanu, Mulungu amene amateteza anthu ake akuti, “Taona, ndachotsa mʼdzanja lako chikho chimene chimakuchititsa kudzandira; sudzamwanso chikho cha ukali wanga.
23 Je la mettrai dans les mains de ceux qui t'ont nui injustement, de ceux qui t'ont abaissée, de ceux qui disaient à ton âme: Couche-toi, afin que nous passions; et tu faisais de ton corps un chemin pour ceux qui passaient.
Ndidzapereka chikhocho kwa anthu amene amakuzunza, amene ankakuwuza kuti, ‘gona pansi tikuyende pa msana.’ Ndipo msana wako anawuyesa pansi popondapo, ngati msewu woti ayendepo.”

< Isaïe 51 >