< Isaïe 46 >

1 Bel est tombé, Nabo a été brisé, leurs statues sont comme des bêtes fauves, comme des bêtes de somme; enlevez-les, attachés comme la charge d'un homme de peine.
Beli wagwada pansi, Nebo wawerama; nyama zonyamula katundu za nyamula milungu yawo. Mafano awo asanduka katundu wolemera pa msana pa ngʼombe. Asandukadi ngati katundu pa msana pa nyama zotopa.
2 Accablés, affamés, sans force, ils n'ont pu se sauver de la guerre; ils ont été emmenés captifs.
Nyamazo zikuwerama ndi kufuna kugwa ndi milunguyo; sizikutha kupulumutsa katunduyo, izo zomwe zikupita ku ukapolo.
3 Écoutez-moi, maison de Jacob, et vous tous, restes d'Israël, vous que je porte depuis que vous êtes sortis des entrailles de votre mère, vous que j'instruis depuis votre enfance
Mverani Ine, Inu nyumba ya Yakobo, inu nonse otsala a mʼnyumba ya Israeli, Ine ndakhala ndi kukusamalirani kuyambira mʼmimba ya amayi anu, ndakhala ndikukunyamulani chibadwire chanu.
4 Jusqu'à la vieillesse. Je suis, et jusqu'à ce que vous soyez parvenus à l'extrême vieillesse, je suis; je vous porte, c'est moi qui vous ai créés, c'est moi qui vous soutiendrai; je vous porterai et je vous sauverai.
Mpaka pamene mudzakalambe ndi kumera imvi ndidzakusamalirani ndithu. Ndinakulengani ndipo ndidzakunyamulani, ndidzakusamalirani ndi kukulanditsani.
5 A qui me comparerez-vous? Voyez, imaginez, vous qui vivez dans l'erreur;
“Kodi inu mudzandifanizira ndi yani, kapena mufananitsa ndi yani? Kodi mudzandiyerekeza kapena kundifanizitsa ndi yani?
6 Vous qui accumulez de l'or dans un sac et de l'argent dans une balance; et ils en ont pesé une part, ils ont payé un fondeur, puis ils feront une idole, et, s'étant prosternés, ils l'adoreront;
Anthu ena amakhuthula golide mʼzikwama zawo ndipo amayeza siliva pa masikelo; amalemba ntchito mʼmisiri wosula kuti awapangire mulungu, kenaka iwo amagwada pansi ndikupembedza kamulunguko.
7 Ils la porteront sur leurs épaules, et se mettront en marche; et s'ils la placent en son lieu, elle y demeurera et ne pourra en bouger. Et celui qui l'invoquera, elle ne pourra l'entendre ni le préserver du mal.
Amanyamula nʼkumayenda nayo milunguyo pa mapewa awo; amayikhazika pa malo pake ndipo imakhala pomwepo. Singathe kusuntha pamalo pakepo. Ngakhale wina apemphere kwa milunguyo singathe kuyankha; kapena kumupulumutsa ku mavuto ake.
8 Rappelez-vous ces choses, et gémissez; repentez-vous, ô vous qui êtes égarés; convertissez-vous en vos cœurs;
“Kumbukirani zimenezi ndipo muchite manyazi, Muzilingalire mu mtima, inu anthu owukira.
9 Et souvenez-vous des premiers âges, des âges d'autrefois; souvenez-vous que je suis Dieu, et qu'il n'en est point, hormis moi;
Kumbukirani zinthu zakale zinthu zamakedzana; chifukwa Ine ndine Mulungu ndipo palibe wina ofanana nane.
10 Moi qui annonce les choses de la fin avant qu'elles soient, et déjà elles sont accomplies. Et j'ai dit: Tous mes conseils seront stables, et tout ce que j'ai résolu, je le ferai.
Ndinaneneratu zakumathero kuchokera pachiyambi pomwe. Kuyambira nthawi yamakedzana ndinaloseratu zoti zidzachitike. Ndikanena zimene ndifuna kuchita ndipo zimachitikadi. Chilichonse chimene ndafuna ndimachichita.
11 J'ai appelé un prince ailé de l'Orient, et d'une contrée lointaine, pour accomplir les choses que j'ai résolues; je lui ai parlé, je l'ai amené, je l'ai créé et formé, je l'ai conduit, et je l'ai mis dans la bonne voie.
Ndikuyitana chiwombankhanga kuchokera kummawa. Ndikuyitana kuchokera ku dziko lakutali munthu amene adzakwaniritsa cholinga changa. Zimene ndanena ndidzazikwaniritsadi; zimene ndafuna ndidzazichitadi.
12 Écoutez-moi, vous dont le cœur est perverti, vous qui vous êtes éloignés de la justice.
Ndimvereni, inu anthu owuma mtima, inu amene muli kutali ndi chipulumutso.
13 Ma justice est proche, et le salut qui viendra de moi ne sera pas différé. J'ai donné dans Sion le salut à Israël pour ma glorification.
Ndikubweretsa pafupi tsiku la chipulumutso changa; sichili kutali. Tsikulo layandikira ndipo sindidzachedwa kukupulumutsani ndi kupereka ulemerero wanga kwa Israeli.

< Isaïe 46 >