< Isaïe 45 >

1 Voici ce que dit le Seigneur Dieu: J'ai dit à mon christ Cyrus que j'ai pris par la main, avant que les nations lui obéissent: Je briserai la force des rois; j'ouvrirai devant toi les portes, et les villes ne te seront pas fermées.
Yehova akuyankhula ndi wodzozedwa wake Koresi amene anamugwira dzanja lamanja kuti agonjetse mitundu ya anthu ndi kuwalanda mafumu zida zawo zankhondo, ndi kutsekula zitseko kuti zipatazo zisadzatsekedwenso ndi ichi:
2 Je marcherai devant toi; j'aplanirai les montagnes; je briserai les portes d'airain; je broierai les verrous de fer.
Ine ndidzayenda patsogolo pako, ndi kusalaza mapiri; ndidzaphwanya zitseko za mkuwa ndi kuthyola mipiringidzo ya chitsulo.
3 Je te donnerai des trésors enfouis dans les ténèbres; j'ouvrirai pour toi les retraites cachées, invisibles; afin que tu saches que je suis le Seigneur ton Dieu, qui t'appelle par ton nom, le Dieu d'Israël.
Ndidzakupatsa chuma chobisika mu mdima, katundu wa pamalo obisika, kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wa Israeli, amene ndakuyitana pokutchula dzina.
4 A cause de mon serviteur Jacob, à cause de mon élu Israël, je t'appellerai par ton nom, et je t'agréerai, toi qui cependant ne m'as pas connu.
Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo, chifukwa cha wosankhidwa wanga Israeli, Ine ndakuyitana pokutchula dzina ndipo ndakupatsa dzina laulemu ngakhale iwe sukundidziwa Ine.
5 Je suis le Seigneur Dieu; et, hormis moi, il n'y a point de Dieu; je t'ai fortifié, et tu ne me connaissais pas.
Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina; kupatula Ine palibenso Mulungu wina. Ndidzakupatsa mphamvu, ngakhale sukundidziwa Ine,
6 Je t'ai fortifié pour que du lever au coucher du soleil on sache qu'il n'y a point de Dieu, hormis moi. Je suis le Seigneur Dieu, et il n'en n'est point d'autre.
kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzulo anthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha. Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
7 C'est moi qui ai préparé la lumière, qui ai formé les ténèbres, qui fais la paix, qui crée les maux; je suis le Seigneur Dieu, qui fais toutes ces choses.
Ndimalenga kuwala ndi mdima, ndimabweretsa madalitso ndi tsoka; ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi.
8 Que du plus haut le ciel se réjouisse; que les nuées répandent la justice comme une rosée. Que la terre produise, qu'elle fasse naître la miséricorde et qu'elle produise en même temps la justice. Moi je suis le Seigneur qui t'ai créé.
“Iwe thambo gwetsa mvula kuchokera kumwamba; mitambo ivumbwe mivumbi ya chilungamo. Dziko lapansi litsekuke, ndipo chipulumutso chiphuke kuti chilungamo chimereponso; Ine Yehova, ndine ndalenga zimenezi.
9 Ai-je fait l'argile supérieure au potier? Le laboureur laboure-t-il tout un jour? L'argile dit-elle au potier: Que fais-tu? tu ne travailles pas; n'as-tu pas des mains? Est-ce que l'œuvre parle à l'ouvrier?
“Tsoka kwa wokangana ndi mlengi wake, ngakhale kuti ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake. Kodi dongo lingafunse munthu wowumba kuti, ‘Kodi ukuwumba chiyani?’ Kodi ntchito yako inganene kuti, ‘Ulibe luso?’
10 C'est comme si on disait à son père: Pourquoi engendrez-vous? et à sa mère: Pourquoi enfantez-vous?
Tsoka kwa wofunsa abambo ake kuti, ‘Kodi munabereka chiyani?’ Kapena amayi ake kuti, ‘Kodi mufuna kubereka chiyani?’
11 Voici ce que dit le Seigneur, le Saint d'Israël, le créateur des choses futures: Questionnez-moi sur mes fils; demandez-moi compte des œuvres de mes mains.
“Yehova Woyerayo wa Israeli, ndiponso Mlengi wake akunena, zokhudza zinthu zimene zikubwera ndi izi: Kodi iwe ukundifunsa za ana anga, kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga?
12 C'est moi qui ai créé la terre, et l'homme sur elle; moi qui de ma main ai affermi le ciel; moi qui ai donné des lois à tous les astres.
Ndine amene ndinapanga dziko lapansi ndikulenga munthu kuti akhalemo. Ine ndi manja anga ndinayalika thambo; ndimalamulira zolengedwa zonse za mlengalenga.
13 C'est moi qui l'ai suscité; il sera roi selon la justice; toutes ses voies seront droites; il rebâtira ma ville; il fera revenir mon peuple de la captivité, sans rançons, sans présents, dit le Seigneur des armées.
Ndine amene ndidzawutsa Koresi kuti chilungamo changa chikwaniritsidwe: ndipo ndidzawongolera njira zake zonse. Iye adzamanganso mzinda wanga ndi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo, wopanda kupereka ndalama kapena mphotho, akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
14 Voici ce que dit le Seigneur des armées: l'Égypte a travaillé pour toi; les marchandises des Éthiopiens et des hommes superbes de Saba traverseront la mer pour venir te trouver; ils te seront asservis; ils te suivront les fers aux mains, ils t'aborderont, ils se prosterneront devant toi, et t'adresseront leurs prières, parce que Dieu est avec toi. Et, hormis vous, Seigneur, il n'est point de Dieu.
Yehova akuti, “Chuma cha ku Igupto ndi chuma cha malonda cha Kusi chidzakhala chanu. Anthu amphamvu zawo ndi athanzi a ku Seba adzabwera kwa inu ndipo adzakhala anthu anu; iwo adzidzakutsatani pambuyo panu ali mʼmaunyolo. Adzakugwadirani ndi kukupemphani, ponena kuti, ‘Ndithudi Mulungu ali ndi inu, ndipo palibenso wina; palibenso mulungu wina.’”
15 Car vous êtes Dieu, et nous ne le savions pas, Dieu d'Israël, Dieu Sauveur!
Zoonadi inu muli ndi Mulungu wobisika amene ali Mulungu ndi Mpulumutsi wa Israeli.
16 Que tous tes adversaires soient humiliés, qu'ils rougissent, qu'ils marchent pleins de honte. Et vous, célébrez des solennités en mon honneur.
Onse amene amapanga mafano adzawachititsa manyazi ndi kuwanyozetsa. Adzakhala osokonezeka maganizo.
17 Israël est sauvé par le Seigneur, sauvé pour tous les siècles; ses enfants ne seront plus humiliés ni confondus à jamais.
Koma Yehova adzapulumutsa Israeli ndi chipulumutso chamuyaya; simudzachitanso manyazi kapena kunyozeka mpaka kalekale.
18 Ainsi dit le Seigneur qui a créé le ciel, le Dieu qui a fait paraître la terre, qui l'a créée, qui lui a donné ses limites; et il ne l'a point formée en vain, mais pour qu'elle fût habitée. Je suis le Seigneur, et il n'en est point d'autre.
Yehova analenga zinthu zakumwamba, Iye ndiye Mulungu; amene akulenga dziko lapansi, ndi kulikhazikitsa, sanalipange kuti likhale lopanda kanthu, koma analipanga kuti anthu akhalemo. Iyeyu akunena kuti: Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
19 Je n'ai point parlé en secret, ni dans quelque lieu obscur de la terre; je n'ai point dit à la race de Jacob: En vain cherchez-vous; c'est moi, c'est moi le Seigneur qui parle selon la justice, qui annonce la vérité.
Ine sindinayankhule mwachinsinsi, pamalo ena a mdima; Ine sindinaziwuze zidzukulu za Yakobo kuti, “Ndifunefuneni ku malo kopanda kanthu.” Ine Yehova, ndimayankhula zoona; ndikunena zolungama.
20 Rassemblez-vous, venez, prenez conseil ensemble, vous qui avez été sauvés des nations qui élevaient des sculptures et des statues de bois, qui vivaient dans l'ignorance et priaient des dieux incapables de sauver.
Yehova akuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere; yandikirani, inu amene munapulumuka pothawa nkhondo kwa anthu a mitundu ina. Ndinu opanda nzeru amene mumanyamula mafano a mitengo, amene mumapemphera kwa milungu imene singathe kupulumutsa.
21 Si elles ont quelque chose à dire, qu'elles approchent, afin d'apprendre toutes à la fois qui a fait connaître ces choses; vous les avez sues dès lors, vous avez su que je suis Dieu; il n'en est point d'autre que moi; je suis le Dieu juste et sauveur; il n'en est point, hormis moi.
Fotokozani mlandu wanu, mupatsane nzeru nonse pamodzi. Kodi ndani ananeneratu zimenezi kalekale? Ndani anazifotokozeratu zimenezi nthawi yamakedzana? Kodi si Ineyo Yehova? Ndipo palibenso Mulungu wina kupatula Ine, Mulungu wolungama ndi Wopulumutsa, palibenso wina kupatula Ine.
22 Convertissez-vous à moi, et vous serez sauvés, ô vous qui venez des extrémités de la terre. C'est moi qui suis Dieu, et il n'en est point d'autre.
“Tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke, inu anthu onse a pa dziko lapansi, pakuti Ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.
23 Je le jure par moi-même, la justice seule va sortir de ma bouche, et ma parole ne sera pas vaine. Tout genou fléchira devant moi; toute langue confessera Dieu,
Ndalumbira ndekha, pakamwa panga patulutsa mawu owona, mawu amene sadzasinthika konse akuti, bondo lililonse lidzagwada pamaso panga; anthu onse adzalumbira potchula dzina langa.
24 Disant: La justice et la gloire viendront à lui, et tous ceux qui se séparent du Seigneur seront confondus.
Iwo adzanene kwa Ine kuti, ‘Chilungamo ndi mphamvu zimapezeka mwa Yehova yekha.’” Onse amene anamuwukira Iye adzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi.
25 Et les autres seront justifiés, et toute la postérité des fils d'Israël mettra sa gloire en Dieu.
Koma mwa Yehova zidzukulu zonse za Israeli zidzapambana ndi kupeza ulemerero.

< Isaïe 45 >