< Isaïe 42 >
1 Jacob mon serviteur, je te protègerai; Israël est mon élu, mon âme l'a agréé; j'ai répandu sur lui mon esprit, et il révèlera mon jugement aux nations.
“Nayu mtumiki wanga, amene ndimamuchirikiza, amene ndamusankha, amenenso ndimakondwera naye. Ndayika Mzimu wanga mwa Iyeyo, ndipo adzaweruza anthu a mitundu yonse mwachilungamo.
2 Il ne criera pas, il ne faiblira pas; sa voix au dehors ne sera pas entendue.
Iye sadzafuwula, sadzamveka mawu, kapena mawu ake kumveka mʼmisewu.
3 Il ne broiera pas le roseau déjà brisé; il n'éteindra pas la mèche qui fume encore; mais il révèlera le jugement selon la vérité.
Bango lophwanyika sadzalithyola, ndipo moto wozilala sadzawuzimitsa. Motero adzaonetsa kuti chilungamo ndicho choonadi;
4 Il brillera et ne sera point détruit jusqu'à ce qu'il ait placé le jugement sur la terre, et les Gentils mettront leur espérance en son nom.
sadzafowoka kapena kukhumudwa mpaka atakhazikitsa chilungamo pa dziko lapansi, ndi mpaka mayiko a mʼmbali mwa nyanja atafika poyembekezera malangizo ake.”
5 Ainsi dit le Seigneur Dieu, qui a créé le ciel et l'a tendu, qui a affermi la terre et tout ce qu'elle contient, qui a donné le souffle au peuple qui l'habite, et la vie à ceux qui y marchent.
Yehova Mulungu amene analenga zamlengalenga ndi kuziyalika, amene analenga dziko lapansi ndi zonse zimene zimabereka, amenenso amapereka mpweya kwa anthu ake okhala mʼdzikomo, ndi moyo kwa onse oyendamo, akuti,
6 Moi, le Seigneur Dieu, je t'ai appelé avec justice, et je te prendrai par la main, et je te fortifierai, et je t'ai donné d'être l'alliance du genre humain et la lumière des nations;
“Ine Yehova, ndakuyitana chifukwa Ine ndine wolungama; ndikugwira dzanja ndipo ndidzakuteteza. Ndakupereka kukhala pangano langa kwa anthu ndi kuwunika kwa anthu a mitundu ina.
7 D'ouvrir les yeux aux aveugles, de tirer de la prison les captifs enchaînés et assis dans les ténèbres.
Udzatsekula maso a anthu osaona, udzamasula anthu a mʼndende ndi kutulutsa mʼndende anthu okhala mu mdima.
8 Je suis le Seigneur Dieu, c'est mon nom; je ne donnerai pas ma gloire à un autre, ni mes vertus à des idoles d'argile.
“Ine ndine Yehova: dzina langa ndi limenelo! Sindidzapereka ulemerero wanga kwa wina aliyense kapena matamando anga kwa mafano.
9 Voilà que les choses du commencement sont venues, comme viendront les choses nouvelles que je vous annonce, et qui, avant que je les annonce, vous ont été prédites.
Taonani, zinthu zimene ndinalosera kale zachitikadi, ndipo ndikuwuzani zinthu zatsopano; zinthuzo zisanaonekere Ine ndakudziwitsani.”
10 Chantez au Seigneur un cantique nouveau, vous qui êtes son royaume; glorifiez son nom des extrémités de la terre, ô vous qui descendez sur la mer pour y naviguer; et vous, îles, et vous qui les habitez!
Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, mutamandeni inu okhala mʼdziko lonse lapansi, inu amene mumayenda pa nyanja, nyanja ikokome ndi zonse zili mʼmenemo. Inu okhala pa zilumba tamandani Yehova.
11 Désert, réjouis-toi; que tes bourgs se réjouissent et tes hameaux, et le peuple de Cédar; et ceux qui habitent parmi les rochers pousseront des cris de joie.
Chipululu ndi mizinda yake zikweze mawu awo; midzi ya Akedara ikondwere. Anthu a ku Sela ayimbe mwachimwemwe; afuwule kuchokera pamwamba pa mapiri.
12 Ils rendront gloire à Dieu; ils feront connaître aux îles ses vertus.
Atamande Yehova ndipo alalike matamando ake kwa anthu apazilumba zonse.
13 Le Seigneur Dieu des armées s'avancera; il brisera tout à la guerre; il excitera son zèle; il criera avec force contre ses ennemis.
Yehova adzapita ku nkhondo ngati munthu wamphamvu, adzawutsa ukali wake ngati munthu wankhondo; akukuwa ndiponso akufuwula mfuwu wankhondo ndipo adzagonjetsa adani ake.
14 J'ai gardé le silence; mais est-ce que je me tairai et me contiendrai toujours? J'ai souffert avec patience comme une femme qui enfante; je vais tout frapper de stupeur; je vais tout flétrir.
Yehova akuti, “Ndakhala ndili chete kwa nthawi yayitali, ndakhala ndili phee osachita kanthu. Koma tsopano, ngati mayi pa nthawi yochira, ndi kubuwula ndi kupuma modukizadukiza ndipo ndili wefuwefu.
15 Je rendrai désertes les montagnes et les collines; j'y sècherai l'herbe; je changerai les fleuves en îles; je mettrai à sec les étangs.
Ndidzawononga mapiri ndi zitunda ndipo ndidzawumitsa zomera zawo zonse; ndidzasandutsa mitsinje kukhala zilumba ndipo ndidzawumitsa maiwe.
16 Je conduirai les aveugles par une voie qu'ils ne connaissaient point; je leur ferai fouler des sentiers inconnus; je ferai que devant eux les ténèbres soient lumière et que les voies tortueuses deviennent droites. Voilà ce que j'accomplirai en leur faveur, et je ne les abandonnerai point.
Ndidzatsogolera anthu osaona mʼmisewu imene sanayidziwe, ndidzawatsogolera mʼnjira zimene sanayendepo; ndidzasandutsa mdima wa kutsogolo kwawo kuti ukhale kuwala ndipo ndidzasalaza malo osalala. Zimenezi ndizo ndidzachite; sindidzawataya.
17 Mais arrière ceux qui se sont détournés de moi! Soyez confondus, vous qui mettez votre confiance en des idoles d'argile et qui dites à des statues de fonte: Vous êtes nos dieux.
Koma onse amene amadalira mafano amene amanena kwa mafanowo kuti, ‘ndinu milungu yathu,’ ndidzawachititsa manyazi kotheratu.
18 Sourds, écoutez; aveugles, levez les yeux pour voir.
“Imvani, agonthi inu; yangʼanani osaona inu, kuti muone!
19 Et qui est aveugle, sinon mes serviteurs? Qui est sourd, sinon ceux qui les gouvernent? Oui, les serviteurs de Dieu sont devenus aveugles.
Ali wosaona ndani, si mtumiki wanga kodi? Ndipo ndani ali wosamva ngati mthenga amene ndamutuma? Kodi ndani ali wosaona ngati uja ndinachita naye pangano, kapena wosaona ndani ngati mtumiki wa Yehova?
20 Vous avez vu tant de fois, et vous n'y avez pas pris garde; vos oreilles étaient ouvertes, et vous n'avez pas entendu.
Iwe waona zinthu zambiri, koma sunazisamale; makutu ako ndi otsekuka koma sumva kanthu.”
21 Le Seigneur a pris conseil, afin qu'on reconnût sa justice et qu'on publiât sa louange.
Chinamukomera Yehova chifukwa cha chilungamo chake, kapena lamulo lake kukhala lalikulu ndi lopambana.
22 Et j'ai vu, et le peuple était pillé et dispersé. Le filet était tendu dans les retraites, dans les demeures, partout où ils se cachaient; et on les saisissait comme un butin, et nul n'était là pour arracher cette proie, nul n'était là pour dire: Rends-la-moi.
Koma awa ndi anthu amene afunkhidwa ndi kuwalanda zinthu zawo, onsewa anawakola mʼmaenje kapena akuwabisa mʼndende. Tsono asanduka chofunkha popanda wina wowapulumutsa kapena kunena kuti, “Abwezeni kwawo.”
23 Qui de vous recueillera ces choses en ses oreilles? écoutez l'avenir.
Kodi ndani wa inu amene adzamvetsera zimenezi kapena kutchera khutu ndi kumva za mʼtsogolomo?
24 Qui a livré comme une proie Jacob et Israël à ceux qui l'ont pris? n'est-ce point Dieu, contre qui ils ont péché, refusant de marcher dans sa voie et d'obéir à ses commandements?
Ndani anapereka Yakobo kwa ofunkha, ndi Israeli kwa anthu akuba? Kodi si Yehova, amene ife tamuchimwirayu? Pakuti sanathe kutsatira njira zake; ndipo sanamvere malangizo ake.
25 Et il a fait éclater contre eux les transports de sa fureur; et la guerre a prévalu sur eux; et ils ont entouré de flammes; et ils ne l'ont pas compris, et ils n'y ont pas arrêté leur âme.
Motero anawakwiyira kwambiri, nawavutitsa ndi nkhondo. Anayatsa moto ponseponse mowazungulira komabe iwo sanamvetse; motowo unawapsereza, koma iwo sanatengepo phunziro ayi.