< Isaïe 38 >

1 En ces jours-là, Ézéchias tomba malade d'une maladie mortelle, et le prophète Isaïe, fils d'Amos, l'alla trouver, et lui dit: Ainsi parle le Seigneur: Donne tes ordres concernant ta maison; car tu mourras, et tu n'as plus guère à vivre.
Nthawi imeneyo Mfumu Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anati “Yehova akuti: Konza bwino nyumba yako, pakuti ukufa; suchira.”
2 Et Ézéchias se retourna la face contre le mur, et il pria le Seigneur,
Hezekiya anatembenuka nayangʼana kukhoma, napemphera kwa Yehova kuti,
3 Disant: Seigneur, souvenez-vous que j'ai marché devant vous dans la vérité, avec un cœur sincère, et que j'ai fait ce qui était agréable à vos yeux. Et Ézéchias pleura des larmes abondantes.
“Inu Yehova, kumbukirani momwe ndayendera pamaso panu mokhulupirika ndi modzipereka ndipo ndakhala ndikuchita zabwino pamaso panu.” Ndipo Hezekiya analira mosweka mtima.
4 Et la parole du Seigneur vint à Isaïe, disant:
Ndipo Yehova analamula Yesaya kuti:
5 Va et dis à Ézéchias: Ainsi parle le Seigneur, Dieu de David, ton aïeul: J'ai entendu ta prière, et j'ai vu tes larmes, et voilà que j'ajoute quinze années à ta vie.
“Pita kwa Hezekiya ndipo ukamuwuze kuti, ‘Yehova, Mulungu wa kholo lake Davide akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona; ndidzakuwonjezera zaka 15 pa moyo wako.
6 Et je te sauverai, toi et cette ville, du roi des Assyriens, et j'étendrai mon bouclier sur cette ville.
Ndipo ndidzakupulumutsa, iwe pamodzi ndi mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya, Ine ndidzawuteteza mzindawu.
7 Tel est le signe du Seigneur qui te montrera que sa parole s'accomplira:
“‘Ichi ndi chizindikiro cha Yehova kwa iwe kutsimikiza kuti Yehova adzachita zimene walonjeza:
8 Voilà que je vais faire reculer l'ombre des marches où le soleil est descendu, de dix degrés sur la maison de ton père; je ferai reculer le soleil de ces dix degrés. Et le soleil remonta les dix marches que l'ombre avait descendues.
Chithunzithunzi chimene dzuwa likuchititsa pa makwerero a Ahazi ndidzachibweza mʼmbuyo makwerero khumi.’” Ndipo chithunzithunzi chinabwerera mʼmbuyo makwerero khumi.
9 Prière d'Ézéchias roi de Juda, quand il avait été malade, et qu'il se releva de sa maladie.
Ndakatulo ya Hezekiya mfumu ya ku Yuda imene analemba atadwala ndi kuchira:
10 J'ai dit: Dans la plénitude de mes jours, je descendrai aux portes de l'enfer, j'abandonnerai le reste de mes années. (Sheol h7585)
Ine ndinaganiza kuti ndidzapita ku dziko la akufa pamene moyo ukukoma. (Sheol h7585)
11 J'ai dit: Je ne verrai plus le salut de Dieu sur la terre des vivants; je ne verrai plus le salut d'Israël sur la terre; je ne verrai plus aucun homme.
Ndinaganiza kuti, “Sindidzaonanso Yehova, mʼdziko la anthu amoyo, sindidzaonanso mtundu wa anthu kapena kukhala pamodzi ndi amene amakhala pa dziko lapansi lino.
12 Le reste de ma vie a disparu, il a été retranché de ma race; il s'en est allé et il m'a quitté, comme le voyageur qui replie sa tente après l'avoir dressée; mon souffle est comme un fil de laine dont l'ouvrière s'approche pour le couper.
Nyumba yanga yasasuka ndipo yachotsedwa. Ngati tenti ya mʼbusa mwapindapinda moyo wanga, ngati munthu wowomba nsalu; kuyambira usana mpaka usiku mwakhala mukundisiya.
13 En ce jour, avant l'aurore, j'ai été livré comme à un lion; c'est ainsi qu'il a broyé tous mes os; car je lui ai été livré depuis le point du jour jusqu'à la nuit.
Ndinkalira kupempha chithandizo usiku wonse mpaka mmawa; koma Inu Yehova munaphwanya mafupa anga ngati mkango, ndipo mwakhala mukundisiya.
14 Je crierai comme l'hirondelle, je gémirai comme la colombe; car mes yeux se sont obscurcis à force de regarder au plus haut des cieux vers le Seigneur, qui enfin m'a relevé,
Ndinkalira ngati namzeze kapena chumba, ndinkabuwula ngati nkhunda yodandaula. Maso anga anatopa nʼkuyangʼana mlengalenga. Inu Ambuye, ine ndili mʼmavuto bwerani mudzandithandize!”
15 qui m'a ôté les douleurs de mon âme.
Koma ine ndinganene chiyani? Yehova wayankhula nane, ndipo Iye ndiye wachita zimenezi. Chifukwa cha kuwawa kwa mtima wanga, ine ndidzayenda modzichepetsa masiku amoyo wanga onse.
16 Seigneur, vous m'avez fait connaître votre volonté sur ma vie, et vous avez ranimé mon souffle; et consolé j'ai vécu.
Ambuye, masiku anga ali mʼmanja mwanu. Mzimu wanga upeza moyo mwa Inu. Munandichiritsa ndi kundikhalitsa ndi moyo.
17 Vous avez délivré mon âme pour m'empêcher de mourir; et vous avez rejeté derrière moi tous mes péchés.
Ndithudi, ine ndinamva zowawa zotere kuti ndikhale ndi moyo; Inu munandisunga kuti ndisapite ku dzenje la chiwonongeko chifukwa mwakhululukira machimo anga onse.
18 Car ceux qui sont en enfer ne vous loueront point, les morts ne vous béniront pas; en enfer on n'espère plus en votre miséricorde. (Sheol h7585)
Pakuti akumanda sangathe kukutamandani, akufa sangayimbe nyimbo yokutamandani. Iwo amene akutsikira ku dzenje sangakukhulupirireni. (Sheol h7585)
19 Les vivants vous béniront, comme je le fais moi-même; à partir de ce jour, j'enseignerai des enfants à publier votre justice.
Amoyo, amoyo okha ndiwo amakutamandani, monga mmene ndikuchitira ine lero lino; abambo amawuza ana awo za kukhulupirika kwanu.
20 Dieu de mon salut, je ne cesserai de vous bénir au son de la harpe, tous les jours de ma vie, devant le temple de Dieu.
Yehova watipulumutsa. Tiyeni tiyimbe ndi zoyimbira za zingwe masiku onse a moyo wathu mʼNyumba ya Yehova.
21 Et Isaïe dit à Ézéchias: Prends un panier de figues, écrase-les, et te les applique, et tu seras guéri.
Yesaya anati, “Anthu atenge mʼbulu wankhunyu ndipo apake pa chithupsacho ndipo Hezekiya adzachira.”
22 Et Ézéchias dit: Quel miracle qu'Ézéchias puisse monter encore au temple de Dieu!
Hezekiya nʼkuti atafunsa kuti, “Kodi chizindikiro chako nʼchiyani chotsimikiza kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova?”

< Isaïe 38 >