< Isaïe 33 >

1 Malheur à ceux qui vous affligent! Que nul ne vous rende misérables; que celui qui vous méprise cesse de vous mépriser. Ceux qui vous comptent pour rien seront pris à leur tour; ils seront subjugués, ils deviendront aussi faibles que le ver sur un manteau.
Tsoka kwa iwe, iwe wowonongawe, amene sunawonongedwepo! Tsoka kwa iwe, iwe mthirakuwiri, iwe amene sunanyengedwepo! Iwe ukadzaleka kuwononga, udzawonongedwa, ukadzasiya umʼthirakuwiri, adzakuwononga, ndipo ukadzaleka kuchita zachinyengo adzakunyenga.
2 Seigneur, faites-nous miséricorde; car nous avons eu confiance en vous; la race des incrédules est allée à sa perte; notre salut viendra au temps de la tribulation.
Inu Yehova, mutikomere mtima ife; tikulakalaka Inu. Tsiku ndi tsiku mutitchinjirize ndi mkono wanu, ndipo mutipulumutse pa nthawi ya masautso.
3 A votre voix redoutable, les peuples ont eu peur de vous, et ils ont été hors d'eux-mêmes, et les Gentils se sont dispersés.
Mukatulutsa liwu lanu longa bingu mitundu ya anthu imathawa; pamene Inu mwadzambatuka mitundu ya anthu imabalalika.
4 Maintenant on recueillera vos dépouilles, celles du petit comme celles du grand; tel un homme ramasse des sauterelles, ainsi on se jouera de vous.
Zofunkha za ku nkhondo za mitundu ina Aisraeli adzazisonkhanitsa ngati mmene limachitira dzombe. Iwo adzalumphira zofunkhazo monga mmene limachitira dzombe.
5 Le Saint, le Seigneur Dieu, qui réside au plus haut des cieux, a rempli Sion de justice et d'équité.
Yehova wakwezeka kwambiri pakuti amakhala pamwamba pa zonse adzadzaza Ziyoni ndi chilungamo ndi chipulumutso.
6 Ils se soumettront à la loi; notre salut est dans ses trésors; c'est là que la sagesse, la science et la piété sont auprès du Seigneur; ce sont là les trésors de la justice.
Iye adzakupatsani mtendere pa nthawi yanu, adzakupatsani chipulumutso chochuluka, nzeru zambiri ndi chidziwitso chochuluka; kuopa Yehova ngati madalitso.
7 Voilà qu'ils vont avoir peur de vous, ceux que vous craigniez; ils crieront à cause de vous; des messagers seront envoyés, pleurant amèrement et implorant la paix.
Taonani, anthu awo amphamvu akulira mofuwula mʼmisewu; akazembe okhazikitsa mtendere akulira kwambiri.
8 Car toutes leurs voies seront désertes; la crainte qu'inspiraient les Gentils est calmée: l'alliance avec eux est rompue; vous ne les compterez plus parmi les hommes.
Mʼmisewu yayikulu mulibe anthu, mʼmisewu mulibe anthu a paulendo. Mdaniyo ndi wosasunga pangano. Iye amanyoza mboni. Palibe kulemekezana.
9 La terre est en deuil; le Liban est confondu; Saron est devenu un marécage; la Galilée et le Carmel sont à découvert.
Dziko likulira ndipo likunka likutha. Nkhalango ya Lebanoni ikuchita manyazi, yafota. Chigwa cha chonde cha Saroni chasanduka chachidalala. Masamba a mitengo ya ku Basani ndi Karimeli akuyoyoka.
10 Alors je me lèverai, dit le Seigneur; alors je serai loué, je serai glorifié
Yehova akunena kuti, “Tsopano ndidzadzambatuka ndipo ndidzaonetsa mphamvu zanga, ndipo ndidzakwezedwa.
11 Vous verrez alors, et vous comprendrez; votre force d'esprit sera vaine, et le feu vous dévorera.
Zolingalira zanu nʼzachabechabe ngati udzu wamanyowa. Mpweya wamoto udzakupserezani.
12 Et les nations seront consumées, comme les ronces d'un champ qu'on arrache et qu'on brûle.
Anthu a mitundu ina adzatenthedwa ngati miyala ya njereza; ndi ngati minga yodulidwa.”
13 Ceux qui demeurent au loin apprendront ce que j'aurai fait; ceux qui sont près de moi connaîtront ma force.
Inu amene muli kutali, imvani zimene ndachita; inu amene muli pafupi, dziwani mphamvu zanga
14 Les pécheurs sont partis de Sion, un tremblement a saisi les impies. Qui vous annoncera que le feu est allumé? Qui vous fera connaître le séjour éternel?
Mu mzinda wa Ziyoni anthu ochimwa agwidwa ndi mantha; anthu osapembedza Mulungu akunjenjemera: Iwo akunena kuti, “Ndani wa ife angathe kukhala mʼmoto wonyeketsa? Ndani wa ife angathe kukhala moto wosatha?”
15 Celui qui marche dans la justice, qui parle avec droiture, qui hait les transgressions et l'iniquité, qui de ses mains repousse les présents, qui fait la sourde oreille quand on excuse l'effusion du sang, qui ferme les yeux pour ne pas voir le mal.
Angathe kuti ndi amene amachita zolungama ndi kuyankhula zoona, amene amakana phindu lolipeza monyenga ndipo salola manja ake kulandira ziphuphu, amene amatseka makutu ake kuti angamve mawu opangana kupha anzawo ndipo amatsinzina kuti angaone zoyipa.
16 Celui-là résidera dans un grotte élevée en une roche inexpugnable. Là on lui donnera des vivres et de l'eau toujours fidèle à couler.
Munthu wotere ndiye adzakhale pa nsanja, kothawira kwake kudzakhala mʼmalinga a mʼmapiri. Azidzalandira chakudya chake ndipo madzi sadzamusowa.
17 Vous verrez le roi dans sa gloire, vos yeux verront de loin la terre;
Nthawi imeneyo maso a ana adzaona mfumu ya maonekedwe wokongola ndi kuona dziko lotambasukira kutali.
18 Et votre âme s'occupera de l'objet de sa crainte. Où sont les scribes? Où sont les conseillers? Où est celui qui apprenait à compter les petits enfants?
Mu mtima mwanu muzidzalingalira zoopsa zinachitika kale zija: “Ali kuti mkulu wa Asilikali uja? Ali kuti wokhometsa misonkho uja? Ali kuti mkulu woyangʼanira nsanja?”
19 On ne verra plus un peuple, grands et petits, sans sagesse, parlant une langue inconnue, qu'un peuple ne pourrait ni ouïr ni comprendre.
Simudzawaonanso anthu odzikuza aja, anthu aja achiyankhulo chosadziwika, chachilendo ndi chosamveka.
20 Voici la ville de Sion, notre salut; tes yeux verront Jérusalem, riche cité; ses tabernacles ne chancelleront pas; les pieux de son tabernacle demeureront inébranlables dans les siècles des siècles, et ses cordages ne se rompront jamais;
Taonani Ziyoni, mzinda wa zikondwerero zachipembedzo chathu; maso anu adzaona Yerusalemu, mzinda wamtendere, tenti imene sidzachotsedwa, zikhomo zake sizidzazulidwa, kapena zingwe zake kuduka.
21 Parce que le nom du Seigneur est grand pour vous: pour vous il y aura une contrée, des fleuves et des canaux larges et spacieux. Mais toi, tu ne prendras pas cette voie; le navire que poussent tes rameurs ne la prendra point.
Kumeneko Yehova adzaonetsa ulemerero wake ndipo mzindawo udzakhala kasupe wa mitsinje yayikulu. Ngalawa za zopalasa sizidzapitamo, sitima zapamadzi zikuluzikulu sizidzayendamo.
22 Car mon Dieu est grand; le Seigneur mon juge ne me dédaignera pas; le Seigneur est notre roi, le Seigneur est notre prince: c'est le Seigneur qui nous sauvera.
Pakuti Yehova ndi woweruza wathu, Yehova ndiye wotilamulira, Yehova ndiye mfumu yathu; ndipo ndiye amene adzatipulumutse.
23 Tes cordages sont rompus, parce qu'ils n'avaient pas de force; ton mât penche, il ne fera pas descendre les voiles; il n'élèvera pas le signal, jusqu'à ce que le navire soit livré au pillage. Et beaucoup de boiteux même y feront du butin.
Zingwe za sitima zapamadzi za adani athu zamasuka, sizikutha kulimbitsa mlongoti wake, matanga ake sakutheka kutambasuka. Ngakhale tidzagawana zofunkha zochuluka kwambiri ndipo ngakhale olumala adzatenga zofunkhazo.
24 Et l'on ne dira pas parmi le peuple qui y demeure: Je suis trop las; car leur péché leur a été remis.
Palibe ndi mmodzi yemwe wokhala mʼZiyoni adzanene kuti, “Ndikudwala” ndipo anthu onse okhala mʼmenemo machimo awo adzakhululukidwa.

< Isaïe 33 >