< Isaïe 32 >

1 Voilà qu'un roi juste va régner, et que les princes gouverneront selon la justice.
Taonani, kudzakhala mfumu ina imene idzalamulira mwachilungamo, ndipo akalonga ake adzaweruza molungama.
2 Et ce sera un homme cachant ses discours, et il se cachera comme on se détourne d'une eau rapide; et il apparaîtra dans Sion comme un fleuve qui coule glorieux sur une terre altérée.
Munthu aliyense adzakhala ngati pothawirapo mphepo ndi malo obisalirapo namondwe, adzakhala ngati mitsinje ya mʼchipululu, ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu la mʼdziko lowuma.
3 Et le peuple ne mettra plus sa confiance en ces hommes; mais ils prêteront l'oreille pour écouter.
Ndipo maso a anthu openya sadzakhalanso otseka, ndipo makutu a anthu akumva adzamvetsetsa.
4 Et le cœur des faibles sera attentif à s'instruire; et les langues mêmes qui bégayent apprendront vite à prononcer des paroles de paix.
Anthu a mtima wopupuluma adzadziwa ndi kuchita zinthu mofatsa, ndipo anthu ovutika kuyankhula adzayankhula mosadodoma ndi momveka.
5 Et alors on ne dira plus à l'insensé: Règne, et tes serviteurs ne te diront plus: Tais-toi;
Chitsiru sichidzatchedwanso munthu waulemu wake ndipo munthu woyipa sadzalemekezedwa.
6 Car l'insensé parlera follement, et son cœur méditera des vanités; il ne pensera qu'à mal faire, à tromper le Tout-Puissant, à disperser les âmes affamées, à renvoyer vides les âmes altérées.
Pakuti munthu opusa amayankhula zauchitsiru, amaganiza kuchita zoyipa: Iye amachita zoyipira Mulungu, ndipo amafalitsa zolakwika zokhudza Yehova; anjala sawapatsa chakudya ndipo aludzu sawapatsa madzi.
7 Car le conseil des méchants projettera des choses iniques, pour détruire les petits avec des paroles injustes, et ruiner dans le jugement la cause des humbles.
Munthu woyipa njira zake ndi zoyipanso, iye kwake nʼkulingalira zinthu zoyipa. Amalingalira zakuti awononge anthu aumphawi ndi mabodza ake ngakhale kuti waumphawiyo akuyankhula zoona.
8 Cependant les hommes pieux ont délibéré des choses sensées, et tel leur conseil demeure.
Koma munthu wolemekezeka amalingaliranso kuchita zinthu zabwino, Iye amakhazikika pa zinthu zabwinozo.
9 Femmes riches, levez-vous et soyez attentives à ma voix; filles, écoutez mes paroles avec confiance.
Khalani maso, inu akazi amene mukungokhala wopanda kulingalira kuti kunja kulinji ndipo imvani mawu anga. Inu akazi odzitama, imvani zimene ndikunena!
10 Gardez-en la mémoire durant une année entière, dans une douleur mêlée d'espérance. La vendange est détruite, elle a cessé, elle ne reviendra plus.
Pakapita chaka ndi masiku pangʼono inu akazi amatama mudzanjenjemera; chifukwa mitengo ya mphesa idzakanika ndipo zipatso sizidzaoneka.
11 Soyez stupéfaites, soyez tristes, vous si confiantes; ôtez vos vêtements, dépouillez-vous, ceignez vos reins.
Nthunthumirani inu okhala mosatekesekanu; ndipo njenjemerani, inu akazi omadzikhulupirira nokhanu. Vulani zovala zanu, ndipo valani ziguduli mʼchiwuno mwanu.
12 Frappez vos poitrines, à cause des moissons regrettées de vos champs, et des fruits de vos vignes.
Dzigugudeni pachifuwa mwachisoni chifukwa minda yachonde, ndi mphesa yawonongeka.
13 La terre de mon peuple ne produira plus que des ronces et de mauvaises herbes; et de toute demeure la joie sera bannie. Cette ville opulente,
Mʼdziko la anthu anga mwamera minga ndi mkandankhuku. Zoona, mulilire nyumba zonse zachikondwerero ndi mzinda uno umene unali wachisangalalo.
14 Et ses maisons sont délaissées; ils abandonneront les richesses de la ville et leurs maisons si convoitées. Les bourgs seront à jamais des cavernes, délices des ânes sauvages, abri pour les pasteurs,
Nyumba yaufumu idzasiyidwa, mzinda waphokoso udzakhala wopanda anthu; malinga ndi nsanja zidzasanduka chipululu mpaka muyaya. Abulu adzasangalalamo ndipo ziweto zidzapezamo msipu.
15 Jusqu'à ce que sur vous vienne l'Esprit d'en haut. Et le Carmel devenu désert sera réputé une forêt.
Yehova adzatipatsa mzimu wake, ndipo dziko lachipululu lidzasanduka munda wachonde, ndipo munda wachonde udzakhala ngati nkhalango.
16 Et la justice habitera dans le désert, et l'équité résidera sur le Carmel.
Tsono mʼchipululu mudzakhala chiweruzo cholungama ndipo mʼminda yachonde mudzakhala chilungamo.
17 Et la paix sera l'œuvre de l'équité, et la justice vivra en repos, et le peuple aura confiance jusqu'à la fin des siècles.
Mtendere udzakhala chipatso chachilungamo; zotsatira za chilungamo zidzakhala bata ndi kudzidalira mpaka muyaya.
18 Et le peuple du Seigneur habitera en assurance la ville de la paix, et il s'y reposera au sein de la richesse.
Anthu anga adzakhala mʼmidzi yamtendere, mʼnyumba zodalirika, ndi malo osatekeseka a mpumulo.
19 Et si la grêle tombe, ce ne sera pas sur vous, et ceux qui habiteront la forêt seront en sûreté comme ceux de la plaine.
Ngakhale nkhalango idzawonongedwa ndi matalala ndipo mzinda udzagwetsedwa mpaka pansi,
20 Heureux ceux qui sèment des terres arrosées, que le bœuf et l'âne foulent aux pieds.
inutu mudzakhala odalitsika ndithu. Mudzadzala mbewu zanu mʼmbali mwa mtsinje uliwonse, ndipo ngʼombe zanu ndi abulu anu zidzadya paliponse.

< Isaïe 32 >