< Isaïe 21 >
1 Vision du désert. Comme une tempête venant de la terre passe de désert en désert, ainsi terrible
Uthenga wonena za chipululu cha mʼmbali mwa Nyanja. Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya adzabwera ngati kamvuluvulu amene akuwomba modutsa mʼmbali ya nyanja, kuchokera ku chipululu, dziko lochititsa mantha.
2 Et épouvantable une vision m'a été révélée: Le prévaricateur marche à ses prévarications, l'homme inique à ses iniquités. Sur moi viennent les Élamites, sur moi les anciens des Perses. Maintenant je gémirai et je me consolerai moi - même.
Ine ndaona zinthu zoopsa mʼmasomphenya: Wonyenga akunyenga, wofunkha akufunkha komanso owononga akuwononga. Elamu, yambani nkhondo! Mediya, zingani mzinda! Ine ndidzathetsa mavuto onse amene anayambitsa Ababuloni.
3 Voilà pourquoi mes reins ont défailli, et des douleurs comme celles de l'enfantement m'ont saisi. Ce que j'entends me fait mal, et je fais tout pour ne pas voir.
Chifukwa cha zimenezi thupi langa likunjenjemera ndi mantha, ndikumva ululu ngati wa mayi amene akubereka; ndikuvutika kwambiri ndi zimene ndikumva, ndathedwa nzeru ndi zimene ndikuziona.
4 Mon cœur s'égare, l'iniquité m'inonde, mon âme succombe dans la terreur.
Mtima wanga ukugunda, ndipo ndikunjenjemera ndi mantha; chisisira chimene ndakhala ndikuchifuna chasanduka chinthu choopsa kwa ine.
5 Dressez la table, mangez, buvez. Levez-vous, princes, préparez vos boucliers;
Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya akukonza matebulo, akuyala mphasa, akudya komanso kumwa! Mwadzidzidzi anamva mawu akuti, “Dzukani inu ankhondo, pakani mafuta zishango zanu!”
6 Car voici ce que m'a dit le Seigneur: Va, place-toi en sentinelle, et ce que tu verras, publie-le.
Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi; “Pita, kayike mlonda kuti azinena zimene akuziona.
7 Et je vis deux cavaliers: un cavalier monté sur un âne, un autre sur un chameau. Écoute avec une grande attention,
Taonani, anthu akubwera ali pa akavalo ndipo akuyenda awiriawiri, okwera pa bulu kapena okwera pa ngamira, mlondayo akhale tcheru kwambiri.”
8 Et appelle Urie au lieu d'observation. Ainsi dit le Seigneur. Et moi je me tins debout tout le jour, et je surveillai le camp toute la nuit.
Ndipo mlondayo anafuwula kuti, “Ambuye anga, tsiku ndi tsiku ndimakhala pa nsanja yolondera; Usiku uliwonse ndimakhala pa malo anga olondera.
9 Et voilà que vint à moi un homme sur un char à deux chevaux. Et, répondant à ma demande, il dit: Elle est tombée, elle est tombée, Babylone; et toutes ses statues et toutes les œuvres de ses mains sont brisées contre terre.
Taonani, uyo munthu akubwera atakwera pa galeta ali ndi gulu la akavalo. Mmodzi wa iwo akuti, ‘Babuloni wagwa, wagwa! Mafano onse a milungu yake agwa pansi ndipo aphwanyika!’”
10 Écoutez, ô vous qui êtes délaissés; et vous qui pleurez, écoutez ce que j'ai appris du Seigneur Dieu des armées, ce que m'a annoncé le Dieu d'Israël.
Inu anthu anga opunthidwa ndi kupetedwa ngati tirigu, ine ndikukuwuzani zimene ndamva ndikukuwuzani Uthenga wochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli.
11 On me crie de Séir: Gardez les créneaux!
Uthenga wonena za Duma: Munthu wina akundiyitana kuchokera ku Seiri kuti, “Iwe mlonda, usikuwu utha liti? Iwe mlonda, utha liti kodi usikuwu?”
12 Je les garde dès le matin et durant la nuit. Si tu cherches un secours, cherche-le bien, et demeure près de moi.
Mlonda akuyankha kuti, “Kukucha, koma kudanso. Ngati ukufuna kufunsa, funsa tsopano; ndipo ubwerenso udzafunse.”
13 Tu dormiras le soir dans la forêt sur le chemin de Daidan.
Uthenga wonena za Arabiya: Inu anthu amalonda a ku Dedani, amene usiku mumagona mʼzithukuluzi za ku Arabiya,
14 Portez de l'eau à la rencontre de l'homme qui a soif; et vous qui habitez la terre de Théman, portez des pains au-devant de ceux qui fuient;
perekani madzi kwa anthu aludzu. Inu anthu a ku Tema perekani chakudya kwa anthu othawa nkhondo.
15 Multitude d'hommes massacrés, multitude d'égarés, multitude de glaives et d'arcs tendus, multitude de guerriers tombés dans le combat.
Iwo akuthawa malupanga, lupanga losololedwa, akuthawa uta wokokakoka ndiponso nkhondo yoopsa.
16 Car voici ce que m'a dit le Seigneur: Encore une année, une année de mercenaire, et la gloire des fils de Cédar sera effacée,
Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi: “Chaka chimodzi chisanathe, potsata mmene amawerengera munthu waganyu, ulemerero wonse wa Kedara udzatheratu.
17 Et il ne restera qu'un petit nombre des vaillants archers de Cédar. Ainsi dit le Seigneur, Dieu d'Israël.
Mwa anthu okoka uta, ankhondo a ku Kedara opulumuka adzakhala owerengeka.” Wayankhula ndi Yehova Mulungu wa Israeli.