< Isaïe 18 >

1 Malheur à la terre fière de ses barques ailées, au delà des fleuves de l'Éthiopie!
Tsoka kwa anthu a ku Kusi. Kumeneko kumamveka mkokomo wa mapiko a dzombe.
2 A cette terre, qui envoie des otages par la mer et des lettres sur les eaux! Car des messagers rapides s'en iront vers une nation superbe, vers un peuple étranger et cruel. Qui habite au delà? Une nation désespérée et foulée aux pieds. Alors les fleuves de leur terre
Dziko limenelo limatumiza akazembe pa mtsinje wa Nailo, mʼmabwato amabango amene amayandama pa madzi, ndikunena kuti, “Pitani, inu amithenga aliwiro, kwa mtundu wa anthu ataliatali a khungu losalala, ndi woopedwa ndi anthu. Akazembe anatumidwa ku dziko la anthu amphamvu ndi logonjetsa anthu ena. Dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje.”
3 Seront tous habités comme une région habitée. Leur terre sera comme un signal élevé sur la montagne, comme le son d'une trompette qui se fait entendre.
Inu nonse anthu a pa dziko lonse, inu amene mumakhala pa dziko lapansi, pamene mbendera yakwezedwa pa mapiri yangʼanani, ndipo pamene lipenga lilira mumvere.
4 Car le Seigneur m'a ainsi parlé: Il y aura sécurité dans ma ville, comme la lumière à l'ardeur de midi, comme le nuage de rosée un jour de moisson,
Pakuti Yehova akunena kwa ine kuti, “Ndili chikhalire ku malo anga kuno, ndidzakhala chete, ndi kumangoyangʼana, monga momwe dzuwa limawalira nthawi yotentha, monganso momwe mame amagwera usiku pa nthawi yotentha yokolola.”
5 Avant la coupe des blés, quand la fleur est passée, que le raisin hors de fleur commence à mûrir, et que les fleurs sont devenues des grains. Alors le Seigneur ôtera les jeunes pousses avec la faux, et il arrachera les sarments et il les coupera.
Pakuti, anthu asanayambe kukolola, maluwa atayoyoka ndiponso mphesa zitayamba kupsa, Iye adzadula mphukira ndi mipeni yosadzira, ndipo adzadula ndi kuchotsa nthambi zotambalala.
6 Et il les abandonnera aux oiseaux du ciel et aux bêtes fauves de la terre. Et tous les oiseaux du ciel viendront s'y rassembler, et toutes les bêtes fauves de la terre accourront contre l'Éthiopien.
Mitembo ya anthu ankhondo adzasiyira mbalame zamʼmapiri zodya nyama ndiponso zirombo zakuthengo; mbalame zidzadya mitemboyo nthawi yonse ya chilimwe, ndipo zirombo zidzayidya pa nthawi yonse yachisanu.
7 En ce temps-là, des présents seront offerts au Seigneur, Dieu des armées, par un peuple contrit et opprimé, par un grand peuple, maintenant et par tous les siècles. Et c'est ce peuple qui espère aujourd'hui, que l'on foule aux pieds, qui habite la terre de ce côté du fleuve, dans le lieu où réside le nom du Seigneur, sur la montagne de Sion.
Pa nthawi imeneyo anthu adzabwera ndi mphatso kwa Yehova Wamphamvuzonse, zochokera kwa anthu ataliatali ndi osalala, kuchokera kwa mtundu wa anthu woopedwa ndi anthu apafupi ndi akutali omwe, mtundu wa anthu amphamvu ndi a chiyankhulo chachilendo, anthu amene dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje. Adzabwera nazo mphatso ku Phiri la Ziyoni, ku malo a Dzina la Yehova Wamphamvuzonse.

< Isaïe 18 >