< Isaïe 16 >

1 J'enverrai comme des reptiles sur la terre. La montagne de Sion, ma fille, n'est-elle pas une roche déserte?
Anthu a ku Mowabu atumiza mphatso za ana ankhosa onenepa, kuchokera ku Sela kudutsa chipululu mpaka kukafika ku phiri la Ziyoni.
2 Comme le petit oiseau enlevé à sa mère, ainsi tu seras, fille de Moab. A ton tour, Arnon,
Monga momwe mbalame zimawulukira uku ndi uku akazimwaza mʼchisa, momwemonso akazi a ku Mowabu akuyendayenda ku madooko a Arinoni.
3 Prends plus mûrement conseil, fais à Moab un abri pour y pleurer toujours; ils voudraient l'ombre pour fuir en plein midi, et ils sont dans la stupeur. Si tu veux échapper à la captivité,
Amowabu aja anawuza a ku Yuda kuti, “Tiwuzeni chochita, gamulani zoti tichite. Inu mutiteteze kwa adani anthu. Mukhale ngati mthunzi wathu dzuwa lili pa liwombo. Mutibise, musatipereke ife othawa nkhondo kwa adani athu.
4 O Moab, que mes fugitifs demeurent chez toi; et ils seront pour toi un refuge aux yeux de ton persécuteur; car ton auxiliaire t'est ravi; il a péri le prince qui foulait la terre.
Lolani kuti anthu othawa nkhondo a ku Mowabu azikhala pakati panu; mukhale populumukira pawo kwa wowonongayo.” Nthawi idzafika ndipo wozunzayo sadzakhalaponso, kuwononga kudzaleka; waukaliyo adzachoka mʼdzikomo.
5 Mais un trône sera érigé avec miséricorde, et un roi y siégera avec vérité dans le tabernacle de David, jugeant et cherchant la justice, et plein de zèle pour l'équité.
Mpando waufumu udzakhazikitsidwa mwachikondi; mmodzi mwa zidzukulu za Davide adzakhalapo mokhulupirika. Iyeyo poweruza adzatsata chilungamo ndipo adzalimbikitsa kuchita zachilungamo.
6 Nous avons appris l'insolence de Moab; son insolence était extrême, et je l'ai abattue; et ses divinations ne se sont point accomplies.
Tinamva kuti Mowabu anadzikuza kwambiri. Kunyada kwawo ndi kunyogodola kwawo ndi kudzitama kwawo, zonse ndi zopanda phindu.
7 Moab poussera des hurlements de douleur, tous les Moabites verseront des pleurs; médite sur les habitants de Seth, et tu ne seras point confondue.
Nʼchifukwa chake Amowabu akulira kwambiri; iwo akulirira dziko lawo. Akubuma momvetsa chisoni chifukwa cha makeke a mphesa a ku Kiri Hareseti.
8 Les champs d'Ésebon et la vigne de Sebama seront dans le deuil. O vous qui dévorez les nations, foulez aux pieds les vignes de Sebama jusqu'à Jaser; ne venez pas en foule, errez dans le désert; les rejetons qui avaient été plantés ont été délaissés, et ils ont passé du côté de la mer.
Minda ya ku Hesiboni yauma, minda ya mpesa ya ku Sibina yaguga. Atsogoleri a mitundu ina anapondaponda minda ya mpesa wabwino, imene nthambi zake zinakafika ku Yazeri, mpaka kutambalalira ku chipululu. Mizu yake inakafika mpaka ku tsidya la nyanja.
9 C'est pourquoi je pleurerai la vigne de Sebama, comme ceux de Jazer la pleurent. Ésebon et Éléalé ont jeté bas tes arbres, ô Moab; et moi, je foulerai tes blés au temps de la moisson, et tes ceps au temps de la vendange; et tout tombera.
Kotero Ine ndikulira, monga mmene akulirira anthu a ku Yazeri, chifukwa cha minda ya mpesa ya ku Sibima. Inu anthu a ku Hesiboni, inu anthu a ku Eleali, ndikukunyowetsani ndi misozi! Mwalephera kupeza zokolola, chifukwa cha nkhondo imene inawononga zokolola zonse.
10 Et la joie et les fêtes seront enlevées à tes vignes, et dans tes vignes il n'y aura plus de réjouissances; et on ne foulera plus le vin dans tes pressoirs, car il n'y aura plus de vendange.
Chimwemwe ndi chisangalalo zalekeka ku minda yanu ya zipatso; palibe amene akuyimba kapena kufuwula mʼminda ya mpesa; palibe amene akupsinya vinyo ku malo opsinyira mphesa, pakuti ndathetsa kufuwula.
11 C'est pourquoi mes entrailles pleureront sur Moab comme une cithare; Seigneur, vous avez tout renouvelé en moi, comme un mur en ruines.
Chifukwa chake moyo wanga ukulira ngati pangwe kulirira Mowabu, mtima wanga ukubuwula chifukwa cha Kiri Hareseti.
12 Et il arrivera pour sa confusion que Moab, lassé de ses autels, ira vers les idoles fabriquées de ses mains, et il les priera; mais elles ne pourront le sauver.
Ngakhale anthu a ku Mowabu apite ku malo awo achipembedzo koma amangodzitopetsa ndi kutaya nthawi chabe chifukwa sizidzatheka.
13 Telle est la prédiction que le Seigneur a prononcée sur Moab.
Awa ndi mawu amene Yehova wayankhula kale zokhudza Mowabu.
14 Et maintenant je dis: Dans trois ans, trois ans d'homme à gages, la gloire de Moab sera confondue avec toutes ses nombreuses richesses; et il n'échappera qu'un petit nombre de ses enfants, et ils seront sans honneur.
Koma tsopano Yehova akuti, “Zisanathe zaka zitatu, potsata mʼmene munthu waganyu amawerengera, ulemerero wa Mowabu udzakhala utatheratu ndipo anthu ake ambiri adzakhala atawonongeka, ndipo opulumuka ake adzakhala ochepa ndi ofowoka.”

< Isaïe 16 >