< Osée 1 >
1 Paroles du Seigneur qui vinrent à Osée, fils de Béeri, durant les jours d'Ozias, et de Joathan, et d'Achaz, et d'Ézéchias, rois de Juda, et durant les jours de Jéroboam, fils de Joas, roi d'Israël.
Awa ndi mawu amene Yehova anayankhula kwa Hoseya mwana wa Beeri pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda ndiponso pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Yowasi mfumu ya ku Israeli.
2 Commencement des paroles du Seigneur à Osée. Et le Seigneur dit à Osée: Va et prends pour toi une femme de prostitution; aie des enfants de la prostitution, parce que la terre se prostitue, et se prostituera en se retirant du Seigneur.
Yehova atayamba kuyankhula kudzera mwa Hoseya, Yehova anati kwa Hoseyayo, “Pita kakwatire mkazi wachiwerewere ndipo ubereke naye ana mʼchiwerewere chake pakuti anthu a mʼdziko muno achimwa pochita chigololo choyipitsitsa, posiya Yehova.”
3 Et il alla, et il prit Gomer, fille de Debélaïm, et elle conçut, et elle lui enfanta un fils.
Motero Hoseya anakwatira Gomeri mwana wamkazi wa Dibulaimu, ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna.
4 Et le Seigneur lui dit: Donne-lui le nom de Jezraël, parce que, encore un peu de temps, et Je vengerai le sang de Jezraël sur la maison de Juda, et Je ferai cesser la royauté de la maison d'Israël.
Tsono Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti Yezireeli, pakuti ndili pafupi kulanga banja la Yehu chifukwa cha anthu amene anawapha ku Yezireeli ndipo ndidzathetsa ufumu wa Israeli.
5 Et il arrivera, en ce jour-là, que Je briserai l'arc d'Israël dans la vallée de Jezraël.
Tsiku limenelo ndidzathyola uta wa Israeli mʼchigwa cha Yezireeli.”
6 Et elle conçut encore, et elle enfanté une fille. Et le Seigneur dit à Osée: Donne-lui le nom de Sans-Pitié, parce que Je ne continuerai plus d'avoir pitié de la maison d'Israël, mais Je lui résisterai et lui résisterai.
Gomeri anakhala woyembekezeranso ndipo anabereka mwana wamkazi. Ndipo Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti ‘Sakondedwa’ pakuti sindidzaonetsanso chikondi changa pa nyumba ya Israeli, kuti ndingawakhululukire konse.
7 Envers les fils de Juda Je serai miséricordieux, et Je les sauverai par le Seigneur leur Dieu; mais Je ne les sauverai pas par l'arc, ni par le glaive, ni par la guerre, ni par les chevaux, ni par les cavaliers.
Komatu ndidzaonetsa chikondi pa nyumba ya Yuda; ndipo ndidzawapulumutsa, osati ndi uta, lupanga kapena nkhondo, kapena akavalo ndi okwerapo ake, koma ine Yehova Mulungu wawo ndidzawapulumutsa.”
8 Et elle sevra cette fille Sans-Pitié; et elle conçut encore, et elle enfanta un fils.
Sakondedwa ataleka kuyamwa, Gomeri anabereka mwana wina wamwamuna.
9 Le Seigneur dit à Osée: Appelle-le Non-Mon-Peuple; parce que vous n'êtes plus Mon peuple, et Je ne suis plus votre Dieu.
Pamenepo Yehova anati, “Umutche dzina loti Sianthuanga,” pakuti inu si ndinu anthu anga ndipo Ine si ndine Mulungu wanu.
10 Et le nombre des fils d'Israël a été comme le sable de la mer, que l'on ne peut ni mesurer ni compter; et ceci arrivera dans le lieu même où il leur a été dit: Vous n'êtes plus Mon peuple; et ils seront appelés fils du Dieu vivant.
“Komabe Aisraeli adzachuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja umene sangathe kuwuyeza kapena kuwuwerenga. Pamalo omwe ananena kuti, ‘Sindinu anthu anga,’ pomweponso adzawatchula kuti ‘Ana a Mulungu wamoyo.’
11 Et les fils de Juda se réuniront, et en même temps ceux d'Israël, et ils institueront pour eux une seule principauté, et ils se répandront sur la terre, parce que le jour de Jezraël est grand.
Anthu a ku Yuda ndi anthu a ku Israeli adzasonkhananso pamodzi ndipo adzasankha mtsogoleri mmodzi ndi kutuluka mʼdzikomo, pakuti tsiku la Yezireeli lidzakhala lalikulu kwambiri.”