< Osée 4 >

1 Écoutez la parole du Seigneur, ô fils d'Israël; car le Seigneur va entrer en jugement avec les habitants de la terre, parce qu'il n'existe plus sur la terre ni vérité, ni miséricorde, ni connaissance de Dieu.
Inu Aisraeli, imvani mawu a Yehova, chifukwa Yehova ali ndi mlandu ndi inu amene mumakhala mʼdzikoli: “Mʼdziko mwanu mulibe kukhulupirika, mulibe chikondi mulibe kulabadira za Mulungu.
2 Les malédictions, le mensonge, le meurtre, le vol, l'adultère, sont répandus sur la terre, et le sang se mêle au sang.
Muli kutemberera kokha, kunama ndi kupha. Kuba ndi kuchita chigololo; machimo achita kunyanya ndipo akungokhalira kuphana.
3 C'est pourquoi la terre sera en deuil, et elle sera affaiblie avec tout ce qui l'habite, avec les bêtes des champs, les reptiles et les oiseaux du ciel; et même les poissons de la mer dépériront.
Chifukwa chake dziko likulira ndipo onse amene amakhalamo akuvutika; zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso nsomba zamʼnyanja zikufa.
4 Que nul n'ait de contestation, que nul ne reprenne autrui; Mon peuple est comme un peuple révolté contre ses prêtres.
“Koma wina asapeze mnzake chifukwa, wina aliyense asayimbe mlandu mnzake, pakuti anthu ako ali ngati anthu amene amayimba mlandu wansembe.
5 Et il perdra sa force de jour en jour, et, avec toi, le prophète aussi perdra sa force; J'ai comparé ta mère à la nuit.
Mumapunthwa usana ndi usiku ndipo aneneri amapunthwa nanu pamodzi. Choncho ndidzawononga amayi anu.
6 Mon peuple est comme s'il ne savait rien; car tu as repoussé la science, et Moi Je te repousserai à Mon tour, pour que tu n'aies plus Mon sacerdoce; tu as oublié la loi de Dieu, et Moi j'oublierai tes enfants.
Anthu anga akuwonongeka chifukwa chosadziwa. “Pakuti mwakana kudziwa, Inenso ndidzakukanani monga ansembe anga; chifukwa mwayiwala lamulo la Mulungu wanu, Inenso ndidzayiwala ana anu.
7 Plus ils se sont multipliés, plus ils ont péché contre Moi; Je changerai leur gloire en opprobre.
Ansembe ankati akachuluka iwo ankandichimwiranso kwambiri; iwo anasinthanitsa ulemerero wawo ndi chinthu china chonyansa.
8 Ils se nourriront des péchés de Mon peuple, et ils mettront leurs âmes en leurs iniquités.
Amalemererapo pa machimo a anthu anga ndipo amafunitsitsa kuti anthuwo azipitiriza kuchimwa.
9 Et tel sera le peuple, tel sera la prêtre; et sur eux Je tirerai vengeance de leurs voies, et Je les rétribuerai selon leurs conseils.
Ndipo zidzakhala motere: zochitikira anthu ena, zidzachitikiranso ansembe. Ndidzawalanga onsewo chifukwa cha njira zawo, ndidzawabwezera chifukwa cha machitidwe awo.
10 Ils mangeront, et ne seront pas rassasiés; ils se sont prostitués, et ne prospèrent point, parce qu'ils ont cessé de prendre garde au Seigneur.
“Iwo azidzadya koma sadzakhuta; azidzachita zachiwerewere koma sadzachulukana, chifukwa anasiya Yehova kuti adzipereke
11 Le cœur de Mon peuple s'est complu dans la prostitution, le vin et l'ivresse.
ku zachiwerewere, ku vinyo wakale ndi watsopano, zimene zimachotsa nzeru zomvetsa zinthu
12 Ils ont consulté des présages, et avec des baguettes on leur a fait des prédictions; ils ont été égarés en un esprit de débauche, et ils se sont prostitués en s'éloignant de leur Dieu.
za anthu anga. Anthu anga amapempha nzeru ku fano lamtengo ndipo ndodo yawo yamtengo imawayankha. Mzimu wachiwerewere umawasocheretsa; iwo sakukhulupirika kwa Mulungu wawo.
13 Ils ont sacrifié sur les hauts lieux; ils ont brûlé de l'encens sur des collines, sous un chêne ou sous un peuplier, ou sous tout arbre touffu, parce qu'ils se plaisent à l'ombre. À cause de cela, vos filles se prostitueront, et vos femmes seront adultères.
Amapereka nsembe pamwamba pa mapiri ndi kufukiza lubani pa zitunda, pa tsinde pa mtengo wa thundu, mnjale ndi mkundi, pamene pali mthunzi wabwino. Nʼchifukwa chake ana anu aakazi akuchita zachiwerewere ndipo akazi a ana anu akuchita zigololo.
14 Et Je ne visiterai plus vos filles quand elles se prostitueront, ni vos femmes quand elles seront adultères, parce que vous-mêmes vous vous êtes souillés avec des prostituées, et que vous avez sacrifié avec des initiés, et que le peuple (un peuple intelligent!) s'est laissé prendre aux filets d'une prostituée.
“Ine sindidzalanga ana anu aakazi pamene iwo adzachita zachiwerewere, kapena akazi a ana anu pamene adzachita zigololo. Paja inu nomwe amunanu mumayenda ndi akazi achiwerewere, ndipo mumapereka nsembe pamodzi ndi akazi achiwerewere a ku malo opembedzerako. Anthu amene alibe nzeru adzawonongeka ndithu!
15 Or sache-le bien, toi, Israël, et toi, Juda: n'allez point en Galgala, ne montez point à la maison de On, et ne jurez point par le Dieu vivant.
“Ngakhale umachita chigololo, iwe Israeli, Yuda asapezeke ndi mlandu wotere. “Usapite ku Giligala. Usapite ku Beti-Aveni. Ndipo usalumbire kuti, ‘Pali Yehova wamoyo!’
16 Car Israël, comme une génisse aiguillonnée par un taon, a eu des transports frénétiques, et maintenant le Seigneur le fera paître comme un agneau dans un lieu spacieux.
Aisraeli ndi nkhutukumve, ngosamva ngati ana angʼombe. Kodi Yehova angathe kuwaweta bwanji ngati ana ankhosa pa msipu wabwino?
17 Éphraïm, qui participe aux idoles, a mis devant lui des pierres d'achoppement.
Efereimu waphathana ndi mafano; mulekeni!
18 Il a provoqué les Chananéens; ils se sont prostitués et prostitués, et ils ont aimé l'ignominie et ses rugissements.
Ngakhale pamene zakumwa zawo zatha, amapitiriza kuchita zachiwerewere; atsogoleri awo amakonda kwambiri njira zawo zochititsa manyazi.
19 Seigneur, Tu es un tourbillon de vent emporté sur ses ailes; pour eux, ils seront confondus à cause de leurs autels.
Adzachotsedwa ndi kamvuluvulu ndipo adzachita manyazi chifukwa cha nsembe zawo.

< Osée 4 >