< Osée 11 >

1 Israël est un enfant, et Moi Je l'aimais, et J'ai rappelé ses fils de l'Égypte.
“Israeli ali mwana, ndinamukonda, ndipo ndinayitana mwana wanga kuti atuluke mu Igupto.
2 Autant Je les ai rappelés, autant ils sont éloignés de Moi; ils ont sacrifié à Baal, et ils ont encensé des idoles.
Koma ndimati ndikamapitiriza kuyitana iwo amandithawa kupita kutali. Ankapereka nsembe kwa Abaala ndipo ankafukiza lubani kwa mafano.
3 Et Moi J'ai bandé les pieds d'Éphraïm, et Je l'ai pris dans Mes bras, et ils n'ont point connu que Je les guérissais.
Ndi Ine amene ndinaphunzitsa Efereimu kuyenda, ndipo ndinawagwira pa mkono; koma iwo sanazindikire kuti ndine amene ndinawachiritsa.
4 Au milieu de la perdition des hommes, je les ai enveloppés dans les nuages de Mon amour, et maintenant Je serai pour eux comme un homme qui en frappe un autre à la joue, et Je Me retournerai sur Éphraïm, et Je prévaudrai contre lui.
Ndinawatsogolera ndi zingwe zachifundo cha anthu ndi zomangira za chikondi; ndinachotsa goli mʼkhosi mwawo ndipo ndinawerama nʼkuwadyetsa.
5 Éphraïm a demeuré en Égypte, et Assur lui-même a été son roi, parce qu'il n'a pas voulu se convertir.
“Sadzabwerera ku Igupto, koma Asiriya ndiye adzakhala mfumu yawo pakuti akana kutembenuka.
6 Et dans ses villes il a été vaincu par le glaive, et il a cessé de le tenir en ses mains; et ils se nourriront des fruits de leurs conseils.
Malupanga adzangʼanima mʼmizinda yawo, ndipo adzawononga mipiringidzo ya zipata zawo nadzathetseratu malingaliro awo.
7 Et le peuple de Dieu sera en suspens dans le lieu de son exil, et Dieu S'irritera des choses mêmes qu'ils estiment le plus, et Il ne l'exaltera point.
Anthu anga atsimikiza zondifulatira Ine. Ngakhale atayitana Wammwambamwamba, sizidzatheka kuti Iye awakwezenso.
8 Que ferai-Je avec toi, Éphraïm? Serai-Je ton protecteur? Ô Israël, que ferai-Je avec toi? Je te traiterai comme Adama et Seboïm. Mon cœur a changé pour toi, et tu as excité tous Mes regrets.
“Kodi ndingakusiye bwanji iwe Efereimu? Kodi ndingakupereke bwanji iwe Israeli? Kodi ndingakuchitire bwanji zimene ndinachitira Adima? Kodi ndingathe bwanji kukuchitira zimene ndinachitira Zeboimu? Mtima wanga wakana kutero; chifundo changa chonse chikusefukira.
9 Mais Je n'agirai point selon le courroux de Mon âme; Je n'abandonnerai point Éphraïm, pour qu'il soit effacé; car Je suis Dieu, et non un homme; un Saint est en toi, et Je n'entrerai pas dans ta ville.
Sindidzalola kuti ndikulange ndi mkwiyo wanga woopsa, kapena kutembenuka ndi kuwononga Efereimu. Pakuti Ine ndine Mulungu osati munthu, Woyerayo pakati panu. Sindidzabwera mwaukali.
10 Je marcherai après le Seigneur; Il rugira comme un lion; il rugira, et les enfants des eaux seront saisis de stupeur.
Iwo adzatsatira Yehova; Iye adzabangula ngati mkango. Akadzabangula, ana ake adzabwera akunjenjemera kuchokera kumadzulo.
11 Les enfants de Mon peuple aussi seront saisis de stupeur, et fuiront de l'Égypte comme un oiseau, et de la terre des Assyriens comme une colombe, et Je les ferai rentrer dans leurs demeures, dit le Seigneur.
Adzabwera akunjenjemera ngati mbalame kuchokera ku Igupto, ngati nkhunda kuchokera ku Asiriya. Ine ndidzawakhazikanso mʼnyumba zawo,” akutero Yehova.
12 Éphraïm M'a entouré de ses mensonges, Israël et Juda de leurs impiétés; maintenant Dieu les connaît, et le peuple saint s'appellera le peuple de Dieu.
Efereimu wandizungulira ndi mabodza, nyumba ya Israeli yandizungulira ndi chinyengo. Ndipo Yuda wawukira Mulungu, wawukira ngakhale Woyerayo amene ndi wokhulupirika.

< Osée 11 >