< Habacuc 3 >

1 Seigneur, j'ai entendu Ta voix, et j'ai eu crainte.
Pemphero la mneneri Habakuku potsata mayimbidwe a Sigionoti.
2 J'ai considéré Tes œuvres, et je me suis extasié. Entre deux animaux Tu Te manifestes; quand les années seront proches, on Te connaîtra; quand les temps seront venus, Tu apparaîtras; quand mon âme est troublée de Ta colère, souviens-Toi de Ta miséricorde.
Inu Yehova, ndamva za kutchuka kwanu; Inu Yehova, ntchito zanu zandiopsa. Muzichitenso masiku athu ano, masiku athu ano zidziwike; mu ukali wanu mukumbukire kuchita chifundo.
3 Dieu viendra de Théman, et le Saint de la montagne ténébreuse de Pharan. Sa vertu est le vêtement des cieux, et la terre est pleine de Sa louange.
Mulungu anabwera kuchokera ku Temani, Woyerayo kuchokera ku Phiri la Parani. (Sela) Ulemerero wake unaphimba mlengalenga ndipo dziko lapansi linadzaza ndi matamando ake.
4 Sa splendeur sera comme la lumière; Il a dans Sa main des cornes (de puissance), et de la force Il a fait un puissant amour.
Kuwala kwa ulemerero wake kunali ngati kutuluka kwa dzuwa; kunyezimira kunkatuluka mʼdzanja lake, mʼmene anabisamo mphamvu zake.
5 Devant Sa face ira une parole; elle cheminera dans les plaines; sur Ses pieds
Patsogolo pake pankagwa mliri; nthenda yoopsa inkagwa kumbuyo kwake.
6 Il S'est dressé, et la terre en a tremblé; Il a regardé, et les nations se sont évanouies. les montagnes ont été violemment agitées; les collines se sont fendues, sous les pas de Sa marche éternelle.
Iye anayimirira ndi kugwedeza dziko lapansi; anayangʼana ndipo mitundu ya anthu inanjenjemera. Mapiri okhazikika anagumuka ndipo zitunda zakalekale zinatitimira. Njira zake ndi zachikhalire.
7 À cause des troubles, j'ai vu les tentes des Éthiopiens renversées; les tentes de la terre de Madian seront aussi frappées d'épouvante.
Ndinaona matenti a ku Kusani ali pa mavuto, mokhala a ku Midiyani muli ululu waukulu.
8 Seigneur, est-ce contre les fleuves que Tu es irrité? Est-ce que Ta colère s'en prend aux fleuves? Attaques-Tu la mer? Car Tu es monté sur Ton char, et Tes chevaux amènent le salut.
Inu Yehova, kodi munakwiyira mitsinje? Kodi munakalipira timitsinje? Kodi munapsera mtima nyanja pamene munakwera pa akavalo anu ndiponso magaleta anu achipulumutso?
9 Tu as fortement tendu ton arc contre les sceptres, dit le Seigneur. le cours des fleuves sera déchiré.
Munasolola uta wanu mʼchimake, munayitanitsa mivi yambiri. (Sela) Munagawa dziko lapansi ndi mitsinje;
10 Les peuples Te verront, Seigneur, et ils auront des douleurs comme celles de l'enfantement. Quand Tu détruis la voie par une inondation, l'abîme a fait entendre sa voix, et il a élevé ses vagues contre Toi.
mapiri anakuonani ndipo anagwedezeka. Madzi amphamvu anasefukira; nyanja yozama inakokoma ndipo mafunde ake anakwera kwambiri.
11 Le soleil s'est levé; la lune s'est tenue au lieu qui lui est prescrit: Tes rayons s'avanceront dans la lumière, à la lueur des éclairs qui jaillissent de Tes armes.
Dzuwa ndi mwezi zinayima chilili mlengalenga, pa kungʼanima kwa mivi yanu yowulukayo, pa kunyezimira kwa mkondo wanu.
12 Par Tes menaces, Tu abaisses la terre, et dans Ton courroux Tu abats les nations.
Munayendayenda mʼdziko lapansi muli ndi ukali, ndipo munapondereza mitundu ya anthu muli ndi mkwiyo.
13 Tu es venu pour le salut de Ton peuple, pour sauver Ton Christ; Tu enverras la mort sur la tête des impies; Tu les as chargés de chaînes jusqu'au cou.
Munapita kukalanditsa anthu anu, kukapulumutsa wodzozedwa wanu. Munakantha mtsogoleri wa dziko la anthu oyipa, munawononga anthu ake onse. (Sela)
14 Tu as frappé de stupeur les bêtes des puissants; ils en trembleront; ils laisseront voir leur frein en ouvrant la bouche, comme un pauvre qui mange en se cachant.
Ndi mkondo wake womwe munalasa mtsogoleri wake pamene ankhondo ake anabwera mwamphamvu kudzatibalalitsa, ankasangalala ngati kuti akudzawononga osauka amene akubisala.
15 Et, monté sur Tes chevaux, Tu es entré dans la mer, et ils en ont troublé l'eau profonde.
Munapondaponda pa nyanja ndi akavalo anu, kuvundula madzi amphamvu.
16 J'ai veillé, et mes entrailles ont frémi au son de la prière de mes lèvres, et l'effroi est entré dans mes os, et tout mon être a été bouleversé. Je me reposerai au jour de l'affliction, et je monterai chez le peuple où je suis passager.
Ndinamva ndipo mtima wanga unagunda kwambiri, milomo yanga inanjenjemera pakumva phokosolo; mafupa anga anaguluka, ndipo mawondo anga anawombana. Komabe ndikuyembekezera mofatsa, tsiku la masautso limene lidzafike pa mtundu wa anthu umene ukutithira nkhondo.
17 Car alors le figuier ne portera pas de fruits; il n'y aura pas de raisin à la vigne; l'œuvre de l'olivier sera trompeuse, et les champs ne produiront pas de nourriture. Les brebis manqueront de fourrage, et il n'y aura pas de bœufs à la crèche.
Ngakhale mtengo wa mkuyu usachite maluwa, ndipo mipesa ikhale yopanda mphesa. Ngakhale mitengo ya olivi isabereke zipatso, ndipo mʼminda musatuluke kanthu. Ngakhale nkhosa ndi ngʼombe zithe mʼkhola,
18 Pour moi, je tressaillirai dans le Seigneur; je mettrai ma joie en Dieu, mon Sauveur.
komabe ine ndidzakondwera mwa Yehova, ndidzasangalala mwa Mulungu Mpulumutsi wanga.
19 Le Seigneur mon Dieu est ma force; Il placera mes pieds sur une base inébranlable; Il m'a fait monter sur les hautes cimes, pour chanter en Son honneur un chant de triomphe.
Ambuye Yehova ndiye mphamvu yanga; amalimbitsa miyendo yanga ngati ya mbawala yayikazi, amandithandiza kukafika pamwamba pa phiri. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za nsambo.

< Habacuc 3 >