< Habacuc 1 >

1 Vision d'Habacuc, le prophète.
Uthenga umene mneneri Habakuku analandira mʼmasomphenya.
2 Jusques à quand, Seigneur, crierai-je sans que Tu m'écoutes? Jusques à quand Te crierai-je que l'on me fait violence? N'en me sauveras-Tu pas?
Kodi inu Yehova, ndidzakhala ndikukupemphani thandizo kwa nthawi yayitali motani, koma wosayankha? Kapena kufuwulira kwa inu kuti, “Chiwawa kuno!” koma wosatipulumutsa?
3 Pourquoi m'as-Tu affligé et m'as-Tu donné la douleur de voir la misère et l'impiété? Je suis en procès, et le juge reçoit des présents.
Chifukwa chiyani mukundionetsa zinthu zoyipa? Chifukwa chiyani mukundionetsa mavutowa? Ndikuona chiwonongeko ndi chiwawa; pali ndewu ndi kukangana kwambiri.
4 À cause de cela, la loi a été déchirée, et le jugement n'arrivera pas à bonne fin, parce que l'impie opprime le juste, et la sentence sera torturée.
Kotero malamulo anu atha mphamvu, ndipo chilungamo sichikugwira ntchito. Anthu oyipa aposa olungama, kotero apotoza chilungamo.
5 Voyez, contempteurs de la loi, regardez et admirez ces merveilles, et soyez anéantis: car, de vos jours, Je vais faire une œuvre que vous ne croirez pas, quoiqu'on vous l'annonce.
“Yangʼanani pakati pa mitundu ya anthu, ndipo penyetsetsani, ndipo muthedwe nazo nzeru. Pakuti ndidzachitadi zinthu pa nthawi yanu zimene inu simudzazikhulupirira, ngakhale wina atakufotokozerani.
6 Voilà que Je vais susciter les Chaldéens, nation cruelle et rapide, qui marche sur les plaines de la terre, pour prendre possession de tentes qui ne sont point les siennes.
Pakuti taonani, Ine ndikuwutsa Ababuloni, anthu ankhanza ndiponso amphamvu, amene amapita pa dziko lonse lapansi kukalanda malo amene si awo.
7 Redoutable et fameuse, c'est d'elle que le jugement procédera; tout son butin proviendra d'elle-même.
Iwowa ndi anthu ochititsa mantha, ndipo ndi owopsa; amadzipangira okha malamulo ndi kudzipezera okha ulemu.
8 Et ses chevaux s'élanceront plus agiles que le léopard; ils courront plus rapides que les loups de l'Arabie. Et ses cavaliers sortiront à cheval, et ils prendront de loin leur élan, et ils se déploieront comme l'aigle ardent à dévorer sa proie.
Akavalo awo ndi aliwiro kwambiri kupambana akambuku ndi owopsa kupambana mimbulu yolusa nthawi ya madzulo. Okwerapo awo akuthamanga molunjika; a pa akavalo awo ndi ochokera kutali, akuwuluka ngati chiwombankhanga chofuna kugwira nyama;
9 La perdition tombera sur les impies qui leur feront face, et leur tiendront tête; et l'envahisseur emmènera des captifs aussi nombreux que les grains de sable.
onse akubwera atakonzekera zachiwawa. Gulu la ankhondo likubwera ngati mphepo ya mʼchipululu ndi kugwira akapolo ochuluka ngati mchenga.
10 Et il se raillera des rois, et les tyrans seront pour lui des jouets, et il rira de chaque forteresse, et il l'entourera de levées de terre, et il la prendra de force.
Akunyoza mafumu ndiponso kuchitira chipongwe olamulira. Akupeputsa mizinda yonse yotetezedwa; akumanga mitumbira ndi kulanda mizindayo.
11 Alors son esprit changera, et il se transformera, et il fera pitié; telle est la force de mon Dieu.
Kenaka amasesa mofulumira ngati mphepo nʼkumangopitirirabe, anthu ochimwa, amene mphamvu zawo ndiye mulungu wawo.”
12 Seigneur, mon Dieu et mon Saint, n'es-Tu pas dès le commencement? Est-ce que nous mourrons? Tu as établi ces choses pour le jugement, et Tu m'as formé, Seigneur, pour annoncer Ton châtiment.
Inu Yehova, kodi sindinu wachikhalire? Mulungu wanga, Woyera wanga, ife sitidzafa. Inu Yehova, munawasankha anthuwo kuti abweretse chiweruzo; Inu Thanthwe, munawayika iwowo kuti atilange.
13 L'œil du Seigneur est trop dur pour regarder le mal et s'arrêter sur les labeurs de l'affliction. Pourquoi, Seigneur, considères-Tu ceux qui Te méprisent? Pourquoi gardes-Tu le silence quand l'impie dévore le juste?
Maso anu ndi oyera kwambiri safuna kuona choyipa; Inu simulekerera cholakwa. Chifukwa chiyani nanga mukulekerera anthu ochita zachinyengowa? Chifukwa chiyani muli chete pamene anthu oyipa akuwononga anthu olungama kupambana iwowo?
14 Traites-Tu les hommes comme les poissons de la mer, ou comme les reptiles qui n'ont point de guide?
Mwasandutsa anthu kukhala ngati nsomba zamʼnyanja, ngati zolengedwa zamʼnyanja zimene zilibe wolamulira.
15 Il a pris toute l'espèce à l'hameçon; il en a tiré un avec le filet; il en a enfermé un autre dans sa nasse. À cause de cela, il sera plein d'allégresse, et se réjouira en son cœur.
Mdani wawo woyipa amakoka anthu onse ndi mbedza, amawakola mu ukonde wake, amawasonkhanitsa mu khoka lake; kotero iyeyo amakondwa ndi kusangalala.
16 À cause de cela, il sacrifiera à sa nasse, il encensera son filet, parce qu'avec leur aide il aura engraissé sa part, et recueilli des aliments de choix.
Choncho iye amaperekera nsembe ukonde wake ndiponso kufukizira lubani khoka lake, popeza ukonde wakewo ndiye umamubweretsera moyo wapamwamba ndipo amadya chakudya chabwino kwambiri.
17 Et, à cause de cela, il jettera encore son filet, et ne se fera jamais faute de tuer les nations.
Kodi iye azipitirabe kugwiritsa ntchito makoka akewo, kuwononga mitundu ya anthu mopanda chifundo?

< Habacuc 1 >