< Genèse 6 >

1 Il vécut dans le temps que les hommes commencèrent à être nombreux sur la terre, et que des filles leur étaient nées.
Anthu atayamba kuchuluka pa dziko lapansi ndi kubereka ana aakazi,
2 Or, les fils de Dieu, ayant vu que les filles des hommes étaient belles, prirent pour femmes, parmi toutes, celles dont ils firent choix.
ana aamuna a Mulungu anaona kuti ana aakazi a anthuwo anali okongola. Ndipo anakwatira aliyense amene anamusankha.
3 Et le Seigneur Dieu dit: Mon esprit ne restera pas toujours avec ces hommes, parce qu'ils ne sont que chair. Désormais leurs jours formeront cent vingt ans.
Tsono Yehova anati, “Sindilola kuti chipwirikiti chikuchitikachi chipitirire mpaka muyaya, pakuti iye ndi munthu; masiku a moyo wake adzakhala zaka 120.”
4 Or, il y avait des géants sur la terre, en ces jours-là; car depuis que les fils de Dieu s'étaient unis aux filles des hommes, elles leur avaient enfanté ces géants, ces hommes fameux.
Masiku amenewo komanso pambuyo pake, pa dziko lapansi panali Anefili, anthu amphamvu ndiponso otchuka. Anthuwa ndi amene ankabadwa ana a Mulungu aja atakwatira ana aakazi a anthu.
5 Or, le Seigneur Dieu ayant vu que les méchancetés des hommes étaient multipliées sur la terre, et que chacun en son cœur tous les jours s'appliquait à penser au mal,
Pamene Yehova anaona kuti kuyipa kwa munthu pa dziko lapansi kunali kwakukulu ndi kuti nthawi zonse amalingalira ndi kukhumbira kuchita zoyipa zokhazokha,
6 Il s'attrista en lui-même d'avoir créé l'homme sur la terre. Et il réfléchit.
Yehova anamva chisoni kuti analenga munthu ndi kumuyika pa dziko lapansi, ndipo anawawidwa mtima.
7 Et Dieu dit: J'effacerai de la face de la terre l'homme que j'ai créé; tout sera détruit depuis l'homme jusqu'aux bestiaux, depuis les reptiles jusqu'aux oiseaux du ciel, parce que j'ai regret de les avoir créés.
Choncho Yehova anati, “Ndidzafafaniza munthu, nyama, zonse zokwawa, ndi mbalame za mu mlengalenga pa dziko lapansi, pakuti ndikumva chisoni kuti ndinazilenga zimenezi.”
8 Noé cependant trouva grâce devant le Seigneur Dieu.
Koma Yehova anamukomera mtima Nowa.
9 Voici les générations de Noé. Noé, homme juste, irréprochable dans sa vie, Noé était agréable à Dieu.
Mbiri ya Nowa inali yotere: Nowa anali munthu wolungama ndi wopanda tchimo pakati pa anthu a mʼbado wake. Ndipo anayenda ndi Mulungu.
10 Et Noé engendra trois fils: Sém, Cham et Japhet.
Nowa anabereka ana aamuna atatu: Semu, Hamu ndi Yafeti.
11 Or, la terre était corrompue devant Dieu, et pleine d'iniquités.
Chiwawa chinadzaza pa dziko lapansi kotero kuti dziko linakhala lowonongeka pamaso pa Mulungu.
12 Et le Seigneur Dieu vit la terre toute corrompue, parce que toute chair sur la terre avait corrompu ses voies.
Mulungu atayangʼana, anaona kuti dziko layipadi chifukwa cha makhalidwe oyipa a anthu onse pa dziko lapansi.
13 Et le Seigneur Dieu dit à Noé: Le temps fatal de tous les hommes est arrivé devant moi, parce que la terre est pleine de leurs iniquités; voilà donc que je vais détruire eux et toute la terre.
Ndipo Mulungu anati kwa Nowa, “Ndatsimikiza mtima kuti ndiwononge anthu onse, pakuti dziko lapansi ladzaza ndi ntchito zawo zoyipa. Ndithudi ndiwawononga pamodzi ndi zonse za pa dziko.
14 Ainsi, fais-toi une arche d'arbres équarris; tu composeras l'arche de cellules, et tu l'enduiras de bitume, au dedans et en dehors.
Tsono udzipangire chombo cha matabwa a mtengo wanjale; mʼkati mwake upange zipinda ndipo upake phula mʼkati ndi kunja.
15 Voici comment tu feras l'arche: trois cents coudées de long, cinquante coudées de large, trente coudées de haut.
Uchipange motere: Chombo chikhale mamita 140 mulitali, mamita 23 mulifupi ndi mamita 13 mu msinkhu wake.
16 Tu construiras l'arche en rassemblant les bois les uns au-dessus des autres; tu donneras au faîte une coudée de plus d'élévation; tu feras la porte de l'arche sur les flancs; elle aura des chambres basses, un étage au- dessus, et un troisième étage.
Uchipangire denga ndi kuchimaliza ndi zenera la masentimita makumi asanu. Uyike khomo mʼmbali mwa chombocho ndi kupanga zipinda zosanjikana; chapansi, chapakati ndi chapamwamba.
17 Car voilà que je prépare un déluge; j'amènerai de l'eau sur la terre pour anéantir toute chair ayant souffle de vie sous le ciel, et tout ce qui est sur la terre périra.
Ndidzagwetsa mvula ya chigumula pa dziko lapansi kuti ndiwononge zamoyo zonse za pansi pa thambo ndipo chilichonse cha pa dziko lapansi chidzafa.
18 J'établirai mon alliance avec toi; puis tu entreras dans l'arche, et avec toi entreront tes fils, ta femme, et les femmes de tes fils.
Koma ndidzachita pangano langa ndi iwe. Iwe, ana ako aamuna, mkazi wako ndi akazi a ana ako nonse mudzalowa mʼchombocho.
19 Ensuite, de tous les bestiaux, de tous les reptiles, de toutes les bêtes fauves, et de toute chair, tu introduiras dans l'arche deux couples pris parmi tous, pour être nourris avec toi; il y aura mâle et femelle.
Iwe udzalowa mʼchombocho ndi zolengedwa zamoyo zonse ziwiriziwiri, chachimuna ndi chachikazi, kuti zisungike ndi moyo pamodzi ndi iwe.
20 De tous les oiseaux ailés, par espèces, et de tous les reptiles se traînant à terre, selon leurs espèces, deux couples, pris parmi tous, mâles et femelles, entreront près de toi, pour être nourris avec toi.
Udzatenga ziwiriziwiri za mitundu yonse ya mbalame, mitundu yonse ya nyama, ndi mitundu yonse ya zokwawa kuti zikhale ndi moyo.
21 En même temps tu prendras avec toi de tous les aliments que vous mangez, tu les transporteras près de toi, et ce sera pour votre nourriture et pour la leur.
Udzatengenso chakudya cha mtundu uliwonse ndi kuchisunga kuti inu ndi nyamazo muzidzadya.”
22 Et tout ce que lui ordonna le Seigneur Dieu, Noé l'accomplit exactement.
Nowa anachita zonse monga Mulungu anamulamulira.

< Genèse 6 >

The World is Destroyed by Water
The World is Destroyed by Water