< Genèse 4 >

1 Or, Adam connut Éve sa femme, qui, ayant conçu, enfanta Caïn; et elle dit: J'ai obtenu un homme grâce à Dieu.
Adamu anagona malo amodzi ndi Hava mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Kaini, ndipo anati, “Ndi thandizo la Yehova ndapeza mwana wamwamuna.”
2 Ensuite elle enfanta son frère Abel, qui fut pasteur des brebis; de son côté Caïn s'adonna au labourage de la terre.
Kenaka anabereka mʼbale wake Abele. Abele anali woweta nkhosa ndipo Kaini anali mlimi.
3 Après bien des jours, il arriva que Caïn apporta des fruits de la terre en offrande au Seigneur.
Patapita nthawi, Kaini anatenga zipatso za ku munda nakazipereka kwa Yehova monga nsembe.
4 Or, Abel apporta des premiers-nés de son troupeaux et de leur graisse. Et Dieu regarda Abel et ses présents.
Nayenso Abele anatenga ana ankhosa oyamba kubadwa pamodzi ndi mafuta ake nakazipereka ngati nsembe kwa Yehova. Yehova anakondwera ndi Abele ndi nsembe yake.
5 Mais il ne fit attention ni à Caïn, ni à son offrande; Caïn en fut très affligé, et eut le visage tout abattu.
Koma sanakondwere ndi Kaini ndi nsembe yake. Kotero Kaini anakwiya kwambiri ndipo nkhope yake inagwa.
6 Le Seigneur dit à Caïn: D'où vient que tu es si fort affligé et que ton visage est tout abattu?
Choncho Yehova anati kwa Kaini, “Chifukwa chiyani wakwiya ndipo bwanji nkhope yako yagwa?
7 Si tu as bien fait de m'apporter des offrandes, en les choisissant mal n'as-tu pas péché? Calme-toi, le péché est sous ta puissance, et c'est à toi de le dominer.
Ukanachita zabwino sindikanakulandira kodi? Koma tsopano wachita zoyipa ndipo tchimo likukudikira pa khomo pako, likufuna kukugwira; koma iwe uyenera kugonjetsa tchimolo.”
8 Et Caïn dit à Abel son frère: Allons aux champs. Et voilà que comme ils étaient aux champs, Caïn se leva contre son frère Abel et le tua.
Tsiku lina Kaini anati kwa mʼbale wake Abele, “Tiye tipite ku munda.” Ndipo ali ku mundako, Kaini anawukira mʼbale wake namupha.
9 Et le Seigneur dit à Caïn: Où est Abel ton frère? Il répondit: Je ne sais: suis-je le gardien de mon frère?
Ndipo Yehova anamufunsa Kaini kuti, “Ali kuti mʼbale wako Abele?” Iye anayankha kuti, “Sindikudziwa. Kodi ine ndine wosunga mʼbale wanga?”
10 Le Seigneur Dieu dit: Qu'as-tu fait? Le cri du sang de ton frère a retenti de la terre jusqu'à moi.
Yehova anati, “Kodi wachita chiyani? Tamvera! Magazi a mʼbale wako akulirira kwa Ine kuchokera mʼnthaka.
11 Maintenant donc, maudit sois-tu sur la terre qui a ouvert la bouche pour recueillir de ta main le sang de ton frère.
Ndipo tsopano ndiwe wotembereredwa ndipo wachotsedwa mʼdziko limene nthaka yake inatsekula pakamwa pake kulandira magazi a mʼbale wako amene unakhetsa.
12 Lorsque tu travailleras à la terre, elle n'emploiera pas sa force pour te faire ses dons; tu seras gémissant et tremblant sur la terre.
Udzalima munda koma nthakayo sidzakupatsanso zokolola zake. Udzakhala wosakhazikika; womangoyendayenda pa dziko lapansi.”
13 Caïn dit au Seigneur: Mon crime est trop grand pour m'être pardonné.
Kaini anati kwa Yehova, “Chilango changa ndi chachikulu kuposera mphamvu zanga.
14 Si vous me bannissez aujourd'hui de la face de cette terre, je serai caché loin de vos yeux; je serai gémissant et tremblant sur la terre, et le premier qui me rencontrera me tuera.
Lero mukundipirikitsa pa dziko ndi pamaso panu; ndidzakhala wosakhazikika, woyendayenda, ndipo aliyense amene adzandipeze adzandipha.”
15 Le Seigneur lui dit: Il n'en sera point ainsi; tout être qui tuerait Caïn encourrait sept châtiments. Et le Seigneur Dieu mit un signe à Caïn, pour que tout être qui le rencontrerait ne le tuât point.
Koma Yehova anamuwuza kuti, “Sizidzatero ayi; aliyense amene adzaphe Kaini adzalangidwa ndi kulipiritsidwa kasanu ndi kawiri.” Pamenepo Yehova anayika chizindikiro pa Kaini kuti aliyense womupeza asamuphe.
16 Or, Caïn s'éloigna de la face de Dieu, et il habita la terre de Nod vis-à- vis Éden.
Ndipo Kaini anachoka pamaso pa Yehova nakakhala ku dziko la Nodi, kummawa kwa Edeni.
17 Après cela Caïn connut sa femme, qui, ayant conçu, enfanta Enoch; ensuite Caïn bâtit une ville, et du nom de son fils, il la nomma Enoch.
Kaini anagona malo amodzi ndi mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Enoki. Kaini nthawi imeneyo nʼkuti akumanga mzinda ndipo anawutcha dzina la mwana wake Enoki.
18 Or, d'Enoch fut engendré Gaïdad, Gaïdad engendra Malalehël, Malalehël engendra Mathusala, et Mathusala engendra Lamech.
Enoki anabereka Iradi; Iradi anabereka Mehuyaeli, ndipo Mehuyaeli anabereka Metusela, ndipo Metusela anabereka Lameki.
19 Et Lamech épousa deux femmes: la première nommée Ada, la seconde nommée Sella.
Lameki anakwatira akazi awiri, wina dzina lake linali Ada ndi winayo dzina lake linali Zila.
20 Ada enfanta Jabel; celui-ci fut le père de ceux qui demeurèrent sous des tentes, des nourrisseurs de bestiaux.
Ada anabereka Yabala; iyeyu anali kholo la onse okhala mʼmatenti ndi oweta ziweto.
21 Et son frère eut le nom Jubal; celui-ci inventa le psaltérion et la cithare.
Dzina la mʼbale wake linali Yubala; iyeyu anali kholo la onse oyimba zeze ndi chitoliro.
22 Or Sella de son côté enfanta Thobel ou Tubalcaïn, et il fut ouvrier au marteau, forgeron du fer et de l'airain. La sœur de Tubalcaïn fut Noéma.
Zila nayenso anali ndi mwana wamwamuna, dzina lake Tubala-Kaini. Iyeyu anali kholo la amisiri onse osula zida za mkuwa ndi chitsulo. Mlongo wake wa Tubala-Kaini anali Naama.
23 Or, Lamech dit à ses femmes Ada et Sella: Écoutez ma voix, femmes de Lamech, faites attention à mes paroles: J'ai tué un homme pour mon malheur, un jeune homme pour ma meurtrissure.
Lameki anawuza akazi akewo kuti, “Ada ndi Zila, ndimvereni; inu akazi anga imvani mawu anga. Ine ndinapha munthu chifukwa anandipweteka. Ndinapha mnyamatayo chifukwa anandimenya.
24 On eût vengé sept fois le meurtre de Caïn; celui de Lamech le serait septante fois sept.
Ngati wopha Kaini amulipsira kasanu nʼkawiri, ndiye kuti wopha ine Lameki adzamulipsira kokwanira 77.”
25 Or, Adam connut Éve sa femme, et, ayant conçu, elle enfanta un fils à qui elle donna le nom de Seth (substitué). Car, dit-elle, Dieu a fait sortir de moi un autre rejeton, en place d'Abel que Caïn a tué.
Adamu anagonanso malo amodzi ndi mkazi wake, ndipo anabereka mwana wamwamuna namutcha Seti, kutanthauza kuti, “Mulungu wandipatsa mwana wina mʼmalo mwa Abele, popeza Kaini anamupha.”
26 Et à Seth naquit un fils, auquel il donna le nom d'Enos; celui-ci, plein de confiance, invoqua le nom du Seigneur Dieu.
Seti naye anali ndi mwana wa mwamuna, ndipo anamutcha Enosi. Pa nthawi imeneyi anthu anayamba kupemphera mʼdzina la Yehova.

< Genèse 4 >