< Genèse 39 >

1 Cependant, Joseph fut conduit en Égypte, et Putiphar, eunuque du Pharaon, Égyptien, chef des cuisines, l'acheta des Ismaélites qui l'avaient amené.
Tsopano Yosefe anatengedwa kupita ku Igupto. Potifara Mwigupto amene anali mmodzi wa akuluakulu a Farao ndiponso mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa Farao, anagula Yosefe kwa Aismaeli amene anapita naye kumeneko.
2 Or, le Seigneur était avec Joseph; c'était un homme à qui tout réussissait, et il demeura dans la maison auprès de son maître égyptien.
Koma Yehova anali ndi Yosefe ndipo zake zonse zimayenda bwino. Iye ankakhala mʼnyumba ya mbuye wake wa ku Igupto.
3 Son maître savait que le Seigneur était avec lui, et que, quoi qu'il entreprît, le Seigneur mettrait en ses mains le succès.
Mbuye wake anaona kuti Yehova anali naye Yosefe ndi kuti pa chilichonse chimene anachita Yehova ankaonetsetsa kuti achite bwino.
4 Joseph trouva donc grâce devant son maître, et il lui était agréable, et son maître l'établit chef de sa maison. Il lui confia tout ce qui lui appartenait, et il n'en disposa plus que par les mains de Joseph.
Potifara anakondwera ndi Yosefe chifukwa cha matumikiridwe ake. Choncho anamusandutsa woyangʼanira nyumba yake ndi zonse za mʼnyumba yake.
5 Or, lorsqu'il l'eut établi chef de sa maison, et lui eut confié tout ce qui lui appartenait, le Seigneur bénit la maison de l'Égyptien à cause de Joseph, et la bénédiction du Seigneur fut sur tout ce qu'il possédait, en sa maison et à ses champs.
Kuchokera pa nthawi imene anamuyika kukhala woyangʼanira wa nyumbayo ndi zonse za mʼnyumbamo, Yehova anadalitsa nyumba ya Mwiguptoyo chifukwa cha Yosefe. Madalitso a Yehova anali pa chilichonse chimene Potifara anali nacho, za mʼnyumba komanso za ku munda.
6 Il confia donc à Joseph et remit en ses mains tout ce qui lui appartenait, et il ne sut rien par lui-même, hormis le pain qu'il mangeait. Joseph était beau de visage, et plein de grâce.
Choncho anasiyira mʼmanja mwa Yosefe chilichonse chomwe anali nacho, kotero kuti samadandaula ndi chilichonse kupatula chakudya chimene ankadya. Tsopano Yosefe anali wa thupi labwino ndi wokongola.
7 Or, après tout cela il arriva que la femme de Putiphar jeta les yeux sur Joseph, et lui dit: Dors avec moi.
Patapita kanthawi, mkazi wa mbuye wake anayamba kusirira Yosefe nati, “Bwanji ugone nane!”
8 Mais lui ne voulut point, et il dit à la femme de son maître: Mon seigneur ne connaît rien dans sa maison, à cause de sa confiance en moi; il a remis en mes mains tout ce qu'il possède.
Koma iye anakana namuwuza kuti, “Inu mukuona kuti mbuye wanga sadandaula ndi kena kalikonse mʼnyumba muno, ndipo chawo chilichonse anachiyika mʼmanja mwanga.
9 Rien dans cette maison n'est au-dessus de mon pouvoir: il ne s'est rien réservé hormis toi, parce que tu es sa femme; comment donc ferai-je cette méchante action, et me rendrai-je à ce point coupable devant Dieu?
Motero kuti palibe wina wamkulu kuposa ine mʼnyumba muno. Ndipo palibe chilichonse chimene mbuye wanga sanachipereke kwa ine kupatula inuyo, chifukwa ndinu mkazi wake. Tsono ndingachite bwanji choyipa choterechi ndi kuchimwira Mulungu?”
10 Et quand tous les jours elle parlait à Joseph, il refusait toujours de dormir avec elle, et de s'unir à elle.
Ndipo ngakhale kuti iye anayankhula mawu omwewa ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefe sanalole kugona naye ngakhale kukhala naye pafupi.
11 Or, un jour il advint que Joseph entra dans la maison au sujet de ses travaux, et nul de ceux de la maison ne se trouvait à l'intérieur.
Tsiku lina Yosefe analowa mʼnyumbamo kukagwira ntchito zake, ndipo munalibe wina aliyense wantchito mʼnyumbamo.
12 Et elle le tira par son manteau, disant: Dors avec moi; mais lui, laissant le manteau dans ses mains, il s'échappa, et sortit.
Mkazi uja anamugwira mkanjo Yosefe nati, “Tiye ugone nane!” Koma Yosefe anasiya mkanjo wake mʼmanja mwa mkaziyo nathawira kunja kwa nyumba.
13 Lorsqu'elle vit qu'il lui avait laissé son manteau dans les mains, qu'il s'était échappé, et était sorti,
Pamene mkazi uja anaona kuti Yosefe wamusiyira mkanjo wake mʼmanja mwake nathawira kunja kwa nyumba,
14 Elle appela tous ceux de sa maison, et dit: Voyez, Putiphar nous a amené un serviteur hébreu pour nous outrager; il est entré ici disant: Dors avec moi, et j'ai jeté de grands cris.
iye anayitana antchito ake a mʼnyumba nati, “Taonani mwamuna wanga anabwera ndi Mhebri uyu mʼnyumba muno kuti adzagone nane. Iyeyu analowa ku chipinda kwanga kuti adzagone nane ndipo ine ndinakuwa kwambiri.
15 Mais lorsqu'il a entendu que j'élevais la voix et que je criais, il a laissé chez moi son manteau, s'est échappé, et est sorti.
Atandimva ndikukuwa, anandisiyira mkanjo wakewu nʼkuthawira kunja.”
16 Elle retint donc le manteau près d'elle jusqu'à ce que le maître revînt en sa maison.
Tsono mkazi wa Potifara uja anasunga mkanjowo mpaka mbuye wake wa Yosefe atabwera ku nyumba.
17 Elle lui fit le même récit, disant: Il est venu près de moi ce serviteur hébreu que tu as introduit chez nous, pour m'outrager, et il m'a dit: Je dormirai avec toi;
Tsono anamuwuza nkhaniyi nati: “Wantchito Wachihebri amene munatibweretsera uja anabwera kuti adzagone nane.
18 Et lorsqu'il a entendu que j'élevais la voix et que je criais, il a laissé chez moi son manteau, s'est échappé, et est sorti.
Koma pamene ndinakuwa, iye anandisiyira mkanjo wake nathawira kunja.”
19 À peine le maître eut-il entendu les paroles de sa femme, lui affirmant que son serviteur l'avait ainsi traitée, qu'il fut transporté de colère.
Mbuye wake wa Yosefe atamva nkhani imene mkazi wake anamuwuza kuti, “Ndi zimene anandichitira wantchito wanu,” anapsa mtima kwambiri.
20 Il prit Joseph et il le jeta en prison, au même lieu où étaient renfermés les prisonniers du roi.
Tsono iye anatenga Yosefe namuyika mʼndende mmene ankasungiramo amʼndende a mfumu. Ndipo Yosefe anakhala mʼndendemo
21 Et le Seigneur était avec Joseph; il répandit sur lui sa miséricorde, il lui fit trouver grâce devant le gardien des prisonniers.
koma Yehova anali naye, ndipo anamuonetsa kukoma mtima kwake, kotero kuti woyangʼanira ndende anakondwera ndi Yosefe.
22 Le geôlier en chef confia même à Joseph la prison avec tous ceux qu'on y avait amenés; et tout ce qui se faisait là, c'était par Joseph.
Choncho woyangʼanira ndende uja anamuyika Yosefe kukhala woyangʼanira onse amene anayikidwa mʼndende. Ndiponso anamupatsa udindo woyangʼanira zonse zochitika mʼndendemo.
23 Le gardien en chef de la prison ne voyait plus rien par lui-même; car tout était entre les mains de Joseph, parce que le Seigneur était avec lui, et que dans tout ce qu'il entreprenait le Seigneur mettait le succès en ses mains.
Woyangʼanira ndende uja sankayangʼaniranso china chilichonse chimene chinali mu ulamuliro wa Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi Yosefe. Ndipo Yehova anaonetsetsa kuti chilichonse chimene Yosefe ankachita chimuyendere bwino.

< Genèse 39 >