< Esdras 1 >

1 La première année de la domination de Cyrus, roi des Perses, la parole du Seigneur qu'avait proférée la bouche de Jérémie le prophète, devait s'accomplir; le Seigneur excita l'esprit de Cyrus, roi des Perses, et il envoya en tout son royaume une proclamation par écrit, disant:
Mʼchaka choyamba cha ufumu wa Koresi mfumu ya Perisiya, pofuna kukwaniritsa zimene anayankhula kudzera mwa Yeremiya, Yehova anayika maganizo mu mtima mwa Koresi mfumu ya Perisiya kuti alengeze mʼdziko lake lonse ndi mawu apakamwa ngakhalenso ochita kulemba.
2 Voici ce qu'a dit Cyrus, roi des Perses: Le Seigneur Dieu du ciel m'a donné tous les royaumes de la terre, et lui-même a jeté les yeux sur moi pour que je lui bâtisse un temple à Jérusalem en Judée.
Iye anati, “Koresi mfumu ya Perisiya ikunena kuti, “‘Yehova, Mulungu wakumwamba wandipatsa maufumu onse a dziko lapansi, ndipo wandipatsa udindo woti ndimumangire Nyumba ku Yerusalemu mʼdziko la Yuda.
3 Qui donc, parmi vous tous, est de son peuple? Son Dieu sera avec lui, et il partira pour Jérusalem en Judée; qu'il y bâtisse le temple du Dieu d'Israël; le seul Dieu est celui qui réside à Jérusalem.
Aliyense wa inu amene ali wa Yehova, Mulungu wakeyo akhale naye. Tsono aliyense wa inu apite ku Yerusalemu, mʼdziko la Yuda kuti akamange Nyumba ya Yehova, Mulungu wa Israeli. Iyeyu ndi Mulungu amene ali mu Yerusalemu.
4 Tous ceux de ce peuple qui vivent encore, en quelque lieu qu'ils habitent, les hommes de ce lieu les aideront de dons en argent, en or, en meubles, ou en bestiaux, outre ce qu'ils offriront volontairement pour le temple de Dieu à Jérusalem.
Ndipo kumalo kulikonse kumene otsalawo akukhala, athandizidwe ndi eni dzikolo powapatsa siliva, golide, katundu ndi ziweto ndi zopereka za ufulu zoti akapereke ku Nyumba ya Yehova imene ili ku Yerusalemu.’”
5 Alors, se levèrent les chefs de famille de Juda et de Benjamin, et les prêtres et les lévites, tous ceux que l'Esprit de Dieu excita à partir et à relever le temple du Seigneur à Jérusalem.
Choncho atsogoleri a mabanja afuko la Yuda ndi la Benjamini komanso ansembe ndi Alevi, aliyense amene Mulungu anawutsa mtima wake, anayamba kukonzeka kupita kukamanga Nyumba ya Yehova imene ili ku Yerusalemu.
6 Et tous ceux qui les entouraient leur fortifièrent les mains avec des vases d'argent, de l'or, des meubles, des bestiaux et des présents, outre les dons volontaires pour le temple.
Onse oyandikana nawo anawathandiza powapatsa ziwiya za siliva ndi zagolide, kuphatikizaponso katundu ndi ziweto, ndiponso mphatso zamtengo wapatali, kuwonjezera pa zopereka zaufulu zija.
7 Et le roi Cyrus offrit les vases du temple du Seigneur que Nabuchodonosor avait enlevés de Jérusalem, et qu'il avait dédiés au temple de son Dieu.
Nayenso mfumu Koresi anatulutsa ziwiya za mʼNyumba ya Yehova zimene Nebukadinezara anazitenga kuzichotsa ku Yerusalemu ndi kuziyika mʼnyumba ya milungu yake.
8 Cyrus, roi des Perses, les donna par la main de Mithradate le trésorier, et celui-ci les compta avec Sasabasar, chef de Juda.
Koresi, mfumu ya ku Perisiya inatulutsa ziwiyazi ndi kuzipereka kwa Miteridati, msungichuma amene anaziwerenga pamaso pa Sesibazara nduna yayikulu ya dziko la Yuda.
9 En voici le nombre: trente coupes d'or, mille d'argent, vingt-neuf de divers genres, trente coupes d'or,
Chiwerengerochi chinali motere: Mabeseni agolide 30 mabeseni asiliva 1,000 a zopereka 29
10 Quatre cent dix doubles coupes d'argent, et mille autres vases.
timiphika tagolide 230 timiphika tasiliva 410 ziwiya zina 1,000.
11 Il y avait en tout cinq mille quatre cents vases d'or et d'argent qui furent emportés par Sasabasar, du lieu d'exil de Babylone, à Jérusalem.
Ziwiya zonse zagolide ndi siliva pamodzi zinalipo 5,400. Zonsezi ndi zimene Sezi-Bazara anabwera nazo pamene otengedwa ukapolo aja ankabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku Babuloni.

< Esdras 1 >