< Esdras 5 >

1 Or, Aggée le prophète, et Zacharie, fils d'Addo, firent, devant les Juifs qui se trouvaient en Juda et à Jérusalem, au nom du Dieu d'Israël, une prophétie qui les concernait.
Nthawi imeneyo aneneri Hagai ndi Zekariya, mwana wa Ido, ankayankhula kwa Ayuda okhala mʼdziko la Yuda ndi mu Yerusalemu mʼdzina la Mulungu wa Israeli, amene anali nawo.
2 Alors, Zorobabel, fils de Salathiel, et Josué, fils de Josedec, se mirent en avant, et ils commencèrent à bâtir le temple de Dieu à Jérusalem, et les prophètes de Dieu étaient avec eux, leur prêtant secours.
Pambuyo pake Zerubabeli mwana wa Sealatieli ndi Yesuwa mwana wa Yozadaki ananyamuka nakayambanso kumanga Nyumba ya Mulungu mu Yerusalemu. Ndipo aneneri a Mulungu anali nawo pamodzi, kuwathandiza.
3 En ce temps-là, Thanthanaï, gouverneur de ce côté de l'Euphrate, et Satharbuzanaï, et les autres serviteurs du roi, vinrent à eux, et leur dirent: Qui a fait en votre faveur un édit pour que vous bâtissiez ce temple et que vous fassiez ces apprêts?
Pa nthawi imeneyo Tatenai, bwanamkubwa wa chigawo cha patsidya pa Yufurate pamodzi ndi Setari-Bozenai ndi anzawo anapita kwa iwo ndi kukawafunsa kuti, “Anakulolani ndani kuti mumangenso Nyumba imeneyi ndi kutsiriza khoma lake?”
4 Et ils ajoutèrent: Quels sont les noms des hommes qui bâtissent cette ville?
Anawafunsanso kuti, “Kodi anthu amene akumanga nyumbayi mayina awo ndani?”
5 Mais les yeux de Dieu étaient ouverts sur la captivité de Juda, et ces hommes ne suspendirent pas les travaux jusqu'à ce qu'un édit fût fait par Darius. Et alors, à ce sujet, le collecteur des impôts envoya
Koma Mulungu wawo amayangʼanira atsogoleri Ayuda, motero kuti anthu aja anaganiza kuti asawaletse kumanga Nyumbayo mpaka atalembera mfumu Dariyo kalata ndi kulandira yankho lake.
6 La traduction de la lettre qu'avaient écrite, pour le roi Darius, Thanthanaï, gouverneur de ce côté de l'Euphrate; Satharbuzanaï et les autres Apharsachéens, serviteurs du roi, sur la rive droite de l'Euphrate.
Iyi ndi kalata imene Tatenai bwanamkubwa wa dera la patsidya pa Yufurate, ndiponso Setari-Bozenai ndi anzake, akazembe amene anali mʼchigawo cha patsidya pa Yufurate, anatumiza kwa mfumu Dariyo
7 Ils avaient écrit pour lui un rapport, et voici en quels termes: Paix entière au roi Darius.
Analemba kalatayo motere: Kwa mfumu Dariyo: Mukhale ndi mtendere wonse.
8 Que le roi sache que nous sommes allés en Judée dans le temple du grand Dieu; or, ce temple est rebâti en pierres de choix, et des bois sont placés sur les murs, et ce travail est bien exécuté, et il va bien entre leurs mains.
Amfumu mudziwe kuti ife tinapita ku dziko la Yuda ku Nyumba ya Mulungu wamkulu. Nyumbayo ikumangidwa ndi miyala ikuluikulu ndipo akuyala matabwa pa makoma. Ntchitoyi ikugwiridwa mwachangu ndipo ikuyenda bwino kwambiri mwautsogoleri wawo.
9 Après l'avoir vu, nous avons interrogé les anciens, et nous leur avons ainsi parlé: Qui a fait en votre faveur un édit pour que vous bâtissiez ce temple, et que vous fassiez ces apprêts?
Ndipo tinawafunsa atsogoleriwo kuti, “Anakulolezani kuti mumangenso Nyumbayi ndi kutsiriza makoma ake ndani?”
10 Et nous leur avons demandé leurs noms, afin de te les faire connaître, et de prendre par écrit les noms de leurs chefs.
Tinawafunsanso mayina a atsogoleri awo, kuti tikalemba mayina atsogoleriwo tidzakudziwitseni kuti muwadziwe.
11 Et voici ce qu'ils nous ont répondu: Nous sommes les serviteurs du Dieu du ciel et de la terre, et nous relevons ce temple qui avait été construit il y a bien des années; un grand roi d'Israël l'avait bâti, et il l'avait établi pour son peuple.
Yankho limene anatipatsa ndi ili: “Ife ndife atumiki a Mulungu wa kumwamba ndi wa dziko lapansi, ndipo tikumanganso Nyumba imene mfumu ina yamphamvu ya Israeli inamanga ndi kuyitsiriza zaka zambiri zapitazo.
12 Mais, après cela, nos pères ont irrité le Dieu du ciel, qui les a livrés à Nabuchodonosor le Chaldéen, roi de Babylone; celui-ci a détruit ce temple, et emmené le peuple captif à Babylone.
Koma chifukwa chakuti makolo athu anakwiyitsa Mulungu wakumwamba, Iye anawapereka kwa Nebukadinezara Mkalideya, mfumu ya Babuloni, amene anawononga Nyumbayi ndi kutenga anthu onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
13 Mais, dans la première année de sa domination, Cyrus, roi des Perses, a fait un édit pour que le temple de Dieu fût rebâti.
“Komabe chaka choyamba cha Koresi, mfumu ya ku Babuloni, mfumu Koresiyo anapereka lamulo lakuti Nyumba ya Mulunguyi imangidwenso.
14 Et il a retiré du temple du roi les vases d'or et d'argent du temple de Dieu, enlevés de Jérusalem par Nabuchodonosor, et placés dans le temple de Babylone, et il les a remis au trésorier Sabanasar;
Ndipo ziwiya zagolide ndi zasiliva za ku Nyumba ya Mulungu zimene Nebukadinezara anazitenga mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu ndi kukaziyika mʼnyumba ya milungu ya ku Babuloni, anakazichotsa ku nyumba ya milungu ya ku Babuloniko ndi kuzipereka kwa Sesibazara, amene mfumu inamusankha kukhala bwanamkubwa.
15 Et il lui a dit: Prends tous ces vases, pars, et remets-les à leur place dans le temple de Jérusalem.
Tsono mfumuyo inamuwuza kuti, ‘Tenga ziwiyazi ukaziyike mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu. Ndipo Nyumba ya Mulunguyo ikamangidwenso pa maziko ake akale.’
16 Alors, ce Sabanasar est venu, et il a jeté les fondations du temple de Dieu à Jérusalem; depuis ce temps; jusqu'à cette heure, on a travaillé à le construire, et il n'est pas encore achevé.
“Choncho Sesibazarayo anabwera ndi kumanga maziko a Nyumba ya Mulunguyo mu Yerusalemu. Kuyambira tsiku limenelo mpaka lero yakhala ikumangidwa ndipo sinathebe.”
17 Et maintenant, si le roi le trouve bon, qu'il fasse faire des recherches dans le palais du trésor du roi de Babylone, afin de s'assurer que le roi Cyrus a fait un édit pour que le temple de Dieu fût relevé en Jérusalem; et, quand le roi s'en sera informé, qu'il envoie auprès de vous.
Nʼchifukwa chake ngati chingakukomereni amfumu, pachitike kafukufuku mʼnyumba yaufumu mosungira chuma ndi mabuku okhudza mbiri ya Babuloni kuti tione ngati mfumu Koresi inalamuladi za kumanganso Nyumba ya Mulungu mu Yerusalemu. Kenaka amfumu mutiwuze zomwe zikukondweretsani kuti mugamule pa nkhani imeneyi.

< Esdras 5 >