< Ézéchiel 45 >

1 Or, lorsque vous mesurerez la terre de votre héritage, vous en séparerez les prémices pour le Seigneur; c'est-à-dire un lieu consacré en cette terre, long de vingt-cinq mille mesures, large de vingt mille; et ce lien sera consacré dans toute son étendue.
“‘Mukamadzagawa dziko kuti fuko lililonse lilandire cholowa chake, mudzapatuleko chigawo chimodzi kuti chikhale cha Yehova. Mulitali mwake mudzakhale makilomita khumi ndi awiri ndi theka ndipo mulifupi mwake makilomita khumi. Malo onsewo adzakhale opatulika.
2 Et de cet espace vous séparerez pour le lieu saint un carré de cinq cents mesures de côté, avec un passage de cinquante coudées alentour.
Mʼkati mwa chigawo chimenechi, malo a mamita 250 mbali iliyonse adzakhala malo a Nyumba ya Mulungu. Pozungulira pake ponse padzakhala malo a mamita 25.
3 En mesurant la terre, vous mesurerez donc un espace qui aura vingt-cinq mille mesures de long sur vingt mille de large, et dans cet espace sera le saint des saints.
Mʼchigawo chopatulikacho muyeze malo a makilomita 12 ndi theka mulitali mwake, makilomita asanu mulifupi mwake. Pamenepo padzakhala malo opatulika kwambiri.
4 Ce sera dans la terre la part des prêtres qui serviront dans le lieu saint, et de ceux qui s'approcheront du Seigneur pour le servir. Et ce sera pour eux un espace où ils auront leurs maisons séparées du lieu saint.
Malo opatulika amenewa adzakhalanso a ansembe amene amatumikira ku malo opatulika, amene amayandikira Yehova kuti amutumikire. Pamenepo padzakhala malo omangapo nyumba zawo ndi malo omangapo Nyumba ya Mulungu.
5 Cette part aura vingt-cinq mille mesures de long sur vingt mille de large. Et aux lévites attachés au service du temple il sera assigné des villes où ils résideront.
Alevi otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzakhala ndi malo a makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake ndi makilomita asanu mulifupi mwake. Kumeneko ndiko kudzakhale midzi yawo.
6 Et à la possession des villes tu ajouteras un espace de vingt-cinq mille mesures de long, sur vingt mille de large, comme l'espace séparé pour le saint des saints; et les prémices de la terre seront pour toute la maison d'Israël.
“‘Moyandikana ndi malo opatulika, padzakhale malo a makilomita awiri ndi theka mulifupi mwake ndi makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake; kuti akhale malo a mzinda. Malo amenewa adzakhala a Aisraeli onse.
7 Quant au prince, il aura, outre ces parts, une part égale à ce qui est désigné pour les prémices du sanctuaire et pour l'espace des villes; elle sera en face des prémices du sanctuaire et en face de l'espace des villes, tant à l'occident que de l'occident à l'orient. Et la longueur sera la même que celle de l'une des parts, depuis les limites occidentales jusqu'aux limites orientales de la terre.
“‘Mfumu idzakhale ndi malo okhudzana ndi chigawo cha malo opatulika ndi cha mzinda. Malowo ayandikane ndi zigawozo chakummawa ndi chakumadzulo. Malowo atalike ngati chigawo chimodzi cha fuko la Israeli kuyambira ku malire akummawa mpaka ku malire akumadzulo.
8 Et ce sera la part du prince en Israël; et les princes d'Israël n'opprimeront plus mon peuple, et la maison d'Israël se partagera la terre par tribus.
Malowa adzakhala chigawo cha mfumu mu Israeli. Choncho mafumu anga sadzazunzanso anthu anga, koma adzidzalola Aisraeli kuti akhale ndi zigawo zawozawo.
9 Voici maintenant ce que dit le Seigneur Dieu: Que cela vous suffise, princes d'Israël; renoncez à l'iniquité et aux vexations; pratiquez la justice et l'équité; éloignez de mon peuple l'oppression, dit le Seigneur Dieu.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsono pakwana, inu akalonga a Israeli. Lekani nkhanza zanu ndi kupondereza anthu anga. Muzitsata chilungamo ndi kuchita zokomera anthu. Musapirikitse anthu anga mʼdzikomo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
10 Que votre balance soit juste, que votre mesure soit juste, que votre éphi soit juste selon la mesure.
Miyeso yanu yoyezera zinthu monga efa ndi bati zizikhala zokhulupirika.
11 Que votre éphi soit égal et uniforme, qu'il soit le dixième du gomor, et que le gomor soit uniforme.
Efa ndi bati ikhale miyeso yolingana kukula kwake. Muyeso wa homeri ukhale wokwanira mabati khumi, ukhalenso wokwanira maefa khumi. Ndiye kuti kukula kwa miyeso iwiriyo kuzidzatsata kukula kwa homeriyo.
12 Que vos poids pèsent vingt oboles, cinq sicles, quinze sicles; et que cinquante sicles fassent une mine.
Muyeso wa sekeli ukhale wokwanira magera makumi awiri. Muyeso wa mina ukhale wolemera masekeli 60.
13 Et voici les prémices que vous séparerez: une mesure pour le sixième d'un gomor de froment; le sixième d'un éphi pour un cor d'orge.
“‘Zopereka zomwe mudzidzapereka ndi izi: chimodzi mwa zigawo 60 za tirigu, barelenso chimodzimodzi ndiponso gawo limodzi la magawo asanu ndi limodzi la efa, kulitapa pa barele wa homeri.
14 Quant à l'huile, voici la règle: un cotyle d'huile sur dix cotyles; car dix cotyles font un gomor.
Gawo loyenera la mafuta, loyezedwa ndi bati, ndiponso chigawo mwa zigawo 100 za mafuta. Miyeso yake ili motere: mabati khumi afanana ndi homeri imodzi kapena kori imodzi.
15 Parmi les menus troupeaux, une tête sur dix sera offerte, en toutes les tribus d'Israël, pour les sacrifices soit d'holocaustes, soit d'hosties pacifiques, afin de vous sanctifier, dit le Seigneur Dieu.
Muperekenso nkhosa imodzi pa gulu lankhosa 200 za pa msipu wabwino wa mu Israeli. Izi zidzagwiritsidwa ntchito monga nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano ndi nsembe zopepesera milandu ya anthu. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
16 Et tout le peuple donnera ces prémices au prince d'Israël.
Anthu onse a mʼdzikomo azidzapereka zimenezi kwa mfumu ya Israeli.
17 Et le prince sera chargé d'offrir les holocaustes, les oblations et les libations les jours de fêtes, aux nouvelles lunes, les jours de sabbat et à toutes les fêtes de la maison d'Israël. Il offrira les offrandes pour le péché, les oblations, les holocaustes et les hosties pacifiques pour la purification de la maison d'Israël.
Udzakhala udindo wa mfumu kupereka zofunikira ku nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, ndi nsembe za zakumwa pa nthawi ya zikondwerero, chikondwerero cha mwezi watsopano ndi cha masabata, nthawi yonse ya zikondwerero zoyikika za Aisraeli. Mfumuyo idzapereka nsembe zopepesera machimo, nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano kuti zikhale nsembe zopepesera machimo a Aisraeli.
18 Voici ce que dit le Seigneur Dieu: Le premier mois, et le premier jour du mois, vous prendrez un veau sans tache pour purifier le sanctuaire.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba muzitenga mwana wangʼombe wamwamuna wopanda chilema ndi kuchita mwambo woyeretsa malo opatulika.
19 Et le prêtre prendra du sang de la purification; et il en mettra sur les portes du temple, sur les quatre coins du sanctuaire, sur l'autel et sur les jambages de la porte du parvis intérieur.
Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera machimoyo ndipo awapake pa mphuthu za Nyumba ya Mulungu, pa ngodya zinayi za pamwamba pa guwa lansembe ndi pa mphuthu za pa chipata cha bwalo la mʼkati.
20 Et tu feras pareillement le septième mois; le premier du mois, tu prendras une part de chaque chose, et vous purifierez le temple.
Muzichita chimodzimodzi pa tsiku la chisanu ndi chiwiri la mwezi, kuchitira aliyense amene wachimwa mosafuna kapena mosadziwa. Motero Nyumba ya Mulungu idzakhala yoyera.
21 Et le premier mois, le quatorzième jour de ce mois, vous aurez la fête de la Pâque; pendant sept jours, vous mangerez des azymes.
“‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita chikondwerero cha Paska, chikondwerero chake cha masiku asanu ndi awiri. Pa masiku amenewo muzidzadya buledi wopanda yisiti.
22 Et ce jour-là le prince sacrifiera un veau pour lui-même, pour le temple et pour tout le peuple de la terre; ce sera un sacrifice pour le péché.
Pa tsiku loyamba la chikondwererocho, mfumu ipereke nsembe ya ngʼombe yayimuna monga nsembe yopepesera machimo ake ndi machimo a anthu onse a mʼdziko.
23 Et pendant les sept jours de la fête il offrira en holocauste au Seigneur sept veaux et sept béliers sans tache, par jour, et il sacrifiera pour le péché un chevreau par jour.
Pa masiku asanu ndi awiri a chikondwererocho, mfumu ipereke kwa Yehova nsembe zopsereza izi: ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, zonsezi zopanda chilema. Pa masikuwa mfumu iziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo.
24 Et il fera cuire un gâteau pour chaque veau, et des gâteaux pour chaque bélier; et il y aura un hin d'huile par gâteau.
Pamodzi ndi ngʼombe iliyonse yayimuna ndi nkhosa iliyonse yayimuna, mfumu ipereke chopereka cha chakudya chokwanira efa imodzi ndiponso mafuta okwanira hini imodzi pa efa iliyonse.
25 Et le septième mois, le quinzième jour du mois, tu célèbreras une fête semblable à celle-ci, durant sept jours; il y aura les mêmes victimes pour le péché, les mêmes holocaustes, les mêmes oblations, les mêmes mesures d'huile.
“‘Pa nthawi ya chikondwerero cha masiku asanu ndi awiri, chimene chimayamba pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mfumuyo iziperekanso nsembe za mtundu womwewo: nsembe zopepesera machimo, nsembe zopsereza, nsembe za chakudya ndi za mafuta.’”

< Ézéchiel 45 >