< Ézéchiel 4 >

1 Et toi, fils de l'homme, prends une brique, et tu la placeras devant toi, et tu dessineras sur cette brique la ville de Jérusalem.
Mulungu anati, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga njerwa, uliyike pamaso pako ndipo ujambulepo chithunzi cha mzinda wa Yerusalemu.
2 Et tu y représenteras un siège, et tu bâtiras des ouvrages contre elle, et tu l'entoureras de palissades, et tu établiras des camps devant elle, et tu dresseras des balistes autour de son enceinte.
Ndipo uwuzinge mzindawo motere: uwumangire nsanja zowuzinga, uwumbire mitumbira ya nkhondo, uwumangire misasa ya nkhondo ndipo uyike zida zogumulira kuzungulira mzindawo.
3 Prends ensuite pour toi-même une poêle de fer; puis tu en feras un mur de fer, que tu placeras entre toi et la ville; et tu tourneras ton visage contre la ville, et elle sera assiégée, et tu l'assiégeras; or ceci est un signe pour les enfants d'Israël.
Kenaka utenge chiwaya chachitsulo uchiyike ngati khoma lachitsulo pakati pa iwe ndi mzindawo. Uyangʼanitsitse mzindawo ndipo udzakhala wozingidwa ndi nsanja za nkhondo. Choncho umangire nsanja zankhondo. Chimenechi chidzakhala chizindikiro kwa Aisraeli.
4 Et tu te coucheras sur le côté gauche, et tu mettras sur ce côté les iniquités de la maison d'Israël, au nombre de cent cinquante, égal à celui des jours où tu te seras couché sur ce côté, et tu porteras leurs iniquités.
“Tsono iwe ugonere kumanzere kwako ndipo ndidzayika pa iwe tchimo la Aisraeli. Iwe udzasenza tchimolo masiku onse amene udzagonere mbali imeneyo.
5 Et je t'ai chargé de leurs iniquités pour un nombre de cent quatre-vingt- dix jours, et tu porteras les iniquités de la maison d'Israël.
Ine ndakuyikira masiku okwana 390 malingana ndi zaka za machimo awo. Umu ndi mmene udzasenzere machimo a Aisraeli.
6 Et tu accompliras ce que j'ai dit d'abord; puis tu te coucheras sur le côté droit, et tu prendras les iniquités de la maison d'Israël, quarante jours; je te donne un jour pour une année.
“Utatha zimenezo udzagonerenso mbali ya kudzanja lamanja, ndipo udzasenza machimo a anthu a ku Yuda masiku makumi anayi, tsiku lililonse kuyimira chaka chimodzi.
7 Et tu tourneras le visage vers le siège de Jérusalem, et tu fortifieras ton bras, et tu prophétiseras contre elle.
Tsono udzayangʼanitsitse nsanja za nkhondo zozinga. Dzanja la mkanjo wako utalikwinya ndi dzanja lako utakweza, udzalosere modzudzula Yerusalemu.
8 Et voilà que je t'ai préparé des chaînes, et tu ne changeras pas de côté que les jours où tu dois être enchaîné ne soient accomplis.
Ine ndidzakumanga ndi zingwe kotero kuti sudzatha kutembenukira uku ndi uku mpaka utatsiriza masiku akuzingidwa ako.
9 Prends encore pour toi du froment, de l'orge, des fèves, des lentilles, du millet, de l'épeautre, et jette le tout dans un pot de terre; tu en feras ensuite des pains, pour autant de jours que tu dois dormir sur le côté, et tu en mangeras pendant cent quatre-vingt-dix jours.
“Tsono tenga tirigu ndi barele, nyemba ndi mphodza, mapira ndi mchewere; ndipo uyike zonsezi mʼmbale imodzi ndipo upange buledi wako. Uzidya pa masiku 390 amene udzakhala ukugonera mbali imodzi.
10 Et tu pèseras tes aliments, et tu en mangeras vingt-six sicles par jour, et tu les mangeras par intervalles.
Uyeze theka la kilogalamu la chakudyacho kuti uzidya tsiku lililonse kamodzi kokha.
11 Et tu boiras de l'eau à la mesure; tu boiras par intervalle, le sixième du hin.
Uyezenso zikho ziwiri zamadzi ndipo uzimwa tsiku ndi tsiku.
12 Et tu les mangeras comme des galettes d'orge, cuites sous la cendre, et tu les feras cuire sous la cendre d'un feu de mottes d'excréments humains aux yeux de tous.
Uzidya chakudya chako ngati momwe amadyera keke ya barele. Uzidzaphika chakudyacho anthu akuona pogwiritsa ntchito ndowe ya munthu ngati nkhuni.”
13 Et tu diras: Ainsi parle le Seigneur Dieu d'Israël. Ainsi les fils d'Israël mangeront des choses impures parmi les nations.
Yehova anati, “Chimodzimodzi anthu a Israeli adzadya chakudya chodetsedwa ku mayiko achilendo kumene Ine ndidzawapirikitsira.”
14 Et je dis: Que cela ne soit pas, Seigneur Dieu d'Israël; car jamais mon âme n'a été souillée de choses impures: depuis ma naissance jusqu'à ce jour, je n'ai point mangé de corps morts ni de bêtes déchirées par des bêtes, et jamais chair corrompue n'est entrée dans ma bouche.
Koma ine ndinati, “Zisatero, Ambuye Yehova! Ine sindinadziyipitsepo pa zachipembedzo. Kuyambira ubwana wanga mpaka tsopano, sindinadyepo kanthu kalikonse kopezeka katafa kapena kophedwa ndi zirombo za kutchire. Palibe nyama yodetsedwa pa zachipembedzo imene inalowa pakamwa panga.”
15 Et le Seigneur me dit: Voilà que je t'accorde des mottes de bouse de vache au lieu de mottes d'excréments humains, et tu prépareras tes pains sur ces mottes.
Iye anati, “Chabwino, ndidzakulola kuti uphike buledi wako ndi ndowe za ngʼombe mʼmalo mwa ndowe za munthu.”
16 Et il me dit: Fils de l'homme, voilà que je vais briser dans Jérusalem le soutien du pain, et ils le mangeront au poids, dans leur besoin, et ils boiront de l'eau à la mesure, dans leur défaillance.
Pambuyo pake anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, anthu a ku Yerusalemu ndidzawachepetsera chakudya. Anthuwo adzadya chakudya chochita kuyeza ndipo azidzadya mwa nkhawa. Azidzamwanso madzi ochita kuyeza ndiponso mwa mantha.
17 C'est au point qu'ils manqueront de pain et d'eau, et le frère tombera mort dans les bras de son frère, et ils se consumeront dans leurs iniquités.
Ndidzachita zimenezi kuti adzasowe chakudya ndi madzi. Choncho adzachita nkhawa akumapenyana ndipo adzatheratu ndi kuwonda chifukwa cha machimo awo.”

< Ézéchiel 4 >