< Ézéchiel 39 >

1 Et toi, fils de l'homme, prophétise maintenant contre Gog, et dis: Ainsi parle le Seigneur: Voilà que je suis contre toi, Gog, prince de Rhos, de Mésoch et de Thubal.
“Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala.
2 Je réunirai tes troupes, et je te guiderai; je te ferai partir des régions les plus lointaines de l'aquilon, et je te conduirai sur les montagnes d'Israël.
Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli.
3 Et alors je briserai ton arc dans ta main gauche, et tes flèches dans ta main droite, et je te renverserai
Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja.
4 Sur les montagnes d'Israël; et tu tomberas, toi et ceux qui t'appartiennent; et les nations qui t'accompagnent seront données à la multitude des oiseaux; et je t'ai donné toi-même à tous les oiseaux et à toutes les bêtes fauves des champs pour qu'ils te dévorent.
Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo.
5 Tu tomberas sur la face de la terre; car moi j'ai parlé, dit le Seigneur.
Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
6 Puis je lancerai la flamme sur Gog et sur les îles qui demeuraient en paix, et elles sauront que je suis le Seigneur.
Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
7 Et mon saint nom sera connu au milieu de mon peuple d'Israël, et ils ne profaneront plus mon saint nom, et les nations sauront que je suis le Seigneur saint en Israël.
“Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli.
8 Voilà que le jour est venu, et l'on saura qu'il est venu, dit le Seigneur; le voilà le jour dont j'avais parlé.
Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.
9 Les habitants des villes en sortiront, et ils se chaufferont en brillant les armes, les boucliers, les épieux, les arcs, les flèches, les bâtons et les javelines; et ils en allumeront leur feu pendant sept ans.
“Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
10 Et ils ne prendront plus de bois dans les champs, et ils n'abattront plus d'arbres dans les forêts; mais ils feront du feu avec les armes, et ils pilleront ceux qui les ont pillés, et ils dépouilleront ceux qui les ont dépouillés, dit le Seigneur.
Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.
11 Et ceci adviendra: en ce jour-là je donnerai à Gog une place de renom, un sépulcre en Israël; ce sera le cimetière des voyageurs du côté de la mer, et l'on entourera de murs l'entrée de la vallée. Là on enterrera Gog et toute sa multitude, et ou l'appellera le cimetière de Gog.
“Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
12 Et la maison d'Israël les y enterrera, afin qu'en sept mois la terre soit purifiée;
“Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko.
13 Et tout le peuple de la terre les y enterrera; et ce sera pour eux une place de renom, le jour où Israël sera glorifié, dit le Seigneur.
Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
14 Et ils ne cesseront pas d'envoyer des hommes qui parcourront la contrée pour ensevelir ceux qui seraient restés sur la face de la terre, et la purifier en sept mois; et ces hommes chercheront avec soin.
“Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo.
15 Et chacun de ceux qui parcourront la terre, à la vue d'un ossement humain, placera auprès une marque, afin que les fossoyeurs l'enterrent dans la vallée, au cimetière de Gog.
Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
16 Car le nom de la vallée sera Cimetière; et la terre sera purifiée.
(Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.
17 Et toi, fils de l'homme, dis: Ainsi parle le Seigneur: Dis à tout oiseau du ciel et à toute bête des champs: Rassemblez-vous, et partez; réunissez-vous de tous les alentours pour mon sacrifice, que je vous ai préparé, grand sacrifice sur les montagnes d'Israël; et mangez-en les chairs, et buvez-en le sang.
“Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi.
18 Mangez les chairs des géants; buvez le sang des princes de la terre; mangez des béliers, des bœufs, des boucs et des bœufs, tous bien engraissés.
Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani.
19 Mangez de la chair à satiété; buvez du sang jusqu'à l'ivresse; c'est la chair et le sang de mon sacrifice, que je vous ai préparé.
Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera.
20 Et vous serez rassasiés à ma table de la chair du cavalier et du cheval, du géant et de tout guerrier, dit le Seigneur.
Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.
21 Et je mettrai en vous ma gloire, et toutes les nations verront mon jugement que j'aurai exécuté, et ma main que j'aurai portée sur eux.
“Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo.
22 Et la maison d'Israël saura de ce jour-là et pour tous les temps que je suis le Seigneur leur Dieu.
Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
23 Et les nations sauront que la maison d'Israël a été captive à cause de ses péchés, et qu'en punition de ce qu'elle m'a répudié, j'ai détourné d'elle mon visage; que je l'ai livrée à ses ennemis, et qu'elle est tombée sous le glaive.
Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo.
24 Je les ai traités selon leurs impuretés et leurs égarements, et j'ai détourné d'eux mon visage.
Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.
25 C'est pourquoi voici ce que dit le Seigneur Maître: Maintenant je ramènerai les captifs en Jacob, et je ferai miséricorde à la maison d'Israël, et je serai jaloux pour l'amour de mon saint nom.
“Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera.
26 Et ils subiront leur déshonneur et l'iniquité qu'ils ont commise quand ils habitèrent leur terre en paix; et nul ne les épouvantera,
Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine.
27 Lorsque je les aurai retirés d'entre les nations et réunis de toutes les contrées des gentils; et en présence des nations je serai sanctifié parmi eux.
Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera.
28 Et ils sauront que je suis le Seigneur leur Dieu, quand je me serai manifesté à eux en présence des nations.
Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo.
29 Et je ne détournerai plus d'eux mon visage, parce que j'aurai assouvi ma colère contre la maison d'Israël, dit le Seigneur Maître.
Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

< Ézéchiel 39 >