< Ézéchiel 38 >

1 Et la parole du Seigneur me vint, disant:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 Fils de l'homme, tourne ton visage contre la terre de Magog et contre Gog, prince de Rhos, de Mésoch et de Thubal, et prophétise contre lui.
“Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Gogi, wa ku dziko la Magogi, amene ali kalonga wamkulu wa mzinda wa Mesaki ndi Tubala. Umuyimbe mlandu.
3 Et dis-lui: Ainsi parle le Seigneur Maître: Voilà que je suis contre toi, prince de Rhos, de Mésoch et de Thubal.
Umuwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa ku Mesaki ndi Tubala.
4 Je rassemblerai ton peuple et toute ton armée, chevaux et cavaliers, tous portant cuirasse; troupe nombreuse armée d'écus, de casques et de glaives.
Ndidzakuzunguza, ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako. Ndidzakutulutsa iweyo pamodzi ndi gulu lako lonse la nkhondo, akavalo ako ndi okwerapo ake. Onse adzakhala atanyamula zida za nkhondo, zishango ndi malihawo ndipo malupanga awo adzakhala osolola.
5 Perses, Éthiopiens et Libyens, tous portant casque et bouclier,
Pamodzi ndi iwowo, padzakhalanso ankhondo a ku Perisiya, ku Kusi, ndi ku Puti. Onsewa adzakhala atanyamula zishango ndi kuvala zipewa zankhondo.
6 Gomer et tous ceux qui lui appartiennent, la maison de Thorgama aux dernières limites du nord, et tous ceux qui lui appartiennent, et beaucoup de nations seront avec toi.
Padzakhalanso Gomeri pamodzi ndi ankhondo ake onse ndiponso banja la Togarima ndi gulu lake lonse lankhondo lochokera kutali kumpoto. Padzakhaladi mitundu yambiri ya anthu pamodzi ndi iwe.
7 Prépare-toi, sois tout prêt, toi et toute ta troupe réunie autour de toi, et sois pour moi un rempart;
“‘Konzekani! Mukhaledi okonzeka, iweyo pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo limene lakusonkhanira. Iweyo udzawatsogolera pokamenya nkhondo.
8 Et il se préparera à la fin de bien des jours, et à la fin des temps il viendra, et il entrera dans une terre sauvée du glaive, quand les peuples de maintes nations étaient rassemblés contre la terre d'Israël, qui avait été entièrement dévastée; et il est venu d'entre les gentils, et ils habiteront tous en paix.
Pakapita masiku ambiri ndidzakuyitana. Zaka zikubwerazi ndidzakulowetsa mʼdziko limene lapulumuka ku nkhondo. Anthu ake anasonkhanitsidwa kuchokera ku mitundu ya anthu ambiri nʼkukakhazikika pa mapiri a Israeli amene kwa nthawi yayitali anali ngati chipululu. Anthu onsewa tsopano akukhala mwa mtendere.
9 Et tu te répandras comme la pluie; et comme une nuée tu viendras couvrir la terre, et tu seras là, toi et tous ceux qui t'appartiennent, et beaucoup de nations avec toi.
Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse ndiponso mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe mudzabwera ngati mphepo yamkuntho. Mudzaphimba dziko lonse ngati mitambo.
10 Or voici ce que dit le Seigneur Maître: En ce jour-là ceci adviendra: des pensées s'élèveront en ton cœur, et tu concevras de mauvais desseins.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limenelo mu mtima mwako mudzabwera maganizo ofuna kukonzekera kuchita zoyipa.
11 Et tu diras: J'entrerai en une terre répudiée; je marcherai contre des hommes qui vivent dans le repos, qui demeurent chez eux en paix, qui habitent une terre où il n'y a ni remparts, ni portes, ni verrous.
Iwe udzanena kuti, ‘Ndikukathira nkhondo dziko la midzi yopanda mipanda; ndikathira nkhondo anthu okhala mwamtendere, anthu amene satchinjirizidwa ndi mipanda, zipata kapena mipiringidzo.
12 Saisis donc cette proie; pille ces dépouilles; porte les mains sur cette terre déserte et repeuplée, sur ce peuple rassemblé d'entre maintes nations, ayant acquis des richesses, et habitant l'intérieur des terres.
Ndipita kukalanda chuma chawo ndi kukafunkha zinthu zawo. Ndidzalimbana ndi midzi imene kale inali mabwinja. Ndikathira nkhondo anthu amene anasonkhanitsidwa kuchokera kwa anthu a mitundu ina. Iwowa ali ndi ziweto zambiri, katundu wochuluka ndiponso amakhala pakatikati pa dziko lapansi.’
13 Saba et Dédan, les marchands de Carthage et toutes leurs villes te diront: Tu es venu pour saisir une proie et piller des dépouilles; tu as rassemblé tes troupes pour prendre de l'argent et de l'or, pour emporter des richesses et recueillir du butin.
Anthu a ku Seba, a ku Dedani ndiponso amalonda a ku Tarisisi pamodzi ndi midzi yake yonse adzakufunsa kuti, ‘Kodi wabwera kudzafunkha? Kodi wasonkhanitsa gulu lako la nkhondo kudzalanda chuma, kudzatenga siliva ndi golide, ziweto ndi katundu kuti zikhale zofunkha zochuluka?’”
14 À cause de cela, prophétise, fils de l'homme, et dis à Gog: Ainsi parle le Seigneur: N'est-ce pas dans le temps même où mon peuple Israël sera en paix dans sa demeure, que tu t'élèveras?
“Nʼchifukwa chake, iwe mwana wa munthu, nenera ndipo uwuze Gogi kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene anthu anga adzakhala pa mtendere, iwe udzanyamuka.
15 Alors tu viendras des régions les plus lointaines du nord, et il y aura avec toi divers peuples, tous rassemblés en grand nombre, immense armée de cavaliers.
Udzabwera kuchokera ku dziko lako kutali kumpoto, iwe pamodzi ndi mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe, onse okwera akavalo, gulu lankhondo lalikulu ndi lamphamvu.
16 Et tu marcheras contre mon peuple d'Israël, comme une nuée qui vient couvrir la terre. Or ceci arrivera vers les jours de la fin: je te conduirai sur ma terre, afin que toutes les nations me connaissent quand devant elles je me sanctifierai en toi.
Udzabwera kudzalimbana ndi anthu anga Aisraeli ngati mtambo wophimba dziko. Masiku amenewo, iwe Gogi, ndidzabwera nawe kuti ulimbane ndi dziko langa, kuti anthu a mitundu ina andidziwe Ine, pamene ndidzaonetsa kuyera kwanga pa zimene ndidzakuchite iweyo.
17 Voici ce que le Seigneur dit à Gog: Tu es celui de qui j'ai parlé dès les jours d'autrefois, par la voix de mes serviteurs les prophètes d'Israël, annonçant qu'en ces années et ces jours-là je te conduirais contre eux.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi iwe si amene ndinayankhula za iwe masiku amakedzana kudzera mwa atumiki anga aneneri a Israeli? Pa zaka zambiri iwo ankalengeza kuti ndidzawutsa iwe kuti udzalimbane ndi Israeli.
18 Et ceci adviendra: le jour où Gog viendra sur la terre d'Israël, dit le Seigneur Maître, ma colère éclatera
Zimene chidzachitika pa tsiku limenelo ndi izi: Gogi akadzathira nkhondo dziko la Israeli, mkwiyo wanga woopsa udzayaka. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.
19 Avec ma jalousie; j'ai parlé dans le feu de ma colère; et, en vérité, ce jour-là il y aura un grand ébranlement dans la terre d'Israël.
Chifukwa cha mkwiyo ndi ukali wanga woyakawo Ine ndikunenetsa kuti pa nthawi imeneyo padzakhala chivomerezi chachikulu mʼdziko la Israeli.
20 Et les poissons de la mer trembleront en présence du Seigneur, ainsi que les oiseaux du ciel, et les bêtes des champs, et les reptiles qui se traînent à terre, et tous les hommes qui seront encore sur la face de la terre. Et les montagnes se fendront, et les vallons seront bouleversés, et toute muraille s'écroulera.
Nsomba za mʼnyanja, mbalame zamumlengalenga, zirombo zakuthengo, cholengedwa chilichonse chimene chimakwawa pansi, ndiponso anthu onse okhala pa dziko lapansi, adzanjenjemera pamaso panga. Mapiri adzangʼambika, malo okwera kwambiri adzagumuka ndipo khoma lililonse lidzagwa pansi.
21 Mais alors contre lui-même j'appellerai tous les épouvantements, dit le Seigneur; et l'épée de l'homme se tournera contre son frère.
Ndidzawutsira Gogi nkhondo kuchokera ku mapiri anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. Anthu a Gogiyo adzaphana okhaokha ndi malupanga.
22 Et à mon tour j'exercerai sur lui mes jugements par la peste, par le sang, par les inondations, par une grêle de pierres; et je ferai tomber sur lui, sur ses compagnons et sur toutes les nations qui seront avec lui, une pluie de soufre et de feu.
Ine ndidzamulanga ndi mliri ndi imfa. Ndidzagwetsa mvula yoopsa ya matalala, ndiponso sulufule ndi miyala ya moto pa iye ndi pa asilikali ake ndiponso pa mitundu yambiri ya anthu imene ili naye.
23 Et je serai célébré, et je serai sanctifié, et je serai glorifié; et je me ferai connaître devant maintes nations, et elles sauront que je suis le Seigneur.
Motero ndidzadzionetsa kuti ndine wamphamvu ndi woyera. Ndiponso ndidzadziwika pamaso pa anthu a mitundu ina yambiri. Momwemo adzadziwadi kuti Ine ndine Yehova.’”

< Ézéchiel 38 >