< Ézéchiel 37 >

1 Et la main du Seigneur fut sur moi, et le Seigneur me ravit en esprit; et il me déposa au milieu d'un champ, et ce champ était rempli d'ossements humains.
Dzanja la Yehova linali pa ine, ndipo Mzimu wa Yehova unandinyamula nʼkukandikhazika pakati pa chigwa. Chigwacho chinali chodzaza ndi mafupa.
2 Et le Seigneur me conduisit tout autour de ces os, et voilà qu'il y en avait une multitude sur la surface du champ, et ils étaient tout desséchés.
Yehova anandiyendetsa uku ndi uku pakati pa mafupawo. Mafupawo anali ochuluka kwambiri mʼchigwa monsemo ndipo anali owuma kwambiri.
3 Et le Seigneur me dit: Fils de l'homme, ces os revivront-ils? Et je répondis: Seigneur, Seigneur, vous le savez.
Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi mafupa amenewa angakhalenso ndi moyo?” Ndinayankha kuti, “Inu Ambuye Yehova, Inuyo nokha ndiye mukudziwa.”
4 Et il me dit: Prophétise sur ces ossements, et dis-leur: Ossements desséchés, écoutez la parole du Seigneur.
Pamenepo anandiwuza kuti, “Lengeza kwa mafupa amenewa ndi kuwawuza kuti amve mawu a Ine Yehova!
5 Or voici ce que dit le Seigneur à ces ossements: Je vais amener sur vous un souffle de vie,
Uwawuze kuti zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena kwa mafupa ndi izi: Ndidzawuzira mpweya mwa inu, ndipo mudzakhalanso ndi moyo.
6 Et je poserai sur vous des nerfs, et j'amènerai sur vous des chairs, et sur vous j'étendrai de la peau, et je mettrai en vous mon souffle, et vous vivrez, et vous saurez que je suis le Seigneur.
Ndidzakupatsani mitsempha ndi mnofu. Ndiponso ndidzakukutani ndi khungu. Pambuyo pake ndidzawuzira mpweya mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
7 Et je prophétisai comme le Seigneur me l'avait prescrit, et ceci advint pendant que je prophétisais: Voilà que les ossements s'agitèrent et vinrent se placer chacun dans sa jointure.
Ndipo ndinanenera monga anandilamulira. Ndipo pamene ndinkanenera, ndinamva gobedegobede, ndipo mafupa aja anayamba kulumikizana, fupa ku fupa linzake.
8 Et je regardai; et voilà que sur les os des nerfs et des chairs se produisirent, et de la peau les recouvrit; mais l'esprit n'était pas encore en eux.
Ine ndinayangʼana, ndipo mitsempha ndi mnofu zinabwera pa mafupawo ndipo khungu linaphimba pamwamba pake, koma munalibe mpweya mwa iwo.
9 Et le Seigneur me dit: Prophétise à l'esprit, prophétise, fils de l'homme, et dis à l'esprit: Voici ce que dit le Seigneur: Viens des quatre vents, et souffle dans ces morts, et qu'ils vivent.
Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Nenera kwa mpweya, nenera iwe mwana wa munthu ndi kuwuza mpweya mawu a Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Bwera kuno iwe mpweya. Bwera kuchokera ku mbali zonse zinayi ndi kudzawuzira anthu ophedwawa kuti akhalenso ndi moyo.’
10 Et je prophétisai comme le Seigneur me l'avait prescrit, et l'esprit entra dans les morts, et ils furent vivants, et ils se dressèrent sur leurs pieds en immense multitude.
Choncho ndinanenera monga anandilamulira ndipo mpweya unalowa mwa iwo; apo anthu akufawo anakhala ndi moyo, nayimirira ndipo linali gulu lalikulu lankhondo.”
11 Et le Seigneur me parla, disant: Fils de l'homme, ces os sont toute la maison d'Israël, et eux-mêmes disent: Nos ossements sont desséchés, notre espérance a péri, et nous sommes sans voix.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, mafupa awa ndi nyumba yonse ya Israeli. Iwo amanena kuti, ‘Mafupa athu awuma ndipo chiyembekezo chathu chatayika, ife tawonongeka!’
12 À cause de cela, prophétise et dis: Voilà que j'ouvre vos sépulcres, dit le Seigneur; je vais vous en faire sortir, et je vous introduirai en la terre d'Israël;
Nʼchifukwa chake nenera ndi kuwawuza kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu anthu anga, ndidzafukula manda anu, ndipo ndidzakutulutsanimo ndi kukubwezerani ku dziko la Israeli.
13 Et vous saurez que moi je suis le Seigneur, quand j'aurai ouvert vos sépulcres, et que de ces sépulcres j'aurai tiré mon peuple.
Ndipo inu, anthu anga, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene ndidzafukula manda anu ndikukutulutsanimo.
14 Et je vous donnerai mon esprit, et vous vivrez, et je vous établirai sur votre terre, et vous saurez que je suis le Seigneur. J'ai parlé, et j'exécuterai, dit le Seigneur.
Ine ndidzayika Mzimu wanga mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pambuyo pake ndidzakulowetsani mʼdziko lanulanu. Choncho mudzadziwa kuti Ambuye Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichitadi. Ndikutero Ine Yehova!’”
15 Et la parole du Seigneur me vint, disant:
Yehova anandiyankhula kuti:
16 Fils de l'homme, prends une baguette, et sur elle écris: Juda et tous les enfants d'Israël de son parti. Prends une autre baguette, et écris sur elle: Pour Joseph; puis une baguette pour Ephraïm; inscris enfin tous les enfants appartenant à Israël.
“Iwe mwana wa munthu, tenga ndodo ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Yuda ndi Aisraeli oyanjana nawo.’ Utengenso ndodo ina ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Efereimu, ndiye kuti fuko la Yosefe ndi Aisraeli onse oyanjana nawo.’
17 Et tu les réuniras ensemble pour n'être qu'une baguette, après les avoir liées, et elles seront dans ta main.
Ulumikize ndodo ziwirizi kuti zikhale ndodo imodzi mʼdzanja lako.
18 Et ceci adviendra: Lorsque les enfants de ton peuple te diront: Ne nous expliqueras-tu point ce que cela signifie?
“Anthu a mtundu wako akadzakufunsa tanthauzo la zimenezi
19 Tu leur diras: Ainsi parle le Seigneur: Voilà que je vais prendre la tribu de Joseph, qui est dans la main d'Éphraïm, et les tribus d'Israël qui appartiennent à celle-ci, et je les réunirai à la tribu de Juda, et elles ne formeront qu'une baguette dans la maison de Juda.
iwe udzawawuze mawu awa a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndidzatenga ndodo ya Yosefe imene ili mʼdzanja la Efereimu, ndi ya mafuko a Aisraeli oyanjana naye, ndi kuyilumikiza ku ndodo ya Yuda, kuti zikhale ndodo imodzi, ndipo zidzakhaladi ndodo imodzi mʼdzanja langa!’
20 Et les baguettes sur lesquelles tu as écrit seront en ta main en présence du peuple.
Ndodo ziwiri zimene udzalembepozo zikadzakhala mʼmanja mwako pamaso pa anthu onse,
21 Et tu leur diras: Ainsi parle le Seigneur Maître: Voilà que je vais retirer toute la maison d'Israël du milieu des nations où elle est entrée; je les rassemblerai d'entre toutes les contrées d'alentour, et je les ramènerai en la terre d'Israël.
udzawawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzawachotsa Aisraeli pakati pa anthu a mitundu ina kumene anapita ku ukapolo. Ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mbali zonse ndi kubwera nawo ku dziko lawolawo.
22 Et j'en ferai une nation dans la terre qui m'appartient et sur les montagnes d'Israël. Et il y aura pour eux un seul prince, et ils ne formeront plus deux nations, et ils ne seront plus jamais divisés en deux royaumes,
Ndidzawasandutsa mtundu umodzi mʼdzikomo, pa mapiri a Israeli. Padzakhala mfumu imodzi yowalamulira, ndipo sadzakhalanso mitundu iwiri kapena kugawikana maufumu awiri.
23 Afin de ne plus se souiller de leurs idoles; et je les préserverai de tous les dérèglements où ils sont tombés, et je les purifierai; et ils seront mon peuple, et moi, le Seigneur, je serai leur Dieu.
Sadzadziyipitsanso ndi mafano awo, kapena ndi zinthu zawo zonyansa, kapenanso ndi ntchito zawo zoyipa zilizonse. Ndidzawapulumutsa ku machimo awo onse ndi kuwayeretsa. Choncho adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
24 Et mon serviteur David sera prince au milieu d'eux; y aura pour eux tous un seul pasteur, parce qu'ils marcheront dans la voie de mes ordonnances et qu'ils garderont mes commandements et les pratiqueront.
“‘Mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu yawo, motero onsewa adzakhala ndi mʼbusa mmodzi. Iwo adzatsatira malamulo anga ndipo adzasamalira kusunga malangizo anga.
25 Et ils habiteront leur terre que j'ai donnée à mon serviteur Jacob, que leurs pères ont habitée; et eux-mêmes y habiteront. Et David, mon serviteur, sera leur prince dans tous les siècles.
Iwo adzakhala mʼdziko limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo, dziko limene makolo anu ankakhalamo. Iwo ndi ana awo pamodzi ndi zidzukulu zawo adzakhala kumeneko ndipo Davide adzakhala mfumu yawo kwa muyaya.
26 Et je ferai avec eux une alliance de paix; et mon alliance avec eux sera éternelle. Et j'établirai au milieu d'eux mon sanctuaire dans tous les siècles.
Ndidzachita nawo pangano lamtendere; lidzakhala pangano lamuyaya. Ndidzawakhazikitsa ndi kuwachulukitsa, ndipo ndidzayika malo anga opatulika pakati pawo kwamuyaya.
27 Et mon tabernacle sera chez eux, et je serai leur Dieu; et ils seront mon peuple.
Nyumba yanga yokhalamo idzakhala pakati pawo; Ine ndidzakhala Mulungu wawo, ndipo iwo adzakhala anthu anga.
28 Et les nations sauront que je suis le Seigneur qui sanctifie les fils d'Israël, en établissant chez eux mon sanctuaire pour tous les siècles.
Pamenepo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti Ine Yehova ndiye amene ndimasandutsa Israeli kukhala woyera, pamene malo anga opatulika adzakhala pakati pawo kwamuyaya!’”

< Ézéchiel 37 >