< Ézéchiel 36 >
1 Et toi, fils de l'homme, prophétise pour les montagnes d'Israël; montagnes d'Israël, écoutez la parole du Seigneur:
“Iwe mwana wa munthu, yankhula kwa mapiri a Israeli ndipo unene kuti, ‘Inu mapiri a Israeli, imvani mawu a Yehova.’
2 Voici ce que dit le Seigneur Maître: Parce que l'ennemi a dit contre vous: Bien, ces déserts éternels seront désormais en notre possession;
Ine Ambuye Yehova ndikuti: Mdani wanu ankanena kuti, ‘Aa! Dziko lamapiri lakalekale lija lasanduka lathu.’
3 À cause de cela, prophétise et dis: Parce que vous avez été méprisées, dit le Seigneur Maître, parce que vous avez été haïes de tous les peuples d'alentour, que vous avez été au pouvoir du reste des nations, et que vous êtes devenues leur fable et le sujet de leurs outrages;
Choncho nenera ndipo uwawuze kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza anakusakazani ndi kukuponderezani ku mbali zonse motero kuti munakhala mʼmanja mwa anthu a mitundu ina yonse ndipo anthu ankakunenani ndi kukunyozani,
4 À cause de cela, montagnes d'Israël, écoutez la parole du Seigneur; voici ce que dit le Seigneur aux montagnes et aux collines, aux torrents et aux vallées, à ces lieux qui ont été désolés et détruits, et aux villes qui ont été abandonnées, pillées et foulées aux pieds par les nations laissées alentour;
choncho, inu mapiri a Israeli, imvani zimene Ine Ambuye Yehova ndikuwuza mapiri ndi magomo, zigwembe ndi zigwa, mabwinja ndi mizinda yosiyidwa imene yakhala ikufunkhidwa komanso kunyozedwa ndi anthu a mitundu ina okuzungulirani.
5 À cause de cela: Puisque dans le feu de ma colère, dit le Seigneur Maître, j'ai parlé contre les autres nations et contre toute l'Idumée, pour s'être approprié avec joie ma terre comme leur héritage, méprisant les âmes, quand il s'agissait de piller et de détruire;
Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti: Mu mkwiyo wanga woopsa ndinayankhula kuyimba mlandu mitundu ina yonse ya anthu makamaka a ku Edomu. Iwowa mwa chimwemwe chodzaza tsaya ndi mwa nkhwidzi analanda dziko langa ndi kulisandutsa lawo ndi kutengeratu dziko la msipu kukhala lawo.’
6 Prophétise donc en faveur de la terre d'Israël, et dis aux montagnes et aux collines, aux vallées et aux forêts: Ainsi dit le Seigneur: Voilà que j'ai parlé dans ma jalousie et ma colère, parce que vous avez subi les outrages des nations.
Nʼchifukwa chake, lengeza ku dziko la Israeli, ndipo uwuze mapiri ndi magomo, zigwembe ndi zigwa kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndikuyankhula ndi mtima wokwiya kwambiri chifukwa inu munalandira chitonzo cha anthu a mitundu ina.’
7 Je lèverai la main contre les nations qui vous entourent; elles-mêmes porteront la peine de leurs outrages.
Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndikulumbira nditakweza dzanja langa kuti mitundu ya anthu idzatozedwanso.
8 Et vous, montagnes d'Israël, mon peuple mangera vos grappes et vos fruits; car ils espèrent revenir.
“Koma Inu mapiri a Israeli mudzaphukanso nthambi ndipo mudzawabalira zipatso anthu anga a Israeli, pakuti ali pafupi kubwerera kwawo.
9 Voilà que je suis près de vous, et je me retournerai vers vous, et vous serez labourées, et vous serez ensemencées.
Taonani, Ine ndili mbali yanu ndipo ndidzakukomerani mtima. Mudzalimidwa ndi kudzalidwa.
10 Sur vous je multiplierai les hommes, et toute la maison d'Israël, jusqu'à ce qu'elle soit complète; et les villes seront habitées, et les déserts couverts de demeures.
Ndidzachulukitsa chiwerengero cha anthu anu, nyumba yonse ya Israeli. Mʼmizinda mudzakhalanso anthu ndipo mabwinja adzamangidwanso.
11 Et je multiplierai sur vous les hommes et les troupeaux, et je vous rendrai peuplées comme en vos premiers jours, et je vous comblerai de biens comme jadis; et vous saurez que je suis le Seigneur.
Ndidzachulukitsa chiwerengero cha amuna pamodzi ndi ziweto zomwe, ndipo adzachuluka kwambiri ndi kubereka ana ambiri. Ndidzakhazika anthu mʼdzikomo monga analili kale, ndi kukulemeretsani kuposa kale. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
12 Et je ferai naître sur vous des hommes, mon peuple Israël; et ils vous possèderont, et vous serez leur héritage; et jamais plus vous ne serez sans enfants.
Ndidzachititsa anthu kuyenda pa inu, ndiye kuti inu anthu anga Aisraeli. Iwowo adzakhazikika pa inu, ndipo inu mudzakhala cholowa chawo. Simudzalandanso ana awo.
13 Voici ce que dit le Seigneur Maître: Parce que l'on t'a dit: Tu es une terre qui dévore les hommes, et que tu as été privée de ta nation et de tes enfants;
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza anthu amanena kuti, ndiwe dziko limene limadya anthu ake ‘kulanda ana a mtundu wake,’
14 À cause de cela, tu ne dévoreras plus les hommes et tu ne seras plus privée de ta nation ni de tes enfants, dit le Seigneur Maître.
nʼchifukwa chake, simudzadyanso anthu kapena kulanda ana a mtundu wako. Ine Ambuye Yehova ndikutero.
15 Et l'on n'entendra plus contre vous les injures des gentils, et vous ne subirez plus les outrages des peuples, dit le Seigneur Maître.
Sindidzakulolaninso kumva mnyozo wa anthu a mitundu ina, kapena kupirira kunyogodola kwawo kapenanso kupunthwitsanso anthu a mʼdziko lako. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
16 Et la parole du Seigneur me vint, disant:
Yehova anandiyankhulanso kuti:
17 Fils de l'homme, la maison d'Israël a demeuré sur sa terre; et ils l'ont souillée en leurs voies par leurs idoles et leurs impuretés; et leurs voies sont devenues à mes yeux comme la souillure d'une femme en son impureté.
“Iwe mwana wa munthu, pamene anthu a Israeli ankakhala mʼdziko lawolawo, analiyipitsa ndi makhalidwe awo ndiponso zochita zawo. Machitidwe awo pamaso panga anali onyansa pa zachipembedzo ngati msambo wa mkazi amene ali pa nthawi yake.
18 Et j'ai répandu sur eux ma colère.
Tsono ndinawalanga chifukwa cha magazi amene anakhetsa mʼdzikomo, ndiponso chifukwa anayipitsa dziko ndi mafano awo.
19 Et je les ai dispersés parmi les nations, et je les ai vannés à travers les royaumes; car je les ai jugés selon leur voie et selon leur péché.
Ndinawamwaza pakati pa anthu a mitundu ina ndipo anabalalikira mʼmayiko onse. Ndinawalanga molingana ndi makhalidwe awo ndi zochita zawo.
20 Et ils se sont mêlés aux nations où ils étaient entrés, et ils ont profané mon saint nom; car les nations disaient: Voilà le peuple du Seigneur; voilà ceux qui sont sortis de son héritage!
Atafika kwa anthu a mitundu ina, kulikonse kumene anapitako, anayipitsa dzina langa loyera. Zinatero popeza anthu ponena za iwo ankanena kuti, ‘Awa ndi anthu a Yehova, komatu anachotsedwa ku dziko lake.’
21 Cependant je les ai épargnés à cause de mon saint nom que la maison d'Israël avait profané chez les nations où elle était allée.
Koma Ine ndinkadera nkhawa dzina langa loyera, limene Aisraeli analiyipitsa pakati pa anthu a mitundu ina kumene anapitako.
22 À cause de cela, dis à la maison d'Israël: Je ne fais point cela à cause de vous, dit le Seigneur, mais à cause de mon saint nom, que vous avez profané chez les nations où vous êtes allés.
“Nʼchifukwa chake awuze Aisraeliwo kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndidzachita zimene ndidzachitezo osati chifukwa cha inuyo Aisraelinu ayi, koma chifukwa cha dzina langa, limene mwaliyipitsa pakati pa anthu a mitundu ina kumene munapitako.
23 Et je sanctifierai mon grand nom, ce nom profané parmi les gentils, profané par vous au milieu d'eux; et les nations sauront que je suis le Seigneur quand j'aurai été sanctifié par vous devant leurs yeux.
Ndidzaonetsa chiyero cha dzina langa lotchuka, limene layipitsidwa pakati pawo. Anthu a mitundu inayo atadzazindikira kuti ndaonetsa kudzera mwa inu kuti dzina langa ndi loyera, iwo adzadziwanso kuti Ine ndine Yehova. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
24 Et je vous retirerai des nations, et je vous rassemblerai de toutes les contrées, et je vous ramènerai en votre terre.
“Pakuti Ine ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina. Ndidzakusonkhanitsani kuchoka ku mayiko onse ndi kukubwezerani ku dziko lanulanu.
25 Et je vous arroserai d'une eau pure, et vous serez purifiés de toutes vos impuretés et de toutes vos idoles, et je vous purifierai moi-même;
Ndidzakuwazani madzi oyera, ndipo mudzakhala oyera mtima. Zonse zimene zimakuyipitsani zidzachoka. Ndidzakuyeretsani pochotsa mafano anu onse.
26 Je vous donnerai un nouveau cœur, et je mettrai en vous un esprit nouveau; j'ôterai de votre sein votre cœur de roche, et j'y placerai un cœur de chair.
Ndidzakupatsani mtima watsopano ndi kulowetsa mzimu watsopano mwa inu. Ndidzachotsa mwa inu mtima wanu wowuma ngati mwala ndi kukupatsani mtima wofewa ngati mnofu.
27 Et je mettrai en vous mon esprit, et je vous ferai marcher dans la voie de mes ordonnances, et vous garderez mes jugements, et vous les mettrez en pratique.
Ndipo ndidzayika Mzimu wanga mwa inu ndipo ndidzakuthandizani kutsatira malangizo anga ndi kukusungitsani mosamala kwambiri malamulo anga.
28 Et vous demeurerez en la terre que j'ai donnée à vos pères; et vous serez mon peuple, et moi, je serai votre Dieu.
Mudzakhala mʼdziko limene ndinapatsa makolo anu. Mudzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu.
29 Et je vous sauverai de toutes vos impuretés; et j'appellerai le froment, et je le multiplierai, et je ne ferai point venir sur vous la famine.
Ndidzakupulumutsani ku zonse zokuyipitsani. Ndidzakuchulukitsirani tirigu ndipo sindidzakugwetseraninso njala.
30 Et je multiplierai les fruits de l'arbre et les récoltes du champ, afin que vous ne subissiez plus l'outrage de la faim parmi les nations.
Ndidzachulukitsa zipatso za mʼmitengo yanu ndi zokolola za mʼmunda mwanu, kotero kuti simudzanyozedwanso pakati pa anthu a mitundu ina chifukwa cha njala.
31 Et vous vous souviendrez alors de vos voies corrompues et de vos habitudes déréglées; et vous vous détesterez vous-mêmes, en considérant vos péchés et les abominations de vos idoles.
Pamenepo mudzakumbukira makhalidwe anu oyipa ndi ntchito zanu zoyipa. Machimo anu ndi ntchito zanu zonyansa zidzakuchititsa nokha manyazi.
32 Mais je ne ferai point cela à cause de vous, dit le Seigneur Maître; sachez-le bien. Soyez donc honteuse et confuse, maison d'Israël, à cause de vos voies.
Tsono dziwani kuti Ine sindidzachita zimenezi chifukwa cha inuyo ayi, ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse. Ndiyetu chitani manyazi ndipo mugwetse nkhope zanu, inu Aisraeli chifukwa cha makhalidwe anu!
33 Voici ce que dit Adonaï le Seigneur: Le jour où je vous purifierai de toutes vos iniquités, où je repeuplerai vos villes, où l'on rebâtira des demeures dans les lieux dévastés;
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limene ndidzayeretse machimo anu onse, ndidzayikamonso anthu mʼmizinda yanu, ndipo ndidzamanganso nyumba pa mabwinja.
34 Où cette terre désolée sera cultivée, au lieu d'être effacée, comme elle l'était aux yeux de tous les passants;
Dziko limene linasanduka chipululu lizidzalimidwanso. Mʼmalo moti aliyense wopitamo alione dzikolo ngati chipululu tsopano adzaliona lolimidwa.
35 Ils diront: Cette terre ravagée est devenue comme un jardin de délices; ses villes, jadis dépeuplées, détruites, abattues, sont relevées maintenant et fortifiées.
Iwo adzati, ‘Dziko ili, limene linali chipululu, lasanduka munda wa Edeni. Mizinda imene inali mabwinja osiyidwa ndi owonongedwa, tsopano ndi yotetezedwa ndi yokhalamo anthu.
36 Et les autres nations, toutes celles qui vous entourent encore, sauront que moi, le Seigneur, j'ai réédifié des ruines et replanté des terres en friche; moi, le Seigneur, j'ai parlé, et j'exécuterai.
Ndipo anthu a mitundu ina okhala pafupi nanu amene anatsala adzadziwa kuti Ine Yehova ndine amene ndinamanganso mizinda yowonongeka ndi kudzalanso zinthu zatsopano mʼmalo mʼmene munali chipululu. Ine Yehova ndayankhula ndipo ndidzazichitadi.’
37 Voici ce que dit encore Adonaï le Seigneur: La maison d'Israël me demandera en outre une chose, et je la lui accorderai: je multiplierai chez eux les hommes comme des troupeaux de brebis,
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzalolanso Aisraeli kuti andipemphe zoti ndiwachitire: Ndidzachulukitsa anthu awo ngati nkhosa.
38 Comme des brebis saintes, comme les brebis de Jérusalem en ses fêtes. Ainsi les villes dépeuplées seront remplies de troupeaux d'hommes, et ils sauront que je suis le Seigneur.
Adzachulukadi ngati nkhosa zomwe ankapereka ngati nsembe ku Yerusalemu pa nthawi za chikondwerero. Choncho mizinda ya mabwinja idzadzaza ndi anthu. Zikadzatero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”