< Ézéchiel 31 >
1 Et en l'année onzième, le troisième mois, le premier jour du mois, la parole du Seigneur me vint, disant:
Pa tsiku loyamba la mwezi wachitatu, chaka cha khumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti:
2 Fils de l'homme, dis au Pharaon, roi d'Égypte, et à son peuple: À qui t'es-tu comparé en ton orgueil?
“Iwe mwana wa munthu, unene kwa Farao mfumu ya Igupto ndi gulu lake lankhondo. Awawuze kuti, “‘Kodi mu ukulu wanu ndani angafanane ndi inu?
3 Voilà qu'Assur était un cyprès du Liban, et il était beau par ses branches, par la hauteur de sa tige et par sa cime s'élevant au milieu des nuées.
Taonani, ndidzakufanizirani ndi mtengo wa mkungudza wa ku Lebanoni, wa nthambi zokongola zochititsa mthunzi mʼnkhalango. Unali wautali, msonga zake zooneka pamwamba pa nkhalango.
4 Les eaux l'avaient nourri; l'abîme l'avait fait croître en conduisant ses fleuves autour de ses racines, et ses ondes se répandaient vers tous les arbres des champs.
Madzi ndiwo ankawukulitsa mkungudzawo, akasupe ozama ankawutalikitsa. Mitsinje yake inkayenda mozungulira malo amene unaliwo ndipo ngalande zake zinkafika ku mitengo yonse ya mʼmunda.
5 Aussi dépassait-il en hauteur tous les arbres des champs, et ses rameaux s'étaient déployés, grâce à l'abondance des eaux.
Choncho unatalika kwambiri kupambana mitengo yonse ya mʼmunda. Nthambi zake zinachuluka ndi kutalika kwambiri, chifukwa inkalandira madzi ambiri.
6 Tous les oiseaux du ciel faisaient leurs nids dans ses branches, et toutes les bêtes des champs mettaient bas sous son feuillage, une multitude de nations habitaient sous son ombre.
Mbalame zonse zamlengalenga zinkamanga zisa zake mʼnthambi za mtengowo. Nyama zakuthengo zonse zinkaswanirana mʼmunsi mwa nthambi zake. Mitundu yotchuka ya anthu inkakhala mu mthunzi wake.
7 Il était beau par sa grandeur et par la multitude de ses rameaux; car ses racines étaient arrosées d'une eau abondante.
Unali wokongola kwambiri, wa nthambi zake zotambalala, chifukwa mizu yake inazama pansi kumene kunali madzi ochuluka.
8 Tels sont les cyprès du paradis de Dieu; les pins ne peuvent lui être comparés pour leurs rejetons; les sapins ne peuvent lui être comparés pour leurs rameaux; nul autre arbre du paradis de Dieu ne lui ressemble en beauté,
Mʼmunda wa Mulungu munalibe mkungudza wofanana nawo, kapena mitengo ya payini ya nthambi zofanafana ndi nthambi zake. Munalibenso mtengo wa mkuyu nthambi zofanafana ndi zake. Mʼmunda wa Mulungu munalibe mtengo wina uliwonse wofanana ndi iwo kukongola kwake.
9 Pour la multitude de ses rameaux. Et les arbres du paradis de délices de Dieu lui portaient envie.
Ine ndinawupanga wokongola wa nthambi zochuluka. Mitengo yonse ya mu Edeni, mʼmunda wa Mulungu inawuchitira nsanje.
10 À cause de cela, voici ce que dit le Seigneur: En punition de ce que tu as tant grandi, de ce que tu as élevé ta cime au milieu des nuées, et que je l'ai vu se glorifier ainsi,
“‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Chifukwa kuti mtengowo unatalika kwambiri, unatulutsa songa zake mpaka ku thambo, ndipo unadzikweza chifukwa cha msinkhu wake,
11 Je l'ai livré aux mains du prince des nations, et il a préparé sa ruine.
ndinawupereka mʼdzanja la mfumu ya mitundu ya anthu kuti awulange molingana ndi kuyipa kwake.
12 Et des hommes de pestilence, des étrangers, venus des nation l'ont détruit, et ils l'ont abattu sur les montagnes; ses rameaux sont tombés dans tous les vallons; sa tige a été brisée dans toutes les plaines de la terre, et tous les peuples des nations se sont retirés de son ombre, et ils l'ont rasé au niveau du sol.
Anthu ankhanza kwambiri amitundu ya anthu achilendo adzawudula ndi kuwusiya. Nthambi zake zidzagwera pa mapiri ndi mu zigwa zonse. Nthambi zake zidzathyokera mʼmitsinje ya mʼdzikomo. Motero mitundu yonse ya anthu a dziko lapansi amene ankasangalala mu mthunzi wake idzawusiya.
13 Sur ses ruines se sont reposés tous les oiseaux du ciel, et toutes les bêtes des champs se sont blotties sous ses grosses branches;
Mbalame zonse zamlengalenga zidzakhala pa mtengo wakugwawo, ndipo nyama zakuthengo zonse zidzakhala pa nthambi zake.
14 Afin que nul des arbres qui croissent au bord des eaux ne se glorifiât de sa grandeur. Ils ont élevé leur cime au milieu des nues; mais ils ne se maintiendront pas en leur élévation; tous ces arbres, baignés des eaux, ont tous été donnés à la mort; ils iront tous au fond de la terre, au milieu des fils des hommes, avec ceux qui descendent à l'abîme.
Zidzakutero kuti pasakhalenso mitengo inanso ya mʼmbali mwa madzi yotalika kwambiri, imene idzatalike kwambiri ndi songa zake kufika mpaka ku mitambo. Komanso kuti pasadzakhalenso mitengo yolandira bwino madzi, imene idzatalika motero. Paja yonseyo kutha kwake ndi kufa, kupita ku dziko lapansi kukhala ndi anthu akufa amene analowa mʼmanda kale.
15 Et voici ce que dit le Seigneur Maître: Le jour où cet arbre est descendu aux enfers, l'abîme a pleuré sur lui. Et j'ai suspendu le cours de tous ses fleuves, et j'ai arrêté les grandes eaux qui l'arrosaient; et le Liban, à cause de lui, s'est couvert de ténèbres, et tous les arbres se sont affaissés de douleur. (Sheol )
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene mkungudzawo unatsikira ku manda, ndinawuza nyanja kuti iwulire maliro pakuwuphimba. Ndinawumitsa mitsinje ndipo madzi ambiri anaphwa. Ndinabweretsa mdima pa Lebanoni chifukwa cha mtengowo ndipo mitengo yonse ya mʼdzikomo inawuma. (Sheol )
16 Au bruit de sa chute, les nations ont tremblé; car je l'ai fait descendre aux enfers avec ceux qui étaient tombés dans l'abîme; et tous les arbres de délices de la terre le consolaient, et tous les beaux arbres du Liban arrosés par les eaux. (Sheol )
Mitundu ya anthu inagwedezeka pakumva mkokomo wa kugwa kwake, pamene ndinawutsitsira ku manda pamodzi ndi iwo amene anafa. Pamenepo ku dziko la akufa mitengo yonse ya ku Edeni pamodzi ndi ya ku Lebanoni yosankhidwa bwino inasangalatsidwa chifukwa cha zimenezi. (Sheol )
17 Et ceux-là aussi sont descendus avec lui aux enfers, parmi les morts frappés par le glaive; et sa race, qui demeurait sous son abri, a péri au milieu de sa vie. (Sheol )
Amene ankakhala mu mthunzi wake, amene ankayanjana nawo, iwonso anapita nawo pamodzi ku manda, kukakhala pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga pakati pa mitundu ya anthu. (Sheol )
18 À quoi te comparer? Descends; sois entraîné, avec tous les arbres de délices, au plus profond de la terre; tu seras étendu au milieu des incirconcis avec les morts frappés par le glaive. Tel sera le Pharaon, telle sera la multitude qui faisait sa force, dit le Seigneur Maître.
“‘Ndi mitengo iti ya mu Edeni imene ingafanane ndi kukongola kwako ndi ulemerero wako? Komabe iwenso, udzatsikira ku dziko la anthu akufa pamodzi ndi mitengo ya mu Edeni. Udzagona pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, anthu amene anaphedwa pa nkhondo. “‘Mtengowo ndi Farao ndi gulu lake lankhondo, akutero Ambuye Yehova.’”