< Ézéchiel 24 >

1 Et la parole du Seigneur vint à moi, en la neuvième année, le dixième mois, le dixième jour du mois, disant:
Pa tsiku lakhumi la mwezi wakhumi chaka chachisanu ndi chinayi, Yehova anandiyankhula kuti:
2 Fils de l'homme, à partir de ce jour où le roi de Babylone a fait tomber sa colère sur Jérusalem, à partir d'aujourd'hui, écris pour toi chaque jour;
“Iwe mwana wa munthu lemba dzina la tsiku lalero, lero lomwe lino, chifukwa mfumu ya Babuloni yazungulira Yerusalemu lero lino.
3 Et parle en parabole à cette maison qui m'irrite, et dis-lui: Ainsi parle le Seigneur: Mets sur le feu une chaudière et verses-y de l'eau;
Uwaphere mwambi anthu owukirawa ndi kuwawuza kuti: ‘Ambuye Yehova akuti, “‘Ikani mʼphika pa moto, ndipo mu mʼphikamo muthiremo madzi.
4 Et jettes-y des parts de victimes, des parts de choix, de la cuisse et de l'épaule réservées, la chair séparée des os,
Mu mʼphikamo muyikemo nthuli za nyama, nthuli zonse zabwino kwambiri za mwendo wathako ndi mwendo wamwamba. Mudzadzemo mafupa abwino kwambiri.
5 Et prises des bêtes choisies; et brûle les os sous les chairs. La chaudière a bouillonné, et les os ont cuit au milieu.
Pa gulu la nkhosa musankhepo nkhosa yabwino kwambiri. Muyike nkhuni pansi pa mʼphikawo. Madzi awire. Kenaka muphike nyamayo pamodzi ndi mafupa omwe.’
6 Voici donc ce que dit le Seigneur: Malheur à toi, ville de sang! tu es la chaudière où il y a de la rouille, et la rouille n'en est point partie; cette ville a offert des parts de victimes, et le sort n'est pas tombé sur elle.
“‘Nʼchifukwa chake, Ambuye Yehova akuti, “‘Tsoka kwa mzinda wokhetsa magazi, tsoka kwa mʼphika wadzimbiri; dzimbiri lake losachoka! Mutulutsemo nthuli imodzimodzi osasankhulapo.
7 Parce que son sang est au milieu d'elle, je l'ai posé sur une pierre lisse; je ne l'ai point répandu sur la terre où il aurait été caché,
“‘Paja magazi amene anakhetsa akanali pakati pake mu mzindamo. Iye awakhuthulira pa thanthwe losalala. Sanawakhutulire pa dothi kuopa kuti fumbi lingawafotsere.
8 Afin que ma colère éclate et châtie; j'ai mis le sang sur une pierre lisse, de peur qu'il ne soit caché.
Ndinasiya magaziwo pa mwala wosalala kuti asafotseredwe ndi fumbi chifukwa ndinafuna kuonetsa mkwiyo wanga ndi kulipsira.
9 À cause de cela, voici ce que dit le Seigneur: Et moi j'agrandirai le foyer.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: “‘Tsoka kwa mzinda wokhetsa magazi! Inenso, ndidzawunjika mulu waukulu wa nkhuni.
10 Et je prodiguerai le bois, et j'y mettrai le feu, afin que les chairs soient consumées, et que le jus se réduise,
Choncho wonjeza nkhuni ndipo muyatse moto. Phikani nyamayo bwinobwino, muthiremo zokometsera, mutsanule msuzi, ndipo mupsereze mafupawo.
11 Et que la chaudière pose sur les braises, que son airain s'échauffe et devienne brûlant, qu'il entre en fusion au milieu de son impureté, et que la rouille soit consumée.
Tsono muyike pa makala mʼphika wopanda kanthuwo mpaka utenthe kuchita kuti psuu kuti zonyansa zake zisungunuke ndi kuti dzimbiri lake lichoke.
12 Et la rouille qui abonde en elle ne sortira pas d'elle.
Koma mʼphikawo walephereka kuyeretsedwa. Dzimbiri lake linalowerera silingatheke kuchoka ngakhale ndi moto womwe.
13 Et sa rouille sera hideuse, en punition de ce que tu t'es souillée. Et pourquoi ne resterais-tu pas impure, jusqu'à ce que j'aie assouvi ma colère?
“‘Tsono dzimbiri limeneli ndi zilakolako za dama lako. Pakuti ine ndinayesa kukutsuka koma iwe sunayere, ndipo sudzayeranso mpaka ukali wanga utakwaniratu pa iwe.
14 C'est moi, le Seigneur, qui ai parlé, et le jour viendra où j'exécuterai, et je ne ferai pas de distinction, et je serai sans pitié. Selon tes voies et selon tes imaginations je te jugerai, dit le Seigneur. À cause de cela, je te jugerai selon le sang que tu as versé; je te jugerai selon les idoles que tu as adorées, toi impure, toi fameuse et féconde en moyens de m'irriter.
“‘Ine Yehova ndayankhula. Zimenezi zikubwera ndipo ndidzazichitadi. Sindidzabwerera mʼmbuyo. Sindidzakulekerera kapena kukuchitira chifundo. Ndidzakulanga molingana ndi makhalidwe ndi machitidwe ako, akutero Ambuye Yehova.’”
15 Et la parole du Seigneur me vint, disant:
Yehova anandiyankhula kuti:
16 Fils de l'homme, voilà que je vais te prendre par violence les délices de tes yeux; mais tu ne te lamenteras point, tu ne pleureras point.
“Iwe mwana wa munthu, Ine ndikulanda mwadzidzidzi mkazi amene amakukomera mʼmaso kwambiri. Koma usadandaule, usalire kapena kukhetsa misozi.
17 Tu auras un soupir de sang, une douleur de reins; tes cheveux sur la tête ne seront point tressés, et tes sandales ne seront point à tes pieds; nulle lèvre ne te consolera, et tu ne mangeras pas le pain des hommes.
Ubuwule koma mwakachetechete. Usamulire wakufayo. Uvale nduwira yako ndithu, nsapato zakonso usavule. Usaphimbe nkhope kapena kudya chakudya cha anamfedwa.”
18 Et je parlai au peuple le matin, comme le Seigneur me l'avait prescrit le soir; et je fis le matin même ce qui m'était commandé.
Choncho ndinayankhula ndi anthu mmawa, ndipo madzulo mkazi wanga anamwalira. Mmawa mwake ndinachita monga momwe anandilamulira.
19 Et le peuple me dit: Ne nous expliques-tu pas pourquoi tu agis ainsi?
Ndipo anthu anandifunsa kuti, “Kodi sutifotokozera tanthauzo la zimene ukuchitazi?”
20 Et je leur répondis: La parole du Seigneur m'est venue, disant:
Ndinawayankha kuti, “Yehova anandipatsa uthenga wakuti,
21 Dis à la maison d'Israël: Ainsi parle le Seigneur: Voilà que je vais profaner mon sanctuaire, l'orgueil de ta force, les délices de tes yeux, et pour lequel vous tremblez de toutes vos âmes. Vos fils et vos filles que vous aurez laissés périront par le glaive.
‘Awuze Aisraeli kuti: Ine Ambuye Yehova ndikuti: ndidzayipitsa Nyumba yanga yopatulika, nyumba imene mwakhala mukuyinyadira. Mumakondwa kwambiri poyiona, ndipo mumayikonda ndi mtima onse. Ana aamuna ndi aakazi amene munawasiya mʼmbuyo adzaphedwa ndi lupanga.
22 Et vous ferez comme je viens de faire: nulle bouche ne vous consolera, et vous ne mangerez pas le pain des hommes.
Ndipo mudzachita monga ndachitira inemu. Inu simudzaphimba nkhope zanu kapena kudya chakudya cha anamfedwa.
23 Et vos cheveux sur votre tête et vos sandales à vos pieds seront comme les miens; vous ne vous lamenterez point, vous ne pleurerez point, et vous vous consumerez en vos iniquités, et chacun de vous invoquera son frère.
Mudzavala nduwira zanu kumutu ndi nsapato zanu ku mapazi anu. Simudzabuma maliro kapena kukhetsa misozi koma mudzavutika kwambiri chifukwa cha machimo anu ndipo mudzabuwula pakati panu.
24 Et Ézéchiel sera pour vous un signe; vous ferez comme je viens de faire, lorsque ces choses arriveront; et vous saurez que je suis le Seigneur.
Ine Ezekieli ndidzakhala chitsanzo chanu. Mudzachita monga momwe ndachitira. Izi zikadzachitika, akutero Yehova, ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Wamphamvuzonse.’
25 Et toi, fils de l'homme, n'est-ce pas le jour où je leur prendrai ce qui fait leur force, le sujet de leur orgueil, les délices de leurs yeux, la joie de leur âme, leurs fils et leurs filles,
“Ndipo Yehova anandiyankhula nati: Iwe mwana wa munthu, tsiku lina ndidzawachotsera anthuwa linga lawo limene ankakondwerera kukongola kwake, limene linkawakomera mʼmaso mwawo, limenenso anayikapo mtima wawo kwambiri. Ndidzawachotsera ana awo aamuna ndi aakazi.
26 N'est-ce pas ce jour-là qu'un homme échappé à la mort viendra te trouver et te parler à l'oreille?
Pa tsiku limenelo wothawa nkhondo adzabwera kudzakuwuzani zimenezo.
27 Ce jour-là ta bouche s'ouvrira pour parler à cet homme sauvé; et tu ne seras pas muet plus longtemps, et tu seras pour eux un signe; et ils sauront que je suis le Seigneur.
Pa tsiku limenelo pakamwa pako padzatsekuka. Udzatha kuyankhula naye ndipo sudzakhalanso chete. Motero udzakhala chizindikiro kwa iwo, ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

< Ézéchiel 24 >