< Ézéchiel 23 >
1 Et la parole du Seigneur me vint, disant:
Yehova anandiyankhula nati:
2 Fils de l'homme, il y avait deux femmes, filles d'une seule mère.
“Iwe mwana wa munthu, panali atsikana awiri ana a mayi mmodzi.
3 Et dans leur jeunesse, elles se sont prostituées en Égypte; c'est là que leurs mamelles sont tombées et qu'elles ont été déflorées de leur virginité.
Iwo ankachita za chiwerewere ku Igupto. Za chiwerewerezo anayamba ali achichepere. Kumeneko anthu ankangowasisita pa chifuwa ndi kuwagwiragwira mawere awo aja.
4 Et elles s'appelaient: l'aînée Oola; sa sœur Ooliba. Et elles ont été à moi, et elles ont enfanté des fils et des filles, et voici leurs vrais noms: Samarie était Oola, et Jérusalem était Ooliba.
Wamkulu dzina lake anali Ohola, ndipo mngʼono wakeyo anali Oholiba. Ine ndinawakwatira ndipo anabereka ana aamuna ndi ana aakazi. Ohola ndiye Samariya, ndipo Yerusalemu ndiye Oholiba.
5 Et Oola me quitta pour se prostituer; elle aima jusqu'à la fureur ses amants les Assyriens, qui demeuraient auprès d'elle,
“Ohola anachita zachiwerewere ngakhale anali mkazi wanga; ndipo iye anakangamira abwenzi ake a ku Asiriya.
6 Vêtus d'hyacinthe, princes et capitaines, jeunes gens d'élite, tous cavaliers montant à cheval.
Amenewo anali asilikali ovala zibakuwa zamlangali, abwanamkubwa ndiponso atsogoleri a nkhondo. Onsewo anali anyamata osiririka ndipo ankakwera pa akavalo.
7 Et c'est à eux qu'elle se livra dans sa débauche, et tous les fils choisis des Assyriens, et tous ceux qu'elle aima si furieusement, la souillèrent au gré de tous leurs désirs.
Ohola anachita zachiwerewere ndi onsewa, anthu otchuka a ku Asiriya. Iye anadziyipitsa ndi mafano a munthu aliyense amene anagona naye.
8 Et elle ne renonça pas à sa débauche de l'Égypte; car c'est là que des hommes avaient dormi avec elle dans sa jeunesse, et ils l'avaient déflorée, et ils avaient versé sur elle leur propre infamie.
Iye sanaleke za chiwerewere zimene anaziphunzira ku Igupto. Paja akanali mtsikana anyamata ankagona naye. Iwo ankamusisita mawere akanali anthete nachita naye zachiwerewere.
9 À cause de cela, je l'ai livrée aux mains de ses amants, aux mains des fils des Assyriens qu'elle a aimés avec fureur.
“Nʼchifukwa chake Ine ndinamupereka kwa achikondi ake, Asiriya, amene iye ankawalakalaka.
10 Ils ont dévoilé sa honte; ils ont pris ses fils et ses filles; et ils l'ont tuée elle-même à coups de glaive. Et elle est devenue la fable des femmes, et ils ont tiré vengeance d'elle sur sa fille.
Iwowa anamuvula, namulanda ana ake aamuna ndi aakazi ndipo anamupha ndi lupanga. Ndipo atalangidwa choncho, iye anasanduka chinthu chonyozeka pakati pa akazi.
11 Et sa sœur Ooliba la vit; et en ses passions elle fut plus dépravée qu'elle, et en sa prostitution elle surpassa la prostitution de sa sœur.
“Mphwake Oholiba anaona zimenezi natengerako. Koma iye anachita zachiwerewere kuposa mkulu wake.
12 Elle aima avec fureur les fils des Assyriens, princes et capitaines, ses voisins, revêtus d'habits brodés, cavaliers montant à cheval, tous jeunes gens d'élite.
Iyenso anakangamira Asiriya, abwanamkubwa, olamulira asilikali, ankhondo ovala zovala zonse za nkhondo ndi okwera pa akavalo. Onsewa anali anyamata osiririka.
13 Et je les vis toutes deux marcher dans les mêmes souillures.
Ndinaona kuti iyenso anadziyipitsa; ndipo onse awiriwo anatsata njira imodzi.
14 Et Ooliba alla plus loin dans sa débauche; elle vit des hommes dessinés sur un mur, images de Chaldéens tracés au pinceau,
“Koma Oholiba uja anachita chigololo kopitirira mkulu wake. Iye anaona zithunzi za amuna pa khoma, zithunzi za Ababuloni zolembedwa ndi inki yofiira,
15 Les reins ceints d'étoffes bigarrées, la tête couverte d'étoffes de couleur, trois fois plus grands que les autres hommes, images de fils des Chaldéens, de la terre de leurs aïeux.
atamanga malamba mʼchiwuno mwawo ndi kuvala nduwira pa mitu yawo. Onse amaoneka ngati atsogoleri a magaleta a Ababuloni, mbadwa za ku Kaldeya.
16 Et les ayant contemplés de ses yeux, elle les aima avec fureur, et elle leur envoya des messagers en la terre des Chaldéens.
Oholiba atangowaona, anawalakalaka ndipo anatuma amithenga ku Kaldeya kukawayitana.
17 Et les fils de Babylone vinrent à elle; ils partagèrent sa couche; ils la souillèrent en sa prostitution, et elle fut souillée par eux; puis son âme s'éloigna d'eux.
Ndipo Ababuloni anabwera nʼkudzagona naye. Choncho mwa chilakolako chawo anamuyipitsa. Koma atamuyipitsa choncho, iye ananyansidwa nawo.
18 Et elle dévoila sa débauche, et elle dévoila sa honte. Et mon âme s'éloigna d'elle comme mon âme s'était éloignée de sa sœur.
Iye atachita chiwerewere chake poyera ndi kuonetsa umaliseche wake, Ine ndinamuchokera monyansidwa monga mmene ndinachitira ndi mʼbale wake.
19 Et tu as multiplié tes débauches, comme pour rappeler le souvenir des jours de ta jeunesse, où tu t'es prostituée en Égypte.
Koma anachitabe zachiwerewere osalekeza. Ankakumbukira masiku a ubwana wake pamene ankachita za chiwerewere mʼdziko la Igupto.
20 Et tu as aimé avec fureur les Chaldéens, qui avaient des chairs comme des ânes, et des membres comme des chevaux.
Kumeneko iye ankalakalaka zibwenzi zake, amene ziwalo zawo zinali ngati za abulu ndipo kutentha kwawo kunali ngati kwa akavalo.
21 Et tu as renouvelé le dérèglement de ta jeunesse, et ce que tu as fait durant ton séjour en Égypte quand tu avais les mamelles de ta jeunesse.
Motero, iwe Oholiba unafuna kuchitanso zadama monga unkachitira ku Igupto pamene unali mtsikana. Nthawi imene ija ankakusisita pa chifuwa ndi kugwiragwira mawere ako osagwa aja.
22 À cause de cela, Ooliba, voici ce que dit le Seigneur: Voilà que je vais susciter contre toi tes amants, de qui ton âme s'est éloignée; je les rassemblerai en cercle contre toi.
“Tsono iwe Oholiba, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakudzutsira zibwenzi zako zimene unkanyansidwa nazo zija kuti zilimbane nawe. Ndidzaziyitana kuti zibwere kuchokera mbali zonse.
23 Les fils de Babylone et tous les Chaldéens, Phacuc, et Sué, et Hychué, et avec eux tous les fils des Assyriens, jeunes gens d'élite, princes et capitaines, tous ayant grand air et grand renom, cavaliers montant à cheval.
Ndidzayitana anthu a ku Babuloni ndi Akaldeya onse, anthu a ku Pekodi, Sowa ndi Kowa pamodzi ndi Asiriya onse. Onsewa ndi amuna osiririka, abwanamkubwa, atsogoleri a ankhondo, oyenda pa magaleta, anthu a maudindo akuluakulu. Onsewa ndi okwera akavalo.
24 Et ils viendront tous contre toi du nord, chars et roues, avec une multitude de peuples, longs boucliers, écus légers; et ils poseront autour de toi des gardes.
Iwo adzabwera kudzalimbana nawe ndi zida za nkhondo, magaleta ndi ngolo, pamodzi ndi anthu ambiri. Adzakuzinga mbali zonse atavala zishango zankhondo ndi zipewa zankhondo. Ndidzakupereka kwa iwo kuti akulange ndipo adzakulanga monga momwe adzafunire.
25 Et je rendrai mon arrêt devant eux, et ils te puniront selon leurs lois. Et j'amènerai contre toi ma jalousie; et ils te traiteront avec des transports de colère. Ils te couperont les narines et les oreilles; ils frapperont du glaive ceux des tiens qui survivront; ils prendront tes fils et tes filles, et le feu dévorera ce qui restera de toi.
Ndidzaonetsa mkwiyo wanga pa iwe ndipo iwo adzakulanga iwe mwankhanza. Adzadula mphuno zanu ndi makutu anu, ndipo amene adzatsalira mwa iwe adzaphedwa ndi lupanga. Iwo adzakulanda ana ako aamuna ndi aakazi ndipo amene adzatsalira adzaphedwa ndi moto.
26 Et ils te dépouilleront de tes vêtements, et ils te prendront les joyaux qui faisaient ton orgueil.
Adzakuvulaninso zovala zanu ndikukulandani zodzikongoletsera zanu zamtengowapatali.
27 Puis je détournerai de toi tes impiétés, et tes débauches de la terre d'Égypte, et tu ne lèveras plus les yeux sur eux, et tu ne te souviendras plus de l'Égypte.
Motero ndidzathetsa zonyansa zako ndi zachigololo zomwe unaziyamba ku Igupto. Choncho sudzalakalaka za ku Igupto kapena kuzikumbukiranso.
28 Ainsi parle-encore le Seigneur Maître: Voilà que je te livre aux mains de ceux que tu hais, de ceux de qui ton âme s'est éloignée.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndikukupereka mʼmanja mwa amene amadana nawe, kwa iwo amene unawafulatira moyipidwa nawo.
29 Ils te traiteront avec haine, et ils te prendront le fruit de tes fatigues et de tes labeurs, et tu seras nue et confuse; et la honte de ta prostitution sera dévoilée; et ton impiété et ta débauche
Adzachita nawe mwachidani. Adzakulanda zonse zimene unagwirira ntchito. Adzakusiya wamaliseche ndiponso wausiwa. Kuyipa kwa makhalidwe ako achiwerewere kudzakhala pammbalambanda. Zonyansa zako ndi chiwerewere chako,
30 T'auront attiré ces maux, parce que tu t'es prostituée en courant après des gentils, et que tu t'es souillée avec leurs idoles.
zabweretsa izi pa iwe chifukwa unachita zonyansa ndi anthu a mitundu ndi kudziyipitsa ndi mafano awo.
31 Tu as marché dans la voie de ta sœur, et je mettrai sa coupe en tes mains.
Unatsata zochita za mkulu wako; choncho Ine ndidzayika chikho cha chilango chake mʼdzanja lako.
32 Voici ce que dit le Seigneur: Bois la coupe de ta sœur, coupe large et profonde; bois-la jusqu'à l'ivresse;
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Udzamwera chikho cha mkulu wako, chikho chachikulu ndi chakuya; anthu adzakuseka ndi kukunyoza, pakuti chikhocho ndi chodzaza kwambiri.
33 Et tu seras tout à fait énervée; la coupe de ta sœur Samarie est une coupe d'extermination.
Udzaledzera ndipo mtima wako udzadzaza ndi chisoni. Chimenechi ndi chikho chachiwonongeko ndi chipasupasu, chikho cha mkulu wako Samariya.
34 Bois-la, et je répudierai tes fêtes et tes jours de nouvelle lune; car c'est moi qui ai parlé, dit le Seigneur.
Udzamwa chikhocho mpaka kugugudiza. Tsono udzaphwanyaphwanya chikhocho ndipo udzangʼamba mawere ako ndi zigoba zake. Ine ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.
35 À cause de cela, voici ce que dit le Seigneur: Parce que tu m'as oublié et rejeté derrière toi, tu recevras la rétribution de ton impiété et de ta débauche.
“Chifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza wandiyiwala Ine ndi kundifulatira, chomwecho uyenera kulangidwa chifukwa cha zonyansa zako ndi chiwerewere chako.”
36 Et le Seigneur me dit: Fils de l'homme, ne jugeras-tu pas Oola et Ooliba? Ne leur feras-tu pas connaître leurs dérèglements,
Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza Ohola ndi Oholiba? Tsono uwayimbe mlandu chifukwa cha machitidwe awo onyansa.
37 Et leurs adultères, et le sang qu'elles ont versé? Elles se sont prostituées à leurs idoles; et leurs enfants qu'elles avaient enfantés pour moi, elles les ont fait passer pour elles à travers la flamme.
Iwo achita chigololo ndipo anapha anthu. Anachita chigololo popembedza mafano awo. Ngakhale ana amene anandiberekera Ine anawapereka kwa mafanowo ngati chakudya chawo.
38 Et aussi longtemps qu'elles ont ainsi fait, elles ont souillé mes choses saintes et profané mes sabbats.
Anachitanso izi: Iwo anayipitsa malo anga opatulika ndi kudetsa masabata anga.
39 Et quand elles égorgeaient leurs enfants pour des idoles, elles entraient dans mon sanctuaire pour le souiller; et voilà ce qu'elles ont fait au milieu de mon temple,
Atapereka ana awo kwa mafano, tsiku lomwelo anakalowanso mʼNyumba yanga yopatulika ndi kuyipitsamo. Izi ndi zimene anachita mʼNyumba mwanga.
40 Avec des hommes venant de loin, à qui elles avaient envoyé des messages. Et comme ils arrivaient tu t'es aussitôt lavée, tu t'es fardée autour des yeux, tu t'es parée de tes joyaux,
“Iwo anatuma amithenga kukayitana amuna a ku mayiko akutali. Anthuwo atabwera, abale awiri aja anasambasamba, kudzola utoto wodzikometsera kumaso, kenaka ndi kuvala zovala zamakaka.
41 Tu t'es assise sur un long siège, et une table était préparée devant toi; et ils se sont réjouis de mes parfums et de mon huile.
Anakhala pa bedi lokongola ndipo patsogolo pawo panali tebulo pamene munayikapo lubani ndi mafuta. Zonse zowapatsa Ine.
42 Et elles ont entonné des chants harmonieux devant quelques-uns des hommes qui étaient venus en foule du désert, et elles leur ont mis des bracelets, et elles leur ont posé sur la tête des couronnes de gloire.
“Mfuwu wa chigulu cha anthu unamveka. Anthu oledzera ochokera ku chipululu anabwera pamodzi ndi anthu wamba ndipo anaveka akaziwo zibangiri kumanja ndi zipewa zaufumu zokongola ku mutu.
43 Et j'ai dit: Ne commettent-elles pas des adultères avec ceux-ci? Cette femme ne se conduit-elle pas comme une prostituée?
Ndipo ine ndinati za mkazi wotheratu ndi chigololoyo, ‘Tsono asiyeni kuti achite naye monga wachiwerewere, pakuti ichi ndi chimene iye ali basi.’
44 Ils sont entrés chez elle comme on entre chez une femme débauchée; et voilà comme ils sont entrés chez Oola et Ooliba, pour s'abandonner au dérèglement.
Tsono anapita kwa iwo monga mmene anthu amapitira kwa mkazi wadama. Momwemo anapita kwa Ohola ndi kwa Oholiba kukachita nawo zadama.
45 Aussi ce sont des hommes justes, ceux qui tireront vengeance contre ces femmes, de leurs adultères et du sang versé; car elles sont adultères et elles ont versé le sang.
Koma anthu olungama adzawazenga anthuwa mlandu wa chigololo ndi wa kupha anthu. Ndi iwodi anthu achigololo ndiponso mʼmanja mwawo muli magazi.
46 Voici ce que dit le Seigneur Maître: Ameute contre elles la foule, et répands chez elles le trouble et le pillage.
“Ambuye Yehova akuti: Itanitsani chigulu cha anthu kuti chidzawalange ndi kulanda chuma chawo.
47 Qu'elles soient lapidées par les pierres de la multitude, qu'elles soient percées par ses glaives; on tuera leurs fils et leurs filles, on brûlera leurs maisons.
Anthuwo adzawaponye miyala akazi awiriwo ndi kuwatema ndi malupanga awo. Ana awo aamuna ndi aakazi adzawaphe ndi kutentha nyumba zawo.
48 Ensuite je détournerai de cette terre l'impiété, et toutes les femmes seront instruites, elles n'imiteront pas l'impiété de celles-ci.
“Motero Ine ndidzathetsa zachigololo mʼdzikomo, ndipo akazi onse adzatengapo phunziro kuti asadzachite zachigololo monga za iwowo.
49 Et votre iniquité retombera sur vous, et vous porterez la peine de vos idoles, et vous connaîtrez que je suis le Seigneur.
Ndidzawalanga chifukwa cha ntchito zawo za dama ndipo adzazunzika chifukwa cha tchimo lawo lopembedza mafano. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.”