< Ézéchiel 19 >

1 Et toi, chante une lamentation sur le prince d'Israël;
“Imba nyimbo ya madandawulo, kuyimbira akalonga a ku Israeli.
2 Et dis: Pourquoi ma mère est-elle devenue une jeune lionne au milieu des lions? Pourquoi, au milieu des lions, a-t-elle multiplié ses lionceaux?
Uzinena kuti, “‘Amayi ako anali ndani? Anali ngati mkango waukazi! Iwo unabwatama pakati pa mikango yayimuna; unkalera ana ake pakati pa misona.
3 Et un de ses lionceaux s'est élancé, et il est devenu lion, et il a appris à ravir sa proie, et il a dévoré des hommes.
Unalera mmodzi mwa ana ake, ndipo mwanayo anasanduka mkango wamphamvu. Unaphunzira kugwira nyama, ndipo unayamba kudya anthu.
4 Et les nations en ont ouï parler, et il a été pris comme il les détruisait, et elles l'ont emmené, dans un filet, en la terre d'Égypte.
Anthu amitundu anamva za mkangowo, ndipo tsiku lina unagwa mʼmbuna mwawo. Iwo anawukoka ndi ngowe kupita nawo ku dziko la Igupto.
5 Et la lionne, ayant vu qu'il était séparé d'elle, et que son espérance en lui avait péri, prit un autre de ses lionceaux, et le fit lion.
“‘Amayi aja ataona kuti mwana ankamukhulupirira uja wagwidwa ndi kuti chiyembekezo chake chapita padera, amayiwo anatenganso mwana wina namusandutsa mkango wamphamvu.
6 Et celui-ci se montra au milieu des lions, et il devint lion, et il apprit à ravir sa proie, et il dévora des hommes.
Unkayendayenda pakati pa mikango inzake, pakuti tsopano unali mkango wamphamvu. Unaphunzira kugwira nyama ndipo unayamba kudya anthu.
7 Et il se reput en son audace, et il dépeupla les villes de la voix de ses rugissements; et il désola la terre et ce qui la remplit.
Unagwetsa malinga awo, ndikuwononga mizinda yawo. Onse a mʼdzikomo anachita mantha chifukwa cha kubangula kwake.
8 Et les peuples des royaumes l'entourèrent, et ils tendirent contre lui leurs filets, et pendant qu'il les détruisait il fut pris.
Pamenepo mitundu ya anthu, makamaka ochokera madera ozungulira, inabwera kudzalimbana nawo. Anawutchera ukonde wawo, ndipo tsiku lina unagwera mʼmbuna mwawo.
9 Et on le mit dans une cage de fer, enveloppé de son filet; et il arriva chez le roi de Babylone, qui le jeta en prison, afin qu'on n'entendit plus sa voix sur la montagne d'Israël.
Anawukoka ndi ngowe nawuponya mʼchitatanga. Anabwera nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ndipo mfumuyo inawuponya mʼndende ndi cholinga choti liwu lake lisamamvekenso ku mapiri a Israeli.
10 Ta mère est comme une vigne et comme une fleur de grenadier planté au bord des eaux; son fruit et ses bourgeons ont crû dans l'abondance de l'eau.
“‘Amayi ako anali ngati mpesa mʼmunda wamphesa wodzalidwa mʼmbali mwa madzi. Unabereka bwino ndipo unali ndi nthambi zambiri chifukwa cha kuchuluka kwa madzi.
11 Mais elle est devenue une verge pour la tribu des rois, et elle s'est élevée dans sa grandeur, au milieu des autres tiges. Et elle a vu sa grandeur en la multitude de ses rameaux.
Nthambi zake zinali zolimba, zoyenera kupangira ndodo yaufumu. Unatalika nusomphoka pakati pa zomera zina. Unkaoneka bwino chifukwa cha kutalika kwake, ndi nthambi zake zambiri.
12 Et elle a été brisée avec fureur; elle a été jetée à terre, et un vent brillant a flétri ses meilleures branches; ils se sont vengés d'elle, et la verge de sa puissance a été desséchée. Le feu l'a dévorée.
Koma unazulidwa mwaukali ndipo unagwetsedwa pansi. Unawuma ndi mphepo ya kummawa, zipatso zake zinayoyoka; nthambi zake zolimba zinafota ndipo moto unapsereza mtengo wonse.
13 Et maintenant on l'a plantée dans le désert en une terre aride.
Ndipo tsopano anawuwokeranso ku chipululu, dziko lowuma ndi lopanda madzi.
14 Et une flamme est sortie d'une verge de ses meilleurs rameaux, et elle l'a dévorée, et elle n'eut plus la verge de sa puissance. Sa race est devenue une parabole de lamentation, une lamentation que l'on chantera.
Moto unatulukanso mu mtengomo ndi kupsereza nthambi ndi zipatso zake. Palibe nthambi yolimba inatsala pa mtengowo yoyenera kupangira ndodo yaufumu. Imeneyi ndi nyimbo yachisoni ndipo yasanduka nyimbo ya pa maliro.’”

< Ézéchiel 19 >