< Exode 26 >

1 Et tu feras le tabernacle avec dix courtines de fin lin retors, d’hyacinthe, de pourpre, d'écarlate retors, ouvrage varié, œuvre du tisserand.
“Panga chihema pogwiritsa ntchito nsalu khumi zofewa, zosalala ndi zolukidwa bwino, zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Ndipo anthu aluso apete pa nsaluzo Akerubi.
2 Chaque courtine aura -vingt-huit coudées de long, sur quatre de large; de même, mesure, seront toutes les courtines.
Nsalu zonse zikhale zofanana. Mulitali mwake zikhale mamita khumi ndi atatu, mulifupi mamita awiri.
3 Cinq courtines seront ajustées l'une tenant à l'autre, et les cinq autres courtines seront attachées l'une à l'autre.
Ulumikize nsalu zisanu kuti ikhale nsalu imodzi. Uchite chimodzimodzi ndi nsalu zisanu zinazo.
4 Tu feras des attaches d'hyacinthe sur la lisière de l'une des courtines, pour la nouer à la suivante; tu feras de même sur la lisière de la courtine opposée, pour la nouer à la première.
Panga zokolowekamo za nsalu yobiriwira mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsiriza ya mbali ina. Uchitenso chimodzimodzi ndi nsalu yotsiriza ya mbali inayo.
5 Tu feras cinquante attaches à chaque courtine, et tu feras cinquante attaches à la suivante, pour les réunir l'une à l'autre, les attaches se correspondant face à face exactement.
Upange zokolowekamo 50 pa nsalu yoyamba ndi zokolowekamo makumi asanu zinanso pa nsalu inayo. Upange motero kuti zokolowekamozo ziziyangʼanana.
6 Tu feras cinquante anneaux d'or et tu en joindras les courtines l'une à l'autre à l'aide des anneaux, et elles formeront un seul tabernacle.
Kenaka upange ngowe zagolide makumi asanu zolumikizira nsalu ziwirizo kuti zipange chihema chimodzi.
7 Tu feras aussi des couvertures en peaux velues pour abriter et envelopper le tabernacle, et tu en feras onze.
“Upange nsalu za ubweya wambuzi zophimba pamwamba pa chihemacho. Nsalu zonse pamodzi zikhale khumi ndi imodzi.
8 Elles auront trente coudées de long, sur quatre de large; de même mesure seront toutes les couvertures.
Nsalu zonse khumi ndi imodzi zikhale zofanana. Mulitali mwake mukhale mamita khumi ndi anayi ndipo mulifupi mwake mukhale mamita awiri.
9 Tu joindras cinq couvertures, et tu joindras les six autres couvertures, et tu replieras en deux la moitié de la sixième sur le devant du tabernacle.
Ulumikize nsalu zisanu kuti ikhale nsalu imodzi ndipo zina zisanu ndi imodzi uzilumikizenso kuti ikhale nsalu imodzinso. Nsalu yachisanu ndi chimodzi imene ili kutsogolo kwa tenti uyipinde pawiri.
10 Tu feras cinquante attaches sur la lisière de chaque couverture, pour les réunir ensemble; et tu feras cinquante attaches sur la lisière de la couverture suivante, pour l’adapter à la première.
Upange zokolowekamo 50 mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsirizira ya nsalu yoyamba yolumikiza ija. Upangenso zokolowekamo zina 50 mʼmphepete mwa nsalu yotsirizira ya nsalu inanso yolumikiza ija.
11 Tu feras cinquante anneaux d'airain, au moyen desquels tu réuniras les attaches, et tu joindras ainsi les couvertures qui n'en feront plus qu'une seule.
Kenaka upange ngowe 50 zamkuwa ndipo uzilowetse mu zokolowekazo. Ndiye uphatikize nsalu ziwirizo kuti tentiyo ikhale imodzi.
12 Et tu fixeras par le bas et par les deux extrémités l'excédant de longueur des couvertures du tabernacle; la moitié de couverture qui restera, tu la replieras, car il y aura excédant de couvertures du tabernacle, et tu en envelopperas le derrière du tabernacle.
Theka lotsalira la nsaluyo lidzalendewera kumbuyo kwa chihemacho.
13 Tu replieras l'excédant de longueur des couvertures du tabernacle, une coudée d'un côté et une coudée de l'autre, de telle sorte qu'il soit couvert.
Nsalu yotsalira ya masentimita 46 mulitali mwake mʼmbali zonse ziwiri idzalendewere kuphimba mbali ziwirizo.
14 Tu feras, pour le tabernacle, une toiture double, le dessous en toisons de béliers teintes en rouge; et par-dessus une couverture de peaux de béliers teintes en bleu.
Upange chikopa cha nkhosa zazimuna cha utoto wofiira chophimbira tentiyo ndipo pamwamba pake upangireponso chophimbira china cha zikopa za akatumbu.
15 Et tu feras les colonnes du tabernacle en bois incorruptible.
“Upange maferemu amatabwa amtengo wa mkesha oyimikira chihemacho.
16 Chaque colonne aura dix coudées de haut, sur une coudée et demie d'épaisseur.
Feremu iliyonse ikhale yotalika mamita anayi ndipo mulifupi mwake mukhale masentimita 69.
17 Il y aura à chaque colonne deux jointures correspondant l’un à l'autre; et il y en aura à toutes les colonnes du tabernacle.
Thabwa lililonse likhale ndi zolumikizira ziwiri. Upange maferemu onse a chihemacho ndi matabwa otere.
18 Il y aura vingt colonnes du côté du nord;
Upange maferemu makumi awiri a mbali yakummwera kwa chihemacho.
19 Puis, tu feras quarante bases d'argent pour les vingt colonnes; une colonne aura une base pour chacune de ses extrémités; une autre colonne une base pour chacune de ses extrémités.
Ndipo upange matsinde 40 asiliva ndipo uwayike pansi pa maferemuwo. Pansi pa feremu iliyonse pakhale matsinde awiri ogwiriziza zolumikizira ziwiri zija.
20 Et le second côté, celui du midi, aura vingt colonnes.
Ndipo mbali yakumpoto ya chihemacho upangenso maferemu makumi awiri.
21 Elles auront quarante ornements d'argent; une colonne aura, un ornement pour chacune de ses extrémités; une autre colonne un ornement pour chacune de ses extrémités.
Upangenso matsinde 40 asiliva, awiri pansi pa feremu iliyonse.
22 Et derrière le tabernacle, du côté de la mer (à l'occident), il y aura six colonnes.
Upange maferemu asanu ndi imodzi a kumbuyo kwa tenti, kumbali yakumadzulo.
23 Tu feras aussi deux colonnes sur les angles du tabernacle, derrière le tabernacle.
Ndipo upangenso maferemu awiri a pa ngodya yakumbuyo kwenikweni kwa tenti.
24 Elles seront semblables par la base, et semblables par les chapiteaux qui seront réunis. Ainsi tu feras pour les deux anges qui seront semblables.
Pa ngodya ziwirizi pakhale maferemu awiri, kuyambira pansi mpaka pamwamba ndipo alumikizidwe pa ngowe imodzi. Maferemu onse akhale ofanana.
25 Il y aura huit colonnes et seize bases d'argent; à chaque colonne une base, pour chacune de ses extrémités, et à une autre colonne une base, pour chacune de ses extrémités.
Choncho pakhale maferemu asanu ndi atatu ndiponso matsinde 16 asiliva, awiri akhale pansi pa feremu iliyonse.
26 Et tu feras des barres de bois incorruptible: cinq pour chaque colonne de l’un des côtés du tabernacle;
“Upange mitanda ya matabwa amtengo wa mkesha: mitanda isanu ikhale ya maferemu a mbali imodzi ya chihema,
27 Cinq barres par colonne de l’autre côté du tabernacle, et cinq barres par colonne des angles de derrière du tabernacle, du côté de la mer.
mitanda isanu inanso ikhale ya maferemu a mbali inayo. Pakhalenso mitanda ina isanu ya mbali yakumadzulo, kumapeto kwenikweni kwa chihema.
28 La barre du milieu, entre deux colonnes, ira de l'une à l'autre.
Mtanda wapakati pa maferemuwo uchokere pa maferemu a mbali ina mpaka mbali inanso.
29 Tu revêtiras d’or fin toutes les colonnes; et tu feras en or les anneaux dans lesquels tu engageras les barres, et tu revêtiras les barres d'or pur.
Maferemuwo uwakute ndi golide ndiponso upange mphete zagolide zogwiriziza mitandayo. Ndipo mitandayonso uyikute ndi golide.
30 Tu dresseras ainsi le tabernacle, selon le modèle qui t'en a été montré sur la montagne.
“Upange chihema mofanana ndi momwe ndinakuonetsera pa phiri paja.
31 Tu feras aussi un voile d'hyacinthe, de pourpre, d'écarlate filé, et de fin filé, et il sera tissu: œuvre variée.
“Upange nsalu yokhala ndi mtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira ndipo nsaluyo ikhale yolukidwa bwino, yofewa ndi yosalala. Ndipo anthu aluso apetepo zithunzi za Akerubi.
32 Et tu le placeras sur quatre colonnes incorruptibles, revêtues d'or pur, qui auront des chapiteaux d'or et quatre bases d'argent.
Nsaluyo uyikoloweke pa nsanamira zinayi zamtengo wa mkesha zokutidwa ndi golide zomwe zili ndi ngowe zagolide, zomwe zayima pa matsinde asiliva anayi.
33 Tu poseras le voile sur les colonnes, et tu introduiras, à l'intérieur du voile, l’arche du témoignage, et le voile séparera pour vous le saint du Saint des saints.
Ukoloweke kataniyo ku ngowe ndipo uyike Bokosi la Chipangano mʼkatimo. Kataniyo idzalekanitse malo wopatulika ndi malo wopatulika kwambiri.
34 Avec ce voile, tu cacheras l’arche du témoignage dans le Saint des saints.
Uyike chivundikiro pa bokosi laumboni ku malo wopatulika kwambiri.
35 Et tu placeras la table devant le voile, et le chandelier vis-à-vis la table, du côté du tabernacle qui regardera le midi; et la table sera au nord.
Uyike tebulo kunja kwa katani yotchinga cha kumpoto kwa chihema ndipo uyike choyikapo nyale chija kummwera moyangʼanana ndi tebulolo.
36 Tu feras en outre, à la porte du tabernacle, un voile d'hyacinthe, de pourpre, d'écarlate filé, et de lin filé; œuvre du brodeur.
“Pa chipata cholowera mu chihema, uyikepo nsalu yamtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira, yomwe ndi yofewa ndi yosalala, yopetedwa bwino ndi amisiri aluso.
37 Et tu feras, pour le voile, cinq colonnes que tu revêtiras d'or pur, et leurs chapiteaux seront d'or, et les cinq bases seront d'airain jeté en fonte.
Upange ngowe zagolide za nsaluyo ndi nsanamira zisanu zamtengo wa mkesha ndipo uzikute ndi golide. Upangenso matsinde asanu amkuwa a nsanamirazo.”

< Exode 26 >