< Esther 10 >

1 Et le roi écrivit ce qui concernait l'empire de la terre et de la mer;
Mfumu Ahasiwero anakhometsa msonkho mʼdziko lake lonse mpaka ku zilumba zonse.
2 Et sa puissance, et sa valeur, et ses richesses, et sa gloire, sont décrites dans le livre des rois des Perses et des Mèdes, comme un mémorial.
Ndipo ntchito zonse zochitika ndi mphamvu zake komanso ndi zonse zofotokoza za ukulu wa Mordekai, kukwezedwa kwake ndi mfumu, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Mediya ndi Peresiya?
3 Et Mardochée fut le lieutenant du roi Artaxerxès, et il fut grand dans le royaume, et il fut glorifié par les Juifs; et, aimé de tous, il exposa la suite de l'événement à tout son peuple.
Pakuti Mordekai Myuda uja anali wachiwiri wa mfumu Ahasiwero. Kwa Ayuda onse Mordekai anali munthu wamkulu ndipo ankamukonda chifukwa ankachitira zabwino mtundu wake ndi kufunira mtendere abale ake.

< Esther 10 >